< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Bienheureux ceux qui sont intègres dans leur voie, qui marchent dans la loi de l’Éternel.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Bienheureux ceux qui gardent ses témoignages, qui le cherchent de tout leur cœur,
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Qui aussi ne font pas d’iniquité; ils marchent dans ses voies.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Tu as commandé tes préceptes pour qu’on les garde soigneusement.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Oh, que mes voies soient dressées, pour garder tes statuts!
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Alors je ne serai pas honteux quand je regarderai à tous tes commandements.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
Je te célébrerai d’un cœur droit, quand j’aurai appris les ordonnances de ta justice.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
Je garderai tes statuts; ne me délaisse pas tout à fait.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Comment un jeune homme rendra-t-il pure sa voie? Ce sera en y prenant garde selon ta parole.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
Je t’ai cherché de tout mon cœur; ne me laisse pas m’égarer de tes commandements.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
J’ai caché ta parole dans mon cœur, afin que je ne pèche pas contre toi.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Éternel! tu es béni; enseigne-moi tes statuts.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
J’ai raconté de mes lèvres toutes les ordonnances de ta bouche.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
J’ai pris plaisir au chemin de tes témoignages, autant qu’à toutes les richesses.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
Je méditerai tes préceptes et je regarderai à tes sentiers.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
Je fais mes délices de tes statuts, je n’oublierai pas ta parole.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Fais du bien à ton serviteur, [et] je vivrai et je garderai ta parole.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Ouvre mes yeux, et je verrai les merveilles qui sont dans ta loi.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
Je suis étranger dans le pays; ne me cache pas tes commandements.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
Mon âme est brisée par l’ardent désir qu’elle a en tout temps pour tes ordonnances.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Tu as tancé les orgueilleux, les maudits, qui s’égarent de tes commandements.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Roule de dessus moi l’opprobre et le mépris; car je garde tes témoignages.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Les princes même se sont assis [et] parlent contre moi; ton serviteur médite tes statuts.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Tes témoignages sont aussi mes délices, les hommes de mon conseil.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
Mon âme est attachée à la poussière; fais-moi vivre selon ta parole.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
Je [t’]ai déclaré mes voies, et tu m’as répondu; enseigne-moi tes statuts.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Fais-moi comprendre la voie de tes préceptes, et je méditerai sur tes merveilles.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
Mon âme, de tristesse, se fond en larmes; affermis-moi selon ta parole.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Éloigne de moi la voie du mensonge, et, dans ta grâce, donne-moi ta loi.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
J’ai choisi la voie de la fidélité, j’ai placé [devant moi] tes jugements.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Je suis attaché à tes témoignages: Éternel! ne me rends point honteux.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
Je courrai dans la voie de tes commandements, quand tu auras mis mon cœur au large.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Éternel! enseigne-moi la voie de tes statuts, et je l’observerai jusqu’à la fin.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Donne-moi de l’intelligence, et j’observerai ta loi, et je la garderai de tout mon cœur.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Fais-moi marcher dans le chemin de tes commandements, car j’y prends plaisir.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Incline mon cœur à tes témoignages, et non point au gain.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Détourne mes yeux pour qu’ils ne regardent pas la vanité; fais-moi vivre dans ta voie.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Confirme ta parole à ton serviteur, qui est [adonné] à ta crainte.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Détourne de moi l’opprobre que je crains; car tes jugements sont bons.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Voici, j’ai ardemment désiré tes préceptes; fais-moi vivre dans ta justice.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
Et que ta bonté vienne à moi, ô Éternel! – ton salut, selon ta parole!
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
Et j’aurai de quoi répondre à celui qui m’outrage; car je me suis confié en ta parole.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Et n’ôte pas entièrement de ma bouche la parole de la vérité; car je me suis attendu à tes jugements.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
Alors je garderai ta loi continuellement, à toujours et à perpétuité;
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
Et je marcherai au large, car j’ai recherché tes préceptes;
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
Et je parlerai de tes témoignages devant des rois, et je ne serai pas honteux;
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
Et je trouverai mes délices en tes commandements que j’ai aimés;
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Et je lèverai mes mains vers tes commandements que j’ai aimés, et je méditerai tes statuts.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Souviens-toi de ta parole à ton serviteur, à laquelle tu as fait que je me suis attendu.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
C’est ici ma consolation dans mon affliction, que ta parole m’a fait vivre.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
Les orgueilleux se sont moqués de moi excessivement: je n’ai pas dévié de ta loi;
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
Je me suis souvenu de tes ordonnances de jadis, ô Éternel! et je me suis consolé.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Une ardente indignation m’a saisi à cause des méchants qui abandonnent ta loi.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Tes statuts m’ont été des cantiques, dans la maison de mon pèlerinage.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
Je me suis souvenu de ton nom pendant la nuit, ô Éternel! et j’ai gardé ta loi.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
Cela m’est arrivé, car j’ai observé tes préceptes.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Ma part, ô Éternel! je l’ai dit, c’est de garder tes paroles.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
Je t’ai imploré de tout mon cœur: use de grâce envers moi selon ta parole.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
J’ai pensé à mes voies, et j’ai tourné mes pieds vers tes témoignages.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
Je me suis hâté, et je n’ai point différé de garder tes commandements.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
Les cordes des méchants m’ont entouré: je n’ai pas oublié ta loi.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
Je me lève à minuit pour te célébrer à cause des ordonnances de ta justice.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
Je suis le compagnon de tous ceux qui te craignent, et de ceux qui gardent tes préceptes.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
La terre, ô Éternel! est pleine de ta bonté; enseigne-moi tes statuts.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Tu as fait du bien à ton serviteur, ô Éternel! selon ta parole.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Enseigne-moi le bon sens et la connaissance; car j’ai ajouté foi à tes commandements.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Avant que je sois affligé, j’errais; mais maintenant je garde ta parole.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Tu es bon et bienfaisant; enseigne-moi tes statuts.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
Les orgueilleux ont inventé contre moi des mensonges; j’observerai tes préceptes de tout mon cœur.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Leur cœur est épaissi comme la graisse; moi, je trouve mes délices en ta loi.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
Il est bon pour moi que j’aie été affligé, afin que j’apprenne tes statuts.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
La loi de ta bouche est meilleure pour moi que des milliers [de pièces] d’or et d’argent.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Tes mains m’ont fait et façonné; rends-moi intelligent, et j’apprendrai tes commandements.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Ceux qui te craignent me verront, et se réjouiront; car je me suis attendu à ta parole.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Je sais, ô Éternel! que tes jugements sont justice, et que c’est en fidélité que tu m’as affligé.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Que ta bonté, je te prie, soit ma consolation, selon ta parole à ton serviteur.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Que tes compassions viennent sur moi, et je vivrai; car ta loi fait mes délices.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Que les orgueilleux soient couverts de honte, car sans cause ils ont agi perversement envers moi; moi, je médite tes préceptes.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Que ceux qui te craignent se tournent vers moi, et ceux qui connaissent tes témoignages.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Que mon cœur soit intègre dans tes statuts, afin que je ne sois pas honteux.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Mon âme languit après ton salut; je m’attends à ta parole.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Mes yeux languissent après ta parole; et j’ai dit: Quand me consoleras-tu?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
Car je suis devenu comme une outre mise à la fumée; je n’oublie pas tes statuts.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
Combien [dureront] les jours de ton serviteur? Quand exécuteras-tu le jugement contre ceux qui me persécutent?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Les orgueilleux ont creusé pour moi des fosses, ce qui n’est pas selon ta loi.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
Tous tes commandements sont fidélité. On me persécute sans cause; aide-moi!
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
Peu s’en est fallu qu’ils ne m’aient consumé sur la terre; mais moi, je n’ai pas abandonné tes préceptes.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Selon ta bonté, fais-moi vivre, et je garderai le témoignage de ta bouche.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Éternel! ta parole est établie à toujours dans les cieux.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Ta fidélité est de génération en génération. Tu as établi la terre, et elle demeure ferme.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Selon tes ordonnances, [ces choses] demeurent fermes aujourd’hui; car toutes choses te servent.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Si ta loi n’avait fait mes délices, j’aurais péri dans mon affliction.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
Jamais je n’oublierai tes préceptes, car par eux tu m’as fait vivre.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
Je suis à toi, sauve-moi; car j’ai recherché tes préceptes.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Les méchants m’attendent pour me faire périr; [mais] je suis attentif à tes témoignages.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
J’ai vu la fin de toute perfection; ton commandement est fort étendu.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
Combien j’aime ta loi! tout le jour je la médite.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Tes commandements m’ont rendu plus sage que mes ennemis, car ils sont toujours avec moi.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
J’ai plus d’intelligence que tous ceux qui m’enseignent, parce que je médite tes préceptes.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
J’ai plus de sens que les anciens, parce que j’observe tes préceptes.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
J’ai gardé mes pieds de toute mauvaise voie, afin que je garde ta parole.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
Je ne me suis pas détourné de tes ordonnances, car c’est toi qui m’as instruit.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
Que tes paroles ont été douces à mon palais, plus que le miel à ma bouche!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Par tes préceptes je suis devenu intelligent; c’est pourquoi je hais toute voie de mensonge.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Ta parole est une lampe à mon pied, et une lumière à mon sentier.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
J’ai juré, et je le tiendrai, de garder les ordonnances de ta justice.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
Je suis extrêmement affligé, ô Éternel! fais-moi vivre selon ta parole!
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Agrée, je te prie, ô Éternel! les offrandes volontaires de ma bouche, et enseigne-moi tes ordonnances.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
Ma vie est continuellement dans ma main, mais je n’oublie pas ta loi.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Les méchants m’ont tendu un piège; mais je ne me suis pas égaré de tes préceptes.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
Tes témoignages me sont un héritage à toujours; car ils sont la joie de mon cœur.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
J’ai incliné mon cœur à pratiquer tes statuts, à toujours, jusqu’à la fin.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
J’ai eu en haine ceux qui sont doubles de cœur, mais j’aime ta loi.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Tu es mon asile et mon bouclier; je me suis attendu à ta parole.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Retirez-vous de moi, vous qui faites le mal, et j’observerai les commandements de mon Dieu.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Soutiens-moi selon ta parole, et je vivrai; et ne me laisse pas être confus en mon espérance.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Soutiens-moi, et je serai sauvé, et je regarderai continuellement tes statuts.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Tu as rejeté tous ceux qui s’égarent de tes statuts; car leur tromperie n’est que mensonge.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
Tu ôtes tous les méchants de la terre, comme des scories; c’est pourquoi j’aime tes témoignages.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Ma chair frissonne de la frayeur que j’ai de toi, et j’ai craint à cause de tes jugements.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
J’ai pratiqué le jugement et la justice; ne m’abandonne pas à mes oppresseurs.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Sois le garant de ton serviteur pour [son] bien; que les orgueilleux ne m’oppriment pas.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mes yeux languissent après ton salut et la parole de ta justice.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Agis envers ton serviteur selon ta bonté, et enseigne-moi tes statuts.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
Je suis ton serviteur; rends-moi intelligent, et je connaîtrai tes témoignages.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
Il est temps que l’Éternel agisse: ils ont annulé ta loi.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
C’est pourquoi j’aime tes commandements plus que l’or, et que l’or épuré.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
C’est pourquoi j’estime droits tous [tes] préceptes, à l’égard de toutes choses; je hais toute voie de mensonge.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Tes témoignages sont merveilleux; c’est pourquoi mon âme les observe.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
L’entrée de tes paroles illumine, donnant de l’intelligence aux simples.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
J’ai ouvert ma bouche, et j’ai soupiré; car j’ai un ardent désir de tes commandements.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Tourne-toi vers moi et use de grâce envers moi, selon ta coutume envers ceux qui aiment ton nom.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Affermis mes pas dans ta parole, et qu’aucune iniquité ne domine en moi.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Rachète-moi de l’oppression de l’homme, et je garderai tes préceptes.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Fais luire ta face sur ton serviteur, et enseigne-moi tes statuts.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Des ruisseaux d’eau coulent de mes yeux, parce qu’on ne garde pas ta loi.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Tu es juste, ô Éternel! et droit dans tes jugements.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Tu as commandé la justice de tes témoignages, et la fidélité, strictement.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Mon zèle m’a dévoré; car mes oppresseurs ont oublié tes paroles.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Ta parole est bien affinée, et ton serviteur l’aime.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
Je suis petit et méprisé; je n’ai pas oublié tes préceptes.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Ta justice est une justice à toujours, et ta loi est vérité.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
La détresse et l’angoisse m’avaient atteint; tes commandements sont mes délices.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
La justice de tes témoignages est à toujours; donne-moi de l’intelligence, et je vivrai.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
J’ai crié de tout mon cœur; réponds-moi, Éternel! j’observerai tes statuts.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
Je t’invoque: sauve-moi! et je garderai tes témoignages.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
J’ai devancé le crépuscule, et j’ai crié; je me suis attendu à ta parole.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Mes yeux ont devancé les veilles de la nuit pour méditer ta parole.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Écoute ma voix, selon ta bonté, ô Éternel! Fais-moi vivre selon ton ordonnance.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
Ceux qui poursuivent la méchanceté se sont approchés de moi; ils s’éloignent de ta loi.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Éternel! tu es proche; et tous tes commandements sont vérité.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Dès longtemps j’ai connu, d’après tes témoignages, que tu les as fondés pour toujours.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Vois mon affliction, et délivre-moi! Car je n’ai pas oublié ta loi.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Prends en main ma cause, et rachète-moi! Fais-moi vivre selon ta parole.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Le salut est loin des méchants, car ils ne recherchent pas tes statuts.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Tes compassions sont en grand nombre, ô Éternel! – fais-moi vivre selon tes ordonnances.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Mes persécuteurs et mes oppresseurs sont en grand nombre; je n’ai point dévié de tes témoignages.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
J’ai vu les perfides, et j’en ai eu horreur, parce qu’ils ne gardaient pas ta parole.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Considère que j’ai aimé tes préceptes; Éternel! fais-moi vivre selon ta bonté.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
La somme de ta parole est [la] vérité, et toute ordonnance de ta justice est pour toujours.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Des princes m’ont persécuté sans cause; mais mon cœur a eu peur de ta parole.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
J’ai de la joie en ta parole, comme un [homme] qui trouve un grand butin.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
Je hais, et j’ai en horreur le mensonge; j’aime ta loi.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Sept fois le jour je te loue, à cause des ordonnances de ta justice.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Grande est la paix de ceux qui aiment ta loi; et pour eux il n’y a pas de chute.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
J’ai espéré en ton salut, ô Éternel! et j’ai pratiqué tes commandements.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
Mon âme a gardé tes témoignages, et je les aime beaucoup.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
J’ai gardé tes préceptes et tes témoignages; car toutes mes voies sont devant toi.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Que mon cri parvienne devant toi, ô Éternel! Rends-moi intelligent, selon ta parole!
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Que ma supplication vienne devant toi; délivre-moi selon ta parole!
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Mes lèvres publieront [ta] louange, quand tu m’auras enseigné tes statuts.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Ma langue parlera haut de ta parole; car tous tes commandements sont justice.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Ta main me sera pour secours, car j’ai choisi tes préceptes.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
J’ai ardemment désiré ton salut, ô Éternel! et ta loi est mes délices.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Que mon âme vive, et elle te louera; et fais que tes ordonnances me soient en aide!
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
J’ai erré comme une brebis qui périt: cherche ton serviteur, car je n’ai pas oublié tes commandements.

< Masalimo 119 >