< Masalimo 40 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mofatsa ndinadikira Yehova Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.
JUNANGGA nu y siningon as Jeova; ya janaegueng maesa güe guiya guajo, ya jajungog y inagangjo.
2 Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko, mʼthope ndi mʼchithaphwi; Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.
Ya güiya chumule yo guinin un joyo chatliion, guinin fache na tadong: ya japolo y adengjo gui jilo acho, ya janafitme y jinanaojo.
3 Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga, nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga. Ambiri adzaona, nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.
Ya japolo gui pachotto canta na mannuebo, junggan, y alabansa gui Yuusta. Megae lumie ya manmaañao, ya ufanangoco as Jeova.
4 Ndi wodala munthu amakhulupirira Yehova; amene sayembekezera kwa odzikuza, kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.
Dichoso y taotao ni jaangoco gui as Jeova: ya ti jaaatan y mansobetbio ni y manabag manmalag y mandague.
5 Zambiri, Yehova Mulungu wanga, ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita. Zinthu zimene munazikonzera ife palibe amene angathe kukuwerengerani. Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera, zidzakhala zambiri kuzifotokoza.
Megae O Jeova, y ninamanmanmo ni unfatinas: yan y jinasomo para jame; ti siña maaregla sija gui menamo: yaguin guajo judeclara ya jusangang sija, tisiña matufong sa gosmegae.
6 Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna, koma makutu anga mwawatsekula; zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo Inu simunazipemphe.
Y inefresen ninae ti yamo: y talangajo jagasja unbaba: inefresen sinenggue ya y ninae pot y isao, ti jagasja ungagao.
7 Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera. Mʼbuku mwalembedwa za ine.
Ayo nae ileco: Estagüe na matoyo: gui finalulon y leblo nae esta matugue pot guajo.
8 Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga; lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”
Yajo para jufatinas y minalagomo, O Yuusso: magajet na y laymo gaegue gui jalom corasonjo.
9 Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu; sinditseka milomo yanga monga mukudziwa Inu Yehova.
Guajo jagas jusangan y tininas gui jalom y dangculo na inetnon taotao: estagüe, na ti junaquiequeto y labiosso, O Jeova, jago tumungo.
10 Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga; ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu. Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu pa msonkhano waukulu.
Ti junaatog y tininasmo gui jalom corasonjo; y minagajetmo yan satbasionmo jagas jusangan: ti jupune y minaasemo yan y minaulegmo gui dangculon inetnon taotao.
11 Musandichotsere chifundo chanu Yehova; chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.
Jago, O Jeova, chamo dumitietietene y minaasemo para guajo: sa y minaasemo yan y minagajetmo juadadaje yo para taejinecog.
12 Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira; machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona. Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga, ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.
Sa gaegue gui oriyajo y tinaelaye asta ti tufungon: jajiguef yo y tinaelayeco sija, ya ti siña juatan julo; megaeña mas que y gapotulo gui ilujo, ya y corasonjo yafae esta.
13 Pulumutseni Yehova; Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.
Malagojao, O Jeova, unnalibreyo: O Jeova, laguse para unayudayo.
14 Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene amakhumba chiwonongeko changa abwezedwe mwamanyazi.
Polo ya ufanmamajlao ya ufaninestotba ayo y umaliligao y antijo para uyulang: polo ya ufanalo tate ya ufanmamajlao, ni y yañija y munataelaye yo.
15 Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!” abwerere akuchita manyazi.
Polo ya ufanlapoble sija, pot y minamajlaoñija, ni y umaalog ni guajo: Ja, ja.
16 Koma iwo amene amafunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”
Polo ya ufanmagof ya ufansemagof ni jago, todo y umaliligao jao: ya polo ya siesiempreja ujaalog, y gumaeya y satbasionmo: Ladangculo Jeova.
17 Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa; Ambuye andiganizire. Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga; Inu Mulungu wanga, musachedwe.
Ya guajo pobleyo ya nesesitaoyo; lao si Jeova jajajasoyo. Jago y umayuyudayo yan y munalibre yo: O Yuusso, chamo atrasasao.

< Masalimo 40 >