< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Bemaventurados os rectos em seus caminhos, que andam na lei do Senhor.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Bemaventurados os que guardam os seus testemunhos, e que o buscam com todo o coração,
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
E não obram iniquidade: andam nos seus caminhos.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Tu ordenaste os teus mandamentos, para que diligentemente os observassemos.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Oxalá que os meus caminhos fossem dirigidos a observar os teus estatutos.
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Então não serei envergonhado, quando tiver respeito a todos os teus mandamentos.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Louvar-te-hei com rectidão de coração, quando tiver aprendido os teus justos juizos.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Observarei os teus estatutos: não me desampares totalmente.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Com que purificará o mancebo o seu caminho? observando-o conforme a tua palavra.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Com todo o meu coração te busquei: não me deixes desviar dos meus mandamentos.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
A tua palavra tenho eu escondido no meu coração, para não peccar contra ti
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Bemdito és tu, ó Senhor; ensina-me os teus estatutos.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Com os meus labios declarei todos os juizos da tua bocca.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Folguei tanto no caminho dos teus testemunhos, como em todas as riquezas.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Meditarei nos teus preceitos, e terei respeito aos teus caminhos.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Recrear-me-hei nos teus estatutos: não me esquecerei da tua palavra.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Faze bem ao teu servo, para que viva e observe a tua palavra.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Abre tu os meus olhos, para que veja as maravilhas da tua lei.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Sou peregrino na terra: não escondas de mim os teus mandamentos.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
A minha alma está quebrantada de desejar os teus juizos em todo o tempo.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Tu reprehendeste asperamente os soberbos que são amaldiçoados, que se desviam dos teus mandamentos.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Tira de sobre mim o opprobrio e o desprezo, pois guardei os teus testemunhos.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Principes tambem se assentaram, e fallaram contra mim, mas o teu servo meditou nos teus estatutos.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Tambem os teus testemunhos são o meu prazer e os meus conselheiros.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
A minha alma está pegada ao pó: vivifica-me segundo a tua palavra.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Eu te contei os meus caminhos, e tu me ouviste: ensina-me os teus estatutos.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Faze-me entender os caminhos dos teus preceitos: assim fallarei das tuas maravilhas.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
A minha alma se derrete de tristeza: fortalece-me segundo a tua palavra.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Desvia de mim o caminho da falsidade, e concede-me piedosamente a tua lei.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Tenho escolhido o caminho da verdade: os teus juizos tenho posto diante de mim.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Tenho-me apegado aos teus testemunhos: ó Senhor, não me confundas.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Percorrerei o caminho dos teus mandamentos, quando dilatares o meu coração.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Ensina-me, ó Senhor, o caminho dos teus estatutos, e guardal-o-hei até ao fim.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Dá-me entendimento, e guardarei a tua lei, e observal-a-hei de todo o meu coração.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Faze-me andar na vereda dos teus mandamentos, porque n'ella tenho prazer.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Inclina o meu coração aos teus testemunhos, e não á cubiça.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Desvia os meus olhos de contemplarem a vaidade, e vivifica-me no teu caminho.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Confirma a tua palavra ao teu servo, que é dedicado ao teu temor.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Desvia de mim o opprobrio que temo, pois os teus juizos são bons.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Eis que tenho desejado os teus preceitos; vivifica-me na tua justiça.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Venham sobre mim tambem as tuas misericordias, ó Senhor, e a tua salvação segundo a tua palavra.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Assim terei que responder ao que me affronta, pois confio na tua palavra.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
E não tires totalmente a palavra de verdade da minha bocca, pois tenho esperado nos teus juizos.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Assim observarei de continuo a tua lei para sempre e eternamente.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
E andarei em liberdade; pois busco os teus preceitos.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Tambem fallarei dos teus testemunhos perante os reis, e não me envergonharei.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
E recrear-me-hei em teus mandamentos, que tenho amado.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Tambem levantarei as minhas mãos para os teus mandamentos, que amei, e meditarei nos teus estatutos.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Lembra-te da palavra dada ao teu servo, na qual me fizeste esperar.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Isto é a minha consolação na minha afflicção, porque a tua palavra me vivificou.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Os soberbos zombaram grandemente de mim; comtudo não me desviei da tua lei.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Lembrei-me dos teus juizos antiquissimos, ó Senhor, e assim me consolei.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Grande indignação se apoderou de mim por causa dos impios que desamparam a tua lei.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Os teus estatutos teem sido os meus canticos, na casa da minha peregrinação.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Lembrei-me do teu nome, ó Senhor, de noite, e observei a tua lei.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Isto fiz eu, porque guardei os teus mandamentos.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
O Senhor é a minha porção: eu disse que observaria as tuas palavras.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Roguei devéras o teu favor com todo o meu coração: tem piedade de mim, segundo a tua palavra.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Considerei os meus caminhos, e voltei os meus pés para os teus testemunhos.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Apressei-me, e não me detive, a observar os teus mandamentos.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Bandos de impios me despojaram, mas eu não me esqueci da tua lei.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Á meia noite me levantarei para te louvar, pelos teus justos juizos.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Companheiro sou de todos os que te temem e dos que guardam os teus preceitos.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
A terra, ó Senhor, está cheia da tua benignidade: ensina-me os teus estatutos.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Fizeste bem ao teu servo, Senhor, segundo a tua palavra.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Ensina-me bom juizo e sciencia, pois cri nos teus mandamentos.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Antes de ser afflicto andava errado; mas agora tenho guardado a tua palavra.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Tu és bom e fazes bem: ensina-me os teus estatutos.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Os soberbos forjaram mentiras contra mim; mas eu com todo o meu coração guardarei os teus preceitos.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Engrossa-se-lhes o coração como gordura, mas eu me recreio na tua lei.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Foi-me bom ter sido afflicto, para que aprendesse os teus estatutos.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Melhor é para mim a lei da tua bocca do que milhares de oiro ou prata.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
As tuas mãos me fizeram e me formaram; dá-me intelligencia para entender os teus mandamentos.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Os que te temem alegraram-se quando me viram, porque tenho esperado na tua palavra.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Bem sei eu, ó Senhor, que os teus juizos são justos, e que segundo a tua fidelidade me affligiste.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Sirva pois a tua benignidade para me consolar, segundo a palavra que déste ao teu servo.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Venham sobre mim as tuas misericordias, para que viva, pois a tua lei é as minhas delicias.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Confundam-se os soberbos, pois me trataram d'uma maneira perversa, sem causa; mas eu meditarei nos teus preceitos.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Voltem-se para mim os que te temem, e aquelles que teem conhecido os teus testemunhos.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Seja recto o meu coração nos teus estatutos, para que não seja confundido.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Desfallece a minha alma pela tua salvação, mas espero na tua palavra.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Os meus olhos desfallecem pela tua palavra; entretanto dizia: Quando me consolarás tu?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Pois estou como odre no fumo; comtudo não me esqueço dos teus estatutos.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Quantos serão os dias do teu servo? Quando me farás justiça contra os que me perseguem?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Os soberbos me cavaram covas, o que não é conforme á tua lei.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Todos os teus mandamentos são verdade: com mentiras me perseguem; ajuda-me.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Quasi que me teem consumido sobre a terra, mas eu não deixei os teus preceitos.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Vivifica-me segundo a tua benignidade; assim guardarei o testemunho da tua bocca.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Para sempre, ó Senhor, a tua palavra permanece no céu.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
A tua fidelidade dura de geração em geração: tu firmaste a terra, e ella permanece firme.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Elles continuam até ao dia d'hoje, segundo as tuas ordenações; porque todos são teus servos.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Se a tua lei não fôra toda a minha recreação, ha muito que pereceria na minha afflicção.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Nunca me esquecerei dos teus preceitos; pois por elles me tens vivificado.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Sou teu, salva-me; pois tenho buscado os teus preceitos.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Os impios me esperam para me destruirem, mas eu considerarei os teus testemunhos.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Tenho visto fim a toda a perfeição, mas o teu mandamento é amplicissimo.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Oh! quanto amo a tua lei! é a minha meditação em todo o dia.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Tu pelos teus mandamentos me fazes mais sabio do que os meus inimigos, pois estão sempre comigo.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Tenho mais entendimento do que todos os meus mestres, porque os teus testemunhos são a minha meditação.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Entendo mais do que os antigos; porque guardo os teus preceitos.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Desviei os meus pés de todo o caminho mau, para guardar a tua palavra.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Não me apartei dos teus juizos, pois tu me ensinaste.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Oh! quão doces são as tuas palavras ao meu paladar, mais doces do que o mel á minha bocca.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Pelos teus mandamentos alcancei entendimento; pelo que aborreço todo o falso caminho.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
A tua palavra é uma lampada para os meus pés e uma luz para o meu caminho.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Jurei, e o cumprirei, que guardarei os teus justos juizos.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Estou afflictissimo; vivifica-me, ó Senhor, segundo a tua palavra.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Acceita, eu te rogo, as offerendas voluntarias da minha bocca, ó Senhor; ensina-me os teus juizos.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
A minha alma está de continuo nas minhas mãos; todavia não me esqueço da tua lei
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Os impios me armaram laço; comtudo não me desviei dos teus preceitos.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Os teus testemunhos tenho eu tomado por herança para sempre, pois são o gozo do meu coração.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Inclinei o meu coração a guardar os teus estatutos, para sempre, até ao fim.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Aborreço a duplicidade, mas amo a tua lei.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Tu és o meu refugio e o meu escudo; espero na tua palavra.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Apartae-vos de mim, malfeitores, pois guardarei os mandamentos do meu Deus.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Sustenta-me conforme a tua palavra, para que viva, e não me deixes envergonhado da minha esperança.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Sustenta-me, e serei salvo, e de continuo terei respeito aos teus estatutos.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Tu tens pisado aos pés todos os que se desviam dos teus estatutos, pois o engano d'elles é falsidade.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Tu tiraste da terra todos os impios, como a escoria, pelo que amo os teus testemunhos.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
O meu corpo se arrepiou com temor de ti, e temi os teus juizos.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Fiz juizo e justiça: não me entregues aos meus oppressores.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Fica por fiador do teu servo para o bem; não deixes que os soberbos me opprimam.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Os meus olhos desfalleceram pela tua salvação e pela promessa da tua justiça.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Usa com o teu servo segundo a tua benignidade, e ensina-me os teus estatutos.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Sou teu servo: dá-me intelligencia, para entender os teus testemunhos.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Já é tempo de operares ó Senhor, pois elles teem quebrantado a tua lei.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Pelo que amo os teus mandamentos mais do que o oiro, e ainda mais do que o oiro fino.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Por isso estimo todos os teus preceitos ácerca de tudo, como rectos, e aborreço toda a falsa vereda.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Maravilhosos são os teus testemunhos; portanto a minha alma os guarda.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
A entrada das tuas palavras dá luz, dá entendimento aos simplices.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Abri a minha bocca, e respirei, pois que desejei os teus mandamentos.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Olha para mim, e tem piedade de mim, conforme usas com os que amam o teu nome.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Ordena os meus passos na tua palavra, e não se apodere de mim iniquidade alguma.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Livra-me da oppressão do homem; assim guardarei os teus preceitos.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Faze resplandecer o teu rosto sobre o teu servo, e ensina-me os teus estatutos.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Rios d'aguas correm dos meus olhos, porque não guardam a tua lei.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Justo és, ó Senhor, e rectos são os teus juizos.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Os teus testemunhos que ordenaste são rectos e muito fieis.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
O meu zelo me consumiu, porque os meus inimigos se esqueceram da tua palavra.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
A tua palavra é muito pura; portanto o teu servo a ama.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Pequeno sou e desprezado, porém não me esqueço dos teus mandamentos.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
A tua justiça é uma justiça eterna, e a tua lei é a verdade.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Aperto e angustia se apoderam de mim; comtudo os teus mandamentos são o meu prazer.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
A justiça dos teus testemunhos é eterna; dá-me intelligencia, e viverei.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Clamei de todo o meu coração; escuta-me, Senhor, e guardarei os teus estatutos.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
A ti te invoquei; salva-me, e guardarei os teus testemunhos.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Preveni a alva da manhã, e clamei: esperei na tua palavra.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Os meus olhos preveniram as vigilias da noite, para meditar na tua palavra.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Ouve a minha voz, segundo a tua benignidade: vivifica-me, ó Senhor, segundo o teu juizo.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Approximam-se os que se dão a maus tratos: affastam-se da tua lei.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Tu estás perto ó Senhor, e todos os teus mandamentos são a verdade.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Ácerca dos teus testemunhos soube, desde a antiguidade, que tu os fundaste para sempre.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Olha para a minha afflicção, e livra-me, pois não me esqueci da tua lei.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Pleiteia a minha causa, e livra-me: vivifica-me segundo a tua palavra.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
A salvação está longe dos impios, pois não buscam os teus estatutos.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Muitas são, ó Senhor, as tuas misericordias: vivifica-me segundo os teus juizos.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Muitos são os meus perseguidores e os meus inimigos; porém não me desvio dos teus testemunhos.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Vi os transgressores, e me affligi, porque não observam a tua palavra.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Considera como amo os teus preceitos: vivifica-me, ó Senhor, segundo a tua benignidade.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
A tua palavra é a verdade desde o principio, e cada um dos teus juizos dura para sempre.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Principes me perseguiram sem causa, mas o meu coração temeu a tua palavra.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Folgo com a tua palavra, como aquelle que acha um grande despojo.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Abomino e aborreço a falsidade, porém amo a tua lei.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Sete vezes no dia te louvo pelos juizos da tua justiça.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Muita paz teem os que amam a tua lei, e para elles não ha tropeço.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Senhor, tenho esperado na tua salvação, e tenho cumprido os teus mandamentos.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
A minha alma tem observado os teus testemunhos; amo-os excessivamente.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Tenho observado os teus preceitos e os teus testemunhos, porque todos os meus caminhos estão diante de ti.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Chegue a ti o meu clamor, ó Senhor: dá-me entendimento conforme a tua palavra.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Chegue a minha supplica perante a tua face: livra-me segundo a tua palavra.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Os meus labios proferiram o louvor, quando me ensinaste os teus estatutos.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
A minha lingua fallará da tua palavra, pois todos os teus mandamentos são justiça.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Venha a tua mão soccorrer-me, pois elegi os teus preceitos.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Tenho desejado a tua salvação, ó Senhor, a tua lei é todo o meu prazer.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Viva a minha alma, e louvar-te-ha: ajudem-me os teus juizos.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Desgarrei-me como a ovelha perdida; busca o teu servo, pois não me esqueci dos teus mandamentos.

< Masalimo 119 >