< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
[Álefe]: Bem-aventurados são os puros em [seus] caminhos, os que andam na lei do SENHOR.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Bem-aventurados são os que guardam os testemunhos dele, [e] o buscam com todo o coração;
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
E não praticam perversidade, [mas] andam nos caminhos dele.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Tu mandaste que teus mandamentos fossem cuidadosamente obedecidos.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Ah! Como gostaria que meus caminhos fossem dirigidos a guardar teus estatutos!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Então não me envergonharia, quando eu observasse todos os teus mandamentos.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Louvarei a ti com um coração correto, enquanto aprendo os juízos de tua justiça.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Eu guardarei teus estatutos; não me abandones por completo.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
[Bete]: Com que um rapaz purificará o seu caminho? Sendo obediente conforme a tua palavra.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Eu te busco como todo o meu coração; não me deixes desviar de teus mandamentos.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Guardei a tua palavra em meu coração, para eu não pecar contra ti.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Bendito [és] tu, SENHOR; ensina-me os teus estatutos.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Com meus lábios contei todos os juízos de tua boca.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Eu me alegro mais com o caminho de teus estatutos, do que com todas as riquezas.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Meditarei em teus mandamentos, e darei atenção aos teus caminhos.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Terei prazer em teus estatutos; não me esquecerei de tua palavra.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
[Guímel]: Trata bem o teu servo, [para] que eu viva, e obedeça tua palavra.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Abre meus olhos, para que eu veja as maravilhas de tua lei.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Eu sou peregrino na terra, não escondas de mim os teus mandamentos.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Minha alma está despedaçada de tanto desejar os teus juízos em todo tempo.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Tu repreendes aos malditos arrogantes, que se desviam de teus mandamentos.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Tira-me de minha humilhação e desprezo, pois eu guardei teus testemunhos.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Até mesmo os príncipes se sentaram, e falaram contra mim; porém o teu servo estava meditando em teus estatutos.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Pois teus testemunhos são meus prazeres [e] meus conselheiros.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
[Dálete]: Minha alma está grudada ao pó; vivifica-me conforme tua palavra.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Eu [te] contei os meus caminhos, e tu me respondeste; ensina-me conforme teus estatutos.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Faze-me entender o caminho de teus preceitos, para eu falar de tuas maravilhas.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Minha alma se derrama de tristeza; levanta-me conforme tua palavra.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Desvia de mim o caminho de falsidade; e sê piedoso dando-me tua lei.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Eu escolhi o caminho da fidelidade; e pus [diante de mim] os teus juízos.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Estou apegado a teus testemunhos; ó SENHOR, não me envergonhes.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Correrei pelo caminho de teus mandamentos, porque tu alargaste o meu coração.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
[Hê]: Ensina-me, SENHOR, o caminho de teus estatutos, e eu o guardarei até o fim.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Dá-me entendimento, e eu guardarei a tua lei, e a obedecerei de todo [o meu] coração.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Faze-me andar na trilha de teus mandamentos, porque nela tenho prazer.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Inclina meu coração a teus testemunhos, e não à ganância.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Desvia meus olhos para que não olhem para coisas inúteis; vivifica-me pelo teu caminho.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Confirma tua promessa a teu servo, que tem temor a ti.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Desvia de mim a humilhação que eu tenho medo, pois teus juízos são bons.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Eis que amo os teus mandamentos; vivifica-me por tua justiça.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
[Vau]: E venham sobre mim tuas bondades, SENHOR; [e também] a tua salvação, segundo tua promessa.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Para que eu tenha resposta ao que me insulta; pois eu confio em tua palavra.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
E nunca tires de minha boca a palavra da verdade, pois eu espero em teus juízos.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Assim obedecerei a tua lei continuamente, para todo o sempre.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
E andarei [livremente] por longas distâncias, pois busquei teus preceitos.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Também falarei de teus testemunhos perante reis, e não me envergonharei.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
E terei prazer em teus mandamentos, que eu amo.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
E levantarei as minhas mãos a teus mandamentos, que eu amo; e meditarei em teus estatutos.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
[Záin]: Lembra-te da palavra [dada] a teu servo, à qual mantenho esperança.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Isto é meu consolo na minha aflição, porque tua promessa me vivifica.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Os arrogantes têm zombado de mim demasiadamente; [porém] não me desviei de tua lei.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Eu me lembrei de teus juízos muito antigos, SENHOR; e [assim] me consolei.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Eu me enchi de ira por causa dos perversos, que abandonam tua lei.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Teus estatutos foram meus cânticos no lugar de minhas peregrinações.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
De noite tenho me lembrado de teu nome, SENHOR; e tenho guardado tua lei.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Isto eu tenho feito, porque guardo teus mandamentos.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
[Hete]: O SENHOR é minha porção; eu disse que guardaria tuas palavras.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Busquei a tua face com todo o [meu] coração; tem piedade de mim segundo tua palavra.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Eu dei atenção a meus caminhos, e dirigi meus pés a teus testemunhos.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Eu me apressei, e não demorei a guardar os teus mandamentos.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Bandos de perversos me roubaram; [porém] não me esqueci de tua lei.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
No meio da noite eu me levanto para te louvar, por causa dos juízos de tua justiça.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Sou companheiro de todos os que te temem, e dos que guardam os teus mandamentos.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
A terra está cheia de tua bondade, SENHOR; ensina-me os teus estatutos.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
[Tete]: Tu fizeste bem a teu servo, SENHOR, conforme tua palavra.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Ensina-me bom senso e conhecimento, pois tenho crido em teus mandamentos.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Antes de ter sido afligido, eu andava errado; mas agora guardo tua palavra.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Tu és bom, e fazes o bem; ensina-me os teus estatutos.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Os arrogantes forjaram mentiras contra mim; [mas] eu com todo o [meu] coração guardo os teus mandamentos.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
O coração deles se incha como gordura; [mas] eu tenho prazer em tua lei.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Foi bom pra mim ter sido afligido, para assim eu aprender os teus estatutos.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Melhor para mim é a lei de tua boca, do que milhares de [peças] de ouro ou prata.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
[Iode]: Tuas mãos me fizeram e me formaram; faze-me ter entendimento, para que eu aprenda teus mandamentos.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Os que te temem olham para mim e se alegram, porque eu mantive esperança em tua palavra.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Eu sei, SENHOR, que teus juízos são justos; e que tu me afligiste [por] tua fidelidade.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Seja agora tua bondade para me consolar, segundo a promessa [que fizeste] a teu servo.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Venham tuas misericórdias sobre mim, para que eu viva; pois tua lei é o meu prazer.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Sejam envergonhados os arrogantes, porque eles me prejudicaram com mentiras; [porém] eu medito em teus mandamentos.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Virem-se a mim os que te temem e conhecem os teus testemunhos.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Seja meu coração correto em teus estatutos, para eu não ser envergonhado.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
[Cafe]: Minha alma desfalece por tua salvação; em tua palavra mantenho esperança.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Meus olhos desfaleceram por tua promessa, enquanto eu dizia: Quando tu me consolarás?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Porque fiquei como um odre na fumaça, [porém] não me esqueci teus testemunhos.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Quantos serão os dias de teu servo? Quando farás julgamento aos meus perseguidores?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Os arrogantes me cavaram covas, aqueles que não são conforme a tua lei.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Todos os teus mandamentos são verdade; com mentiras me perseguem; ajuda-me.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Estou quase que destruído por completo sobre a terra; porém eu não deixei teus mandamentos.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Vivifica-me conforme tua bondade, então guardarei o testemunho de tua boca.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
[Lâmede]: Para sempre, SENHOR, tua palavra permanece nos céus.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Tua fidelidade [dura] de geração em geração; tu firmaste a terra, e [assim] ela permanece.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Elas continuam por tuas ordens até hoje, porque todos são teus servos.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Se a tua lei não fosse meu prazer, eu já teria perecido em minha aflição.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Nunca esquecerei de teus mandamentos, porque tu me vivificaste por eles.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Eu sou teu, salva-me, porque busquei teus preceitos.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Os perversos me esperaram, para me destruírem; [porém] eu dou atenção a teus testemunhos.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
A toda perfeição eu vi fim; [mas] teu mandamento é extremamente grande.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
[Mem]: Ah, como eu amo a tua lei! O dia todo eu medito nela.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Ela me faz mais sábio do que meus inimigos [por meio de] teus mandamentos, porque ela está sempre comigo.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Sou mais inteligente que todos os meus instrutores, porque medito em teus testemunhos.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Sou mais prudente que os anciãos, porque guardei teus mandamentos.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Afastei meus pés de todo mau caminho, para guardar tua palavra.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Não me desviei de teus juízos, porque tu me ensinaste.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Como são doces tuas palavras ao meu paladar! Mais que o mel em minha boca.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Obtenho conhecimento por meio de teus preceitos; por isso odeio todo caminho de mentira.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
[Nun]: Tua palavra é lâmpada para meus pés e luz para meu caminho.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Eu jurei, e [assim] cumprirei, de guardar os juízos de tua justiça.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Eu estou muito aflito, SENHOR; vivifica-me conforme a tua palavra.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Agrada-te das ofertas voluntárias de minha boca, SENHOR; e ensina-me teus juízos.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Continuamente arrisco minha alma, porém não me esqueço de tua lei.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Os perversos me armaram um laço de armadilha, mas não me desviei de teus mandamentos.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Tomei teus testemunhos por herança para sempre, pois eles são a alegria de meu coração.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Inclinei meu coração para praticar os teus testemunhos para todo o sempre.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
[Sâmeque]: Odeio os inconstantes, mas amo a tua lei.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Tu és meu refúgio e meu escudo; eu espero em tua palavra.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Afastai-vos de mim, malfeitores, para que eu guarde os mandamentos de meu Deus.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Sustenta-me conforme a tua promessa, para que eu viva; e não me faças ser humilhado em minha esperança.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Segura-me, e estarei protegido; então continuamente pensarei em teus estatutos.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Tu atropelas a todos que se desviam de teus estatutos; pois o engano deles é mentira.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Tu tiras a todos os perversos da terra como [se fossem] lixo; por isso eu amo teus testemunhos.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Meu corpo se arrepia de medo de ti; e temo os teus juízos.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
[Áin]: Eu fiz juízo e justiça; não me abandones com os meus opressores.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Sê tu a garantia do bem de teu servo; não me deixes ser oprimido pelos arrogantes.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Meus olhos desfaleceram [de esperar] por tua salvação, e pela palavra de tua justiça.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Age para com teu servo segundo tua bondade, e ensina-me teus estatutos.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Eu sou teu servo. Dá-me entendimento; então conhecerei teus testemunhos.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
É tempo do SENHOR agir, porque estão violando tua lei.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Por isso eu amo teus mandamentos mais que o ouro, o mais fino ouro.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Por isso considero corretos todos os [teus] mandamentos quanto a tudo, e odeio todo caminho de falsidade.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
[Pê]: Maravilhosos são teus testemunhos, por isso minha alma os guarda.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
A entrada de tuas palavras dá luz, dando entendimento aos simples.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Abri minha boca, e respirei; porque desejei teus mandamentos.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Olha-me, e tem piedade de mim; conforme [teu] costume para com os que amam o teu nome.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Firma meus passos em tua palavra, e que nenhuma perversidade me domine.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Resgata-me da opressão dos homens; então guardarei teus mandamentos.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Brilha teu rosto sobre teu servo, e ensina-me teus estatutos.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Ribeiros d'água descem de meus olhos, porque eles não guardam tua lei.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
[Tsadê]: Tu és justo, SENHOR; e corretos são teus juízos.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Tu ensinaste teus testemunhos justos e muito fiéis.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Meu zelo me consumiu, porque meus adversários se esqueceram de tuas palavras.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Refinada é a tua palavra, e teu servo a ama.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Eu sou pequeno e desprezado; [porém] não me esqueço de teus mandamentos.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Tua justiça é justa para sempre, e tua lei é verdade.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Aperto e angústia me encontraram; [ainda assim] teus mandamentos são meus prazeres.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
A justiça de teus testemunhos [dura] para sempre; dá-me entendimento, e então viverei.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
[Cofe]: Clamei com todo o [meu] coração; responde-me, SENHOR; guardarei teus estatutos.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Clamei a ti; salva-me, e então guardarei os teus testemunhos.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Eu me antecedi ao amanhecer, e gritei; [e] mantive esperança em tua palavra.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Meus olhos antecederam as vigílias da noite, para meditar em tua palavra.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Ouve minha voz, segundo tua bondade, SENHOR; vivifica-me conforme teu juízo.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Aproximam-se [de mim] os que praticam maldade; eles estão longe de tua lei.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
[Porém] tu, SENHOR, estás perto [de mim]; e todos os teus mandamentos são verdade.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Desde antigamente eu soube de teus testemunhos, que tu os fundaste para sempre.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
[Rexe]: Olha a minha aflição, e livra-me [dela]; pois não me esqueci de tua lei.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Defende minha causa, e resgata-me; vivifica-me conforme tua palavra.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
A salvação está longe dos perversos, porque eles não buscam teus estatutos.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Muitas são tuas misericórdias, SENHOR; vivifica-me conforme teus juízos.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Muitos são meus perseguidores e meus adversários; [porém] eu não me desvio de teus testemunhos.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Eu vi aos enganadores e os detestei, porque eles não guardam tua palavra.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Vê, SENHOR, que eu amo teus mandamentos; vivifica-me conforme a tua bondade.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
O princípio de tua palavra é fiel, e o juízo de tua justiça [dura] para sempre.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
[Xin]: Príncipes me perseguiram sem causa, mas meu coração temeu a tua palavra.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Eu me alegro em tua palavra, tal como alguém que encontra um grande tesouro.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Odeio e abomino a falsidade; [mas] amo a tua lei.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Louvo a ti sete vezes ao dia, por causa dos juízos de tua justiça.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Muita paz têm aqueles que amam a tua lei; e para eles não há tropeço.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Espero por tua salvação, SENHOR; e pratico teus mandamentos.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Minha alma guarda teus testemunhos, e eu os amo muito.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Eu guardo teus preceitos e teus testemunhos, porque todos os meus caminhos estão diante de ti.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
[Tau]: Chegue meu clamor perante teu rosto, SENHOR; dá-me entendimento conforme tua palavra.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Venha minha súplica diante de ti; livra-me conforme tua promessa.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Meus lábios falarão muitos louvores, pois tu me ensinas teus estatutos.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Minha língua falará de tua palavra, porque todos os teus mandamentos são justiça.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Que tua mão me socorra, porque escolhi [seguir] teus preceitos.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Desejo tua salvação, SENHOR; e tua lei é o meu prazer.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Que minha alma viva e louve a ti; e que teus juízos me socorram.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Tenho andado sem rumo, como uma ovelha perdida; busca a teu servo, pois eu não me esqueci de teus mandamentos.

< Masalimo 119 >