< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova. 2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse. 3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake. 4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu. 5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu! 6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse. 7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama. 8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu. 9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu. 10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu. 11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni. 12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu. 13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu. 14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri. 15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu. 16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu. 17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu. 18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu. 19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu. 20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse. 21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu. 22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu. 23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu. 24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza. 25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu. 26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu. 27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu. 28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu. 29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu. 30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga. 31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi. 32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga. 33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto. 34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse. 35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa. 36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma. 37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu. 38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe. 39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino. 40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu. 41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu; 42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu. 43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu. 44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi. 45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu. 46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi, 47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda. 48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu. 49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo. 50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga. 51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu. 52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo. 53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu. 54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako. 55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu. 56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu. 57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu. 58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu. 59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu. 60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu. 61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu. 62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama. 63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu. 64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu. 65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu. 66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu. 67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu. 68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu. 69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse. 70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu. 71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu. 72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide. 73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu. 74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu. 75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu. 76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu. 77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa. 78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu. 79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu. 80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi. 81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu. 82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?” 83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu. 84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza? 85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu. 86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa. 87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu. 88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu. 89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako. 90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe. 91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu. 92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga. 93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga. 94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu. 95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu. 96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse. 97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse. 98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse. 99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu. 100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu. 101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu. 102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa. 103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga! 104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa. 105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga. 106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama. 107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu. 108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu. 109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu. 110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu. 111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga. 112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni. 113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu. 114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu. 115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga! 116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe. 117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu. 118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu. 119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu. 120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu. 121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza. 122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze. 123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama. 124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu. 125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu. 126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa. 127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino, 128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa. 129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera. 130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa. 131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu. 132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu. 133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira. 134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu. 135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu. 136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu. 137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino. 138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu. 139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu. 140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda. 141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu. 142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona. 143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu. 144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo. 145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu. 146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu. 147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu. 148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu. 149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu. 150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu. 151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona. 152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya. 153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu. 154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu. 155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu. 156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu. 157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu. 158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu. 159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika. 160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya. 161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu. 162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri. 163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu. 164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama. 165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse 166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu. 167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri. 168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu. 169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu. 170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu. 171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu. 172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama. 173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu. 174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu. 175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize. 176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.

< Masalimo 119 >