< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Esengo na bato oyo bazangi pamela mpe batambolaka kolanda mibeko ya Yawe!
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Esengo na bato oyo babatelaka malako na Ye mpe balukaka Ye na mitema na bango mobimba!
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Basalaka mabe te, kasi balandaka banzela ya Nzambe.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Opesaki mibeko mpo ete etosama malamu.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Tika ete nabongisa etamboli na ngai mpo ete natosa mitindo na Yo!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Na bongo, nakoyoka soni te tango nakotosa mibeko na Yo nyonso.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Nakosanzola Yo na motema ya sembo wana nakoyekola mibeko ya bosembo na Yo.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Nalingi kotosa mitindo na Yo; kosundola ngai libela te!
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Ndenge nini elenge akoki kowumela na nzela ya sembo? Ezali na kotambola kolanda liloba na Yo.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Nalukaka Yo na motema na ngai mobimba; batela ngai mpo ete napengwa te mosika ya mibeko na Yo!
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
Nabatelaka liloba na Yo kati na motema na ngai mpo ete nasala masumu te na miso na Yo.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Yawe, tika ete opambolama! Lakisa ngai mitindo na Yo!
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
Na monoko na ngai, natangaka mibeko na Yo nyonso.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
Nasepelaka kotambola kolanda malako na Yo lokola nde nazali na bomengo nyonso.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Nakanisaka malako na Yo mpe natambolaka na banzela na Yo.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Nasepelaka mingi na malako na Yo mpe nabosanaka liloba na Yo te.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Salela ngai, mosali na Yo, bolamu mpo ete nabika mpe natosa liloba na Yo.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Fungola miso na ngai mpo ete namona kitoko ya mibeko na Yo.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Nazali mopaya awa na mokili; kobombela ngai mibeko na Yo te.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Molimo na ngai ezalaka tango nyonso na posa makasi ya koyeba mibeko na Yo.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Otelemelaka bato ya lofundu, bato oyo balakelama mabe mpe bapengwaka mosika ya mibeko na Yo.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Longola soni mpe kotiolama na bomoi na ngai, pamba te natosaka malako na Yo.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Ezala soki bakambi basali likita mpe bayokani kotelemela ngai, mosali na Yo, nakokanisa kaka mitindo na Yo.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Malako na Yo esepelisaka ngai makasi, epesaka ngai toli.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Nakangami na putulu; batela bomoi na ngai kolanda liloba na Yo.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Nayebisaki Yo banzela na ngai, mpe oyanolaki ngai; lakisa ngai mibeko na Yo!
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Sala ete nasosola nzela ya mitindo na Yo mpo ete nakanisa misala minene na Yo!
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Nazali kolela mpo na pasi na motema; pesa ngai mpiko kolanda liloba na Yo.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Mema ngai mosika ya nzela ya lokuta; mpe, na boboto na Yo, teya ngai mobeko na Yo.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
Naponaki nzela ya bosolo; natambolaka kolanda mibeko na Yo.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Nakangami na malako na Yo; Yawe, koyokisa ngai soni te.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Nakimaka mbangu kati na nzela ya mibeko na Yo, pamba te opesaka ngai bososoli na yango.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Yawe, teya ngai nzela ya mitindo na Yo mpo ete nabatela yango kino na suka.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Pesa ngai bososoli mpo ete natosa mibeko na Yo mpe nalanda yango na motema na ngai mobimba.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Tambolisa ngai kati na nzela ya mibeko na Yo, pamba te nasepelaka na yango.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Sala ete motema na ngai esepela na malako na Yo, kasi na bomengo te!
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Longola miso na ngai na makambo ya pamba, batela bomoi na ngai kati na banzela na Yo!
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Kokisela mosali na Yo bilaka oyo opesaki mpo na bato oyo batosaka Yo.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Longola mosika na ngai soni oyo nabangaka, pamba te mibeko na Yo ezali malamu.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Nasepelaka makasi na mibeko na Yo; batela bomoi na ngai kati na bosembo na Yo!
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Yawe, tika ete bolingo ekomela ngai, mpe lobiko na Yo, kolanda elaka na Yo;
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
bongo nakokoka kozwa eyano ya kopesa na mofingi na ngai, pamba te natiaka elikya na liloba na Yo.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Tika ete monoko na ngai elobaka kaka bosolo, pamba te natiaka elikya kati na mibeko na Yo.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Nakotosa mibeko na Yo tango nyonso, mpe libela na libela.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Nakobika na bonsomi ya solo, pamba te nasepelaka kotosa mitindo na Yo.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Nakolobela malako na Yo liboso ya bakonzi na kozanga koyoka soni.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Nasepelaka mingi na mibeko na Yo mpe nalingaka yango mingi.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Nalapi ndayi mpo na mibeko na Yo, oyo nalingaka, mpe nakokanisa mitindo na Yo.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Kanisa makambo oyo olobaki na mosali na Yo, pamba te opesaki ngai elikya.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
Kati na pasi na ngai, liloba na Yo ebondisaka; batela bomoi na ngai kolanda elaka na Yo.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Solo, bato ya lolendo batiolaki ngai makasi; kasi ngai, natikalaki kopengwa te na mibeko na Yo.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Yawe, tango nakanisaka mikano na Yo ya kala, nazwaka kati na yango kobondisama.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Nayokaka pasi mingi na motema tango namonaka bato mabe kosundola mibeko na Yo.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Nakoma koyemba mitindo na Yo na bisika nyonso epai wapi nazali moleki nzela.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Yawe, nakanisaka Yo na butu mpo ete nabatela mibeko na Yo;
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
pamba te libula na ngai ezali: kotosa mibeko na Yo.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Yawe, nalobi lisusu ete libula na ngai ezali: kotosa liloba na Yo.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Na motema na ngai mobimba, nalukaka kosepelisa Yo; salela ngai ngolu kolanda bilaka na Yo!
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
Natali malamu etamboli na ngai mpe namizongisi kati na malako na Yo.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Natosaka mibeko na Yo noki, nazelisaka te.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Solo, mitambo ya bato mabe ekangaki ngai, kasi ngai nabosanaki te mibeko na Yo.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Na kati-kati ya butu, nalamukaka mpo na kokumisa Yo likolo na mibeko na Yo ya sembo.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Nazali moninga ya bato nyonso oyo batosaka Yo mpe babatelaka mitindo na Yo.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
Yawe, mokili etondi na bolingo na Yo; lakisa ngai mitindo na Yo!
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Yawe, salela mosali na Yo bolamu kolanda liloba na Yo.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Teya ngai bolamu ya bososoli mpe ya mayele, pamba te namipesaka na mibeko na Yo.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Liboso ete obeta ngai, nazalaki mopengwi; kasi sik’oyo, nakomi kotosa liloba na Yo.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Ozali malamu mpe osalaka makambo ya malamu; teya ngai mitindo na Yo!
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Bato ya lolendo bakoselaka ngai makambo; kasi ngai, natosaka mitindo na Yo na motema na ngai mobimba.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Mitema na bango ezali mabanga; kasi ngai, nasepelaka na mibeko na Yo.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Ezalaki penza malamu mpo na ngai ete obeta ngai, mpo ete nayekola mitindo na Yo.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Mpo na ngai, mibeko oyo ozwaki mpe osakolaki na monoko na Yo ezali malamu koleka biloko nkoto moko ya wolo mpe ya palata.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Osalaki mpe olendisaki ngai na maboko na Yo, pesa ngai mayele mpo ete nayekola mibeko na Yo!
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Tango bato oyo batosaka Yo bamonaka ngai, basepelaka makasi, mpo ete natiaka elikya na liloba na Yo.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Yawe, nayebi malamu ete mibeko na Yo ezali sembo, mpe ete ezali kaka mpo na bolingo na Yo nde obetaki ngai.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Tika ete bolingo na Yo ebondisa ngai, kolanda elaka na Yo epai ya mosali na Yo!
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Talisa ngai mawa na Yo mpo ete nabika, pamba te nasepelaka na mibeko na Yo.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Tika ete bato wana ya lofundu, oyo bamonisaka ngai pasi na kozanga tina, bakufa soni! Kasi ngai nakokanisa kaka mibeko na Yo.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Tika ete bato oyo batosaka Yo, ba-oyo bayebi malako na Yo, bazongela ngai.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Tika ete motema na ngai ezanga pamela mpo na kotosa mitindo na Yo, mpo ete nakufa soni te.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Natondi na posa ya lobiko na Yo, nazali na elikya kati na liloba na Yo.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Miso na ngai elembi kozela kokokisama ya elaka na Yo; nakomi komituna: « Okobondisa ngai tango nini? »
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Nakomi lokola mbeki oyo ezali kokawuka na milinga, nzokande nabosanaka mitindo na Yo te.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Mikolo ya bomoi ya mosali na Yo ezali motango boni? Mokolo nini okopesa banyokoli na ngai etumbu?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Bato ya lolendo batimoli mabulu mpo na kokanga ngai, baboyi kotosa mibeko na Yo.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Mibeko na Yo nyonso ezali sembo; kasi bazali konyokola ngai kaka pamba; yaka kosunga ngai!
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Etikali moke mpo ete balongola ngai na mokili; kasi atako bongo, nasundoli mibeko na Yo te.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Kati na bolingo na Yo, batela bomoi na ngai mpo ete natosa malako na Yo.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Yawe, liloba na Yo ezali mpo na seko, epikama kati na likolo;
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
boyengebene na Yo ekowumela seko na seko. Okela mabele, mpe ezali kaka kino na mokolo ya lelo;
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
opesa mibeko, mpe ezali kaka kino na mokolo ya lelo, pamba te nyonso kati na mokili mobimba epesaka Yo lokumu.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Soki nasepelaki na mibeko na Yo te, mbele nakufa kala kati na pasi na ngai.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Nakotikala kobosana ata moke te mitindo na Yo, pamba te obatelaka bomoi na ngai na nzela na yango.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Bikisa ngai, pamba te nazali moto na Yo mpe natosaka mitindo na Yo!
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Bato mabe bazali koluka koboma ngai, kasi ngai nakangami kaka na malako na Yo.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
Na nyonso oyo emonanaka lokola ya kokoka, namonaki mondelo; kasi mibeko na Yo ezalaka na mondelo te.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Nalingaka mibeko na Yo mingi! Nakanisaka yango mikolo nyonso.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Mibeko na Yo ekomisaka ngai moto ya bwanya koleka banguna na ngai; ezalaka elongo na ngai tango nyonso.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
Naleki balakisi na ngai nyonso na mayele, pamba te nakanisaka malako na Yo.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
Naleki mibange na bososoli, pamba te natosaka mibeko na Yo.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
Natambolaka te na banzela nyonso ya mabe mpo na kotosa liloba na Yo.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Nakangamaka na mibeko na Yo, pamba te Yo moko nde oteyaka ngai yango.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Tala ndenge mitindo na Yo ezali elengi na monoko na ngai! Ezali malamu koleka mafuta ya nzoyi.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Mitindo na Yo ekomisi ngai moto ya bososoli; yango wana nayinaka nzela nyonso ya mabe.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Liloba na Yo ezali mwinda mpo na makolo na ngai, mpe pole mpo na nzela na ngai.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
Nalapaki ndayi oyo mpe nakokokisa yango: « Nakotosaka mibeko ya bosembo na Yo. »
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Motema na ngai etutami makasi; Yawe, batela bomoi na ngai kolanda liloba na Yo.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Yawe, ndima likabo ya bibebu na ngai, mpe teya ngai mibeko na Yo.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Solo, nakutanaka tango nyonso na makama, kasi nabosanaka mibeko na Yo te.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Bato mabe batiaka mitambo mpo ete nakweya, kasi nakangamaka kaka na mibeko na Yo.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Malako na Yo ezali libula na ngai mpo na libela, esalaka esengo ya motema na ngai.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
Nazwa mokano ya kotambola kolanda mitindo na Yo, tango nyonso, kino na suka.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
Nayinaka bato ya mitema mibale, kasi nalingaka nde mibeko na Yo.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ozali ebombamelo mpe nguba na ngai; natiaka elikya kati na liloba na Yo.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Bato ya misala mabe, bokende mosika na ngai! Nakotosa mibeko ya Nzambe na ngai!
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Sunga ngai kolanda elaka na Yo, mpe nakobika; koyokisa elikya na ngai soni te.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Sunga ngai mpo ete nabika; nakotikala kobosana mitindo na Yo ata moke te.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Obwakaka bato nyonso oyo bapesaka mitindo na Yo mokongo, pamba te mokano na bango ezalaka ya lokuta.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Olongolaka bato nyonso ya mabe ya mokili lokola bosoto; yango wana nalingaka malako na Yo.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Nalengaka na somo liboso na Yo mpe nabangaka mikano na Yo.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
Natambolaka na bosembo mpe bosolo; kokaba ngai na maboko ya banyokoli na ngai te!
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Kamata mokumba ya bolamu na ngai, mosali na Yo; tika ete bato ya lolendo banyokola ngai te.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Miso na ngai elembi kozela lisungi kowuta na Yo mpe kokokisama ya bosembo na Yo kolanda elaka na Yo.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Salela ngai, mosali na Yo, kolanda bolingo na Yo, lakisa ngai mitindo na Yo.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Nazali mosali na Yo; pesa ngai mayele mpo ete nasosola malako na Yo.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Yawe, tango ya kosala ekoki; pamba te bazali kobuka mibeko na Yo!
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Yango wana nalingaka mibeko na Yo koleka wolo, koleka kutu wolo ya peto;
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
namonaka mpe malako na Yo nyonso alima; nzokande, nayinaka lokuta nyonso.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Malako na Yo ezali kitoko, yango wana nabatelaka yango.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
Emoniseli ya liloba na Yo engengisaka, epesaka bazoba mayele.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
Monoko na ngai efungwamaka makasi likolo ya kozela, pamba te nazali na posa makasi ya mibeko na Yo.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Baluka epai na ngai mpe talisa ngai ngolu na Yo kolanda ndenge okata mpo na bato oyo balingaka Kombo na Yo.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Lendisa bomoi na ngai na nzela ya liloba na Yo mpe pekisa mabe ete ekonza ngai te.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Kangola ngai wuta na minyoko ya bato, mpe nakotosa mibeko na Yo.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Tika ete elongi na Yo engengela ngai, mosali na Yo; lakisa ngai mibeko na Yo!
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Miso na ngai ezali kosopa mpinzoli, pamba te mibeko na Yo ezali kotosama te.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Yawe, ozali sembo, mpe mibeko na Yo ezali alima;
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
osalaki malako na Yo na bosembo mpe na bolingo.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Mpo ete banguna na ngai bazwaka liloba na Yo na motuya te, nayokaka kanda makasi komata ngai na motema.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Nzokande liloba na Yo ezali penza peto; mpe ngai, mosali na Yo, nalingaka yango.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Atako nazali moke mpe batiolaka ngai, kasi nabosanaka mitindo na Yo te.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Bosembo na Yo ekotikala bongo mpo na libela, ekotikala kobongwana te; mpe mibeko na Yo ezali solo.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Pasi ekangi ngai, mpe mayele esili ngai; kasi mibeko na Yo epesaka ngai esengo.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Malako na Yo ezali sembo mpo na libela; pesa ngai bososoli mpo ete nabika!
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
Nazali kobelela Yo na motema na ngai mobimba: « Yawe, yanola ngai; nakotosa mitindo na Yo!
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Nazali kobelela Yo: bikisa ngai, mpo ete natosa malako na Yo!
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Nalamukaka liboso ete tongo etana mpo na kobelela Yo, nazali na elikya kati na liloba na Yo.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Nalamukaka na kati-kati ya butu mpo na kokanisa mitindo na Yo.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Yoka ngai na bolingo na Yo! Yawe, batela bomoi na ngai kolanda mibeko na Yo!
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Bato oyo basalaka mabongisi mabe, oyo batosaka mibeko na Yo te, bazali koya pene na ngai.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Nzokande Yo, Yawe, ozali pene, mpe mibeko na Yo nyonso ezali bosolo.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Wuta kala, ngai nayebi, na nzela ya malako na Yo, ete otia mibeko yango mpo na libela.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Mona malamu pasi na ngai mpe kangola ngai, pamba te nabosanaka mibeko na Yo te.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Kota likambo na ngai mpe kangola ngai, batela bomoi na ngai kolanda elaka na Yo!
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Lobiko ezalaka mosika ya bato mabe, pamba te bamonaka pamba mitindo na Yo.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Yawe, mawa na Yo ezali monene penza; batela bomoi na ngai kolanda mibeko na Yo.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Banyokoli mpe banguna na ngai bazali solo ebele, kasi ngai nakangamaka kaka na malako na Yo.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
Natalaka na nkele bato oyo bazangi kondima, ba-oyo batosaka liloba na Yo te.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Yawe, tala ndenge nalingaka mitindo na Yo! Batela bomoi na ngai kolanda bolingo na Yo.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Moboko ya liloba na Yo ezali bosolo, mpe mibeko nyonso ya bosembo na Yo ezali mpo na libela.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Bakambi banyokolaka ngai kaka pamba, kasi kaka liloba na Yo nde ebangisaka motema na ngai.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
Nasepelaka na liloba na Yo lokola moto oyo azwi bomengo ebele ya bitumba.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Nayinaka lokuta mpe nayokaka yango nkele, nalingaka nde mibeko na Yo.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Nakumisaka Yo mbala sambo na mokolo mpo na mibeko ya bosembo na Yo.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Bato oyo balingaka mibeko na Yo bazali bato na kimia monene, mpe eloko moko te ekobetisa bango lisusu mabaku.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
Yawe, natielaka Yo motema mpo ete obikisa ngai, mpe natosaka mibeko na Yo.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Natosaka malako na Yo, pamba te nalingaka yango makasi.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Natosaka malako mpe mibeko na Yo, pamba te oyebi banzela na ngai nyonso.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Yawe, tika ete koganga na ngai ekoma kino epai na Yo! Pesa ngai bososoli kolanda liloba na Yo!
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Tika ete mabondeli na ngai ekoma kino epai na Yo! Kangola ngai kolanda elaka na Yo.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Tika ete bibebu na ngai ekumisa Yo, pamba te olakisaka ngai mitindo na Yo!
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Tika ete lolemo na ngai eyemba liloba na Yo, pamba te mibeko na Yo nyonso ezali sembo.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Tika ete loboko na Yo esunga ngai, pamba te napona kolanda malako na Yo.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
Yawe, nazali na posa makasi ya lobiko na Yo; mibeko na Yo epesaka ngai esengo.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Tika ete nazala na bomoi mpo na kokumisa Yo, mpe tika ete mibeko na Yo esunga ngai!
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Nazali koyengayenga lokola meme oyo ebungi; luka ngai, mosali na Yo, pamba te nabosani mibeko na Yo te. »

< Masalimo 119 >