< Masalimo 40 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mofatsa ndinadikira Yehova Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.
Potrpežljivo sem čakal na Gospoda in on se je nagnil k meni ter slišal moj klic.
2 Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko, mʼthope ndi mʼchithaphwi; Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.
Privedel me je tudi iz strašne jame, ven iz blatnega ila in moja stopala je postavil na skalo in utrdil moje korake.
3 Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga, nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga. Ambiri adzaona, nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.
V moja usta je položil novo pesem, celó hvalo našemu Bogu. Mnogi bodo to videli ter se bali in bodo zaupali v Gospoda.
4 Ndi wodala munthu amakhulupirira Yehova; amene sayembekezera kwa odzikuza, kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.
Blagoslovljen je tisti človek, ki svoje trdno upanje postavlja [v] Gospoda in ne spoštuje ponosnega niti takšnega, ki odvrača k lažem.
5 Zambiri, Yehova Mulungu wanga, ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita. Zinthu zimene munazikonzera ife palibe amene angathe kukuwerengerani. Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera, zidzakhala zambiri kuzifotokoza.
Mnoga, oh Gospod, moj Bog, so tvoja čudovita dela, ki si jih storil in tvoje misli, ki so do nas, ne morejo biti po vrsti izračunane k tebi. Če želim oznaniti in govoriti o njih, jih je več, kakor jih je mogoče prešteti.
6 Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna, koma makutu anga mwawatsekula; zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo Inu simunazipemphe.
Klavne daritve in darovanja si nisi zaželel, odprl si mi ušesa. Žgalne daritve in daritve za greh nisi zahteval.
7 Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera. Mʼbuku mwalembedwa za ine.
Potem sem rekel: »Glej! Prihajam. V zvezku knjige je zapisano o meni,
8 Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga; lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”
veselim se, da izpolnim tvojo voljo, oh moj Bog. Da, tvoja postava je znotraj mojega srca.
9 Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu; sinditseka milomo yanga monga mukudziwa Inu Yehova.
Oznanjal sem pravičnost v veliki skupnosti. Glej, svojih ustnic nisem zadrževal, oh Gospod, ti veš.
10 Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga; ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu. Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu pa msonkhano waukulu.
Tvoje pravičnosti nisem skrival v svojem srcu; oznanjal sem tvojo zvestobo in tvojo rešitev duše. Tvoje ljubeče skrbnosti in tvoje resnice nisem prikrival pred veliko skupnostjo.
11 Musandichotsere chifundo chanu Yehova; chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.
Svojih nežnih usmiljenj ne zadržuj pred menoj, oh Gospod. Naj me nenehno varujeta tvoja ljubeča skrbnost in tvoja resnica.
12 Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira; machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona. Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga, ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.
Kajti obkrožila so me brezštevilna zla, polastile so se me moje krivičnosti, tako da nisem zmožen pogledati kvišku. Več jih je kakor las moje glave, zato mi peša srce.
13 Pulumutseni Yehova; Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.
Bodi vesel, oh Gospod, da me osvobodiš. Oh Gospod, podvizaj se, da mi pomagaš.
14 Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene amakhumba chiwonongeko changa abwezedwe mwamanyazi.
Naj bodo hkrati osramočeni in zbegani, ki strežejo po moji duši, da jo uničijo. Naj bodo odgnani nazaj in osramočeni tisti, ki mi želijo zlo.
15 Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!” abwerere akuchita manyazi.
Naj bodo zapuščeni, za nagrado njihove sramote, ki mi pravijo: ›Aha, aha.‹
16 Koma iwo amene amafunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”
Naj se vsi tisti, ki te iščejo, razveselijo in bodo veseli v tebi. Naj tisti, ki ljubijo tvojo rešitev duše, nenehno govorijo: ›Poveličan bodi, Gospod.‹
17 Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa; Ambuye andiganizire. Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga; Inu Mulungu wanga, musachedwe.
Toda jaz sem ubog in pomoči potreben, vendarle Gospod misli name. Ti si moja pomoč in moj osvoboditelj; ne mudi se, oh moj Bog.«

< Masalimo 40 >