< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
ALEPH. Blessed are those whose ways are blameless, who walk according to the law of the LORD.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Blessed are those who keep his decrees, who seek him with their whole heart.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
Yes, they do nothing wrong. They walk in his ways.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
You have commanded your precepts, that we should fully obey them.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
Oh that my ways were steadfast to obey your statutes.
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Then I wouldn't be disappointed, when I consider all of your commandments.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
I will give thanks to you with uprightness of heart, when I learn your righteous judgments.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
I will observe your statutes. Do not utterly forsake me.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
BET. How can a young man keep his way pure? By living according to your word.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
With my whole heart, I have sought you. Do not let me wander from your commandments.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
In my heart I have hidden your word, that I might not sin against you.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Blessed are you, LORD. Teach me your statutes.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
With my lips, I have declared all the ordinances of your mouth.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
I have rejoiced in the way of your testimonies, as much as in all riches.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
I will meditate on your precepts, and consider your ways.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
I will delight myself in your statutes. I will not forget your word.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
GIMEL. Deal bountifully with your servant, that I may live and keep your word.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Open my eyes, that I may see wondrous things out of your Law.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
I am a stranger on the earth. Do not hide your commandments from me.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
My soul is consumed with longing for your ordinances at all times.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
You have rebuked the proud who are cursed, who wander from your commandments.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Take reproach and contempt away from me, for I have kept your statutes.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
Though princes sit and slander me, your servant will meditate on your statutes.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
Indeed your statutes are my delight, and my counselors.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
DALET. My soul is laid low in the dust. Revive me according to your word.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
I declared my ways, and you answered me. Teach me your statutes.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Let me understand the teaching of your precepts. Then I will meditate on your wondrous works.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
My soul is weary with sorrow: strengthen me according to your word.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Keep me from the way of deceit. Grant me your Law graciously.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
I have chosen the way of truth. I have set your ordinances before me.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
I cling to your statutes, LORD. Do not let me be disappointed.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
I run in the path of your commandments, for you have set my heart free.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
HEY Teach me, LORD, the way of your statutes. I will keep them to the end.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Give me understanding, and I will keep your Law. Yes, I will obey it with my whole heart.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Direct me in the path of your commandments, for I delight in them.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Turn my heart toward your statutes, not toward selfish gain.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Turn my eyes away from looking at worthless things. Revive me in your ways.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Fulfill your promise to your servant, that you may be feared.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Take away my disgrace that I dread, for your ordinances are good.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Look, I long for your precepts. Revive me in your righteousness.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
WAW. Let your loving kindness also come to me, LORD, your salvation, according to your word.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
So I will have an answer for him who reproaches me, for I trust in your word.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
Do not snatch the word of truth out of my mouth, for I put my hope in your ordinances.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
So I will obey your Law continually, forever and ever.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
I will walk in liberty, for I have sought your precepts.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
I will also speak of your statutes before kings, and will not be disappointed.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
I will delight myself in your commandments, because I love them.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
I reach out my hands for your commandments, which I love. I will meditate on your statutes.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
ZAYIN. Remember your word to your servant, because you gave me hope.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
This is my comfort in my affliction, for your word has revived me.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
The arrogant mock me excessively, but I do not swerve from your Law.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
I remember your ordinances of old, LORD, and have comforted myself.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Indignation has taken hold on me, because of the wicked who forsake your Law.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Your statutes have been my songs, in the house where I live.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
I have remembered your name, LORD, in the night, and I obey your Law.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
This is my way, that I keep your precepts.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
HET. The LORD is my portion. I promised to obey your words.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
I sought your favor with my whole heart. Be merciful to me according to your word.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
I considered my ways, and turned my steps to your statutes.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
I will hurry, and not delay, to obey your commandments.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
The ropes of the wicked bind me, but I won't forget your Law.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
At midnight I will rise to give thanks to you, because of your righteous ordinances.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
I am a friend of all those who fear you, of those who observe your precepts.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
The earth is full of your loving kindness, LORD. Teach me your statutes.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
TET. Do good to your servant, according to your word, LORD.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Teach me good judgment and knowledge, for I believe in your commandments.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Before I was afflicted, I went astray; but now I observe your word.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
You are good, and do good. Teach me your statutes.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
The proud have smeared a lie upon me. With my whole heart, I will keep your precepts.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Their heart is as callous as the fat, but I delight in your Law.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
It is good for me that I have been afflicted, that I may learn your statutes.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
The Law you have spoken is better to me than thousands of pieces of gold and silver.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
YOD Your hands have made me and formed me. Give me understanding, that I may learn your commandments.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Those who fear you will see me and be glad, because I have put my hope in your word.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
LORD, I know that your judgments are righteous, that in faithfulness you have humbled me.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Please let your loving kindness be for my comfort, according to your word to your servant.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Let your tender mercies come to me, that I may live; for your Law is my delight.
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Let the proud be disappointed, for they have overthrown me wrongfully. I will meditate on your precepts.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Let those who fear you turn to me. They will know your statutes.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Let my heart be blameless toward your decrees, that I may not be disappointed.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
KAPH. My soul faints for your salvation. I hope in your word.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
My eyes fail for your word. I say, "When will you comfort me?"
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
For I have become like a wineskin in the smoke. I do not forget your statutes.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
How many are the days of your servant? When will you execute judgment on those who persecute me?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
The proud have dug pits for me, contrary to your Law.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
All of your commandments are faithful. They persecute me wrongfully. Help me.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
They had almost wiped me from the earth, but I did not forsake your precepts.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Preserve my life according to your loving kindness, so I will obey the statutes of your mouth.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
LAMED. LORD, your word is settled in heaven forever.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Your faithfulness is to all generations. You have established the earth, and it remains.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
Your laws remain to this day, for all things serve you.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Unless your Law had been my delight, I would have perished in my affliction.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
I will never forget your precepts, for with them, you have revived me.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
I am yours. Save me, for I have sought your precepts.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
The wicked have waited for me, to destroy me. I will consider your statutes.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
I have seen a limit to all perfection, but your commands are boundless.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
MEM. How I love your Law. It is my meditation all day.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Your commandments make me wiser than my enemies, for your commandments are always with me.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
I have more understanding than all my teachers, for your testimonies are my (meditation)
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
I understand more than the aged, because I have kept your precepts.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
I have kept my feet from every evil way, that I might observe your word.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
I have not turned aside from your ordinances, for you have taught me.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
How sweet are your promises to my taste, more than honey to my mouth.
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Through your precepts, I get understanding; therefore I hate every false way.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
NUN. Your word is a lamp to my feet, and a light for my path.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
I have sworn, and have confirmed it, that I will obey your righteous ordinances.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
I am afflicted very much. Revive me, LORD, according to your word.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Please accept the freewill offerings of my mouth, LORD, and teach me your ordinances.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
My soul is continually in my hand, yet I won't forget your Law.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
The wicked have laid a snare for me, yet I haven't gone astray from your precepts.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
I have taken your testimonies as a heritage forever, for they are the joy of my heart.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
I have set my heart to perform your statutes forever, even to the end.
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
SAMEKH. I hate double-minded men, but I love your Law.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
You are my hiding place and my shield. I hope in your word.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Depart from me, you evildoers, that I may keep the commandments of my God.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Uphold me according to your word, that I may live. Let me not be ashamed of my hope.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Hold me up, and I will be safe, and will have respect for your statutes continually.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
You reject all those who stray from your statutes, for their deceit is in vain.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
You put away all the wicked of the earth like dross. Therefore I love your testimonies.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
My flesh trembles for fear of you. I am afraid of your judgments.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
AYIN. I have done what is just and righteous. Do not leave me to my oppressors.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Ensure your servant's well-being. Do not let the proud oppress me.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
My eyes fail looking for your salvation, for your righteous word.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Deal with your servant according to your loving kindness. Teach me your statutes.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
I am your servant. Give me understanding, that I may know your testimonies.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
It is time to act, LORD, for they break your Law.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Therefore I love your commandments more than gold, yes, more than pure gold.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Therefore I consider all of your precepts to be right. I hate every false way.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
PEY. Your testimonies are wonderful, therefore my soul keeps them.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
The entrance of your words gives light. It gives understanding to the simple.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
I opened my mouth wide and panted, for I longed for your commandments.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Turn to me, and have mercy on me, as you always do to those who love your name.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Establish my footsteps in your word. Do not let any iniquity have dominion over me.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Redeem me from the oppression of man, so I will observe your precepts.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Make your face shine on your servant. Teach me your statutes.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Streams of tears run down my eyes, because they do not observe your Law.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
TZADE. You are righteous, LORD. Your judgments are upright.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
You have commanded your statutes in righteousness. They are fully trustworthy.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
My zeal wears me out, because my enemies ignore your words.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Your promises have been thoroughly tested, and your servant loves them.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
I am small and despised. I do not forget your precepts.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Your righteousness is an everlasting righteousness. Your Law is truth.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Trouble and anguish have taken hold of me. Your commandments are my delight.
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Your testimonies are righteous forever. Give me understanding, that I may live.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
QOPH. I have called with my whole heart. Answer me, LORD. I will keep your statutes.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
I have called to you. Save me. I will obey your statutes.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
I rise before dawn and cry for help. I put my hope in your words.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
My eyes stay open through the night watches, that I might meditate on your word.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Hear my voice according to your loving kindness. Revive me, LORD, according to your ordinances.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
They draw near who follow after wickedness. They are far from your Law.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
You are near, LORD. All your commandments are truth.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Of old I have known from your testimonies, that you have founded them forever.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
RESH. Consider my affliction, and deliver me, for I do not forget your Law.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Plead my cause, and redeem me. Revive me according to your promise.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Salvation is far from the wicked, for they do not seek your statutes.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Great are your tender mercies, LORD. Revive me according to your ordinances.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Many are my persecutors and my adversaries. I haven't swerved from your testimonies.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
I look at the faithless with loathing, because they do not observe your word.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Consider how I love your precepts. Revive me, LORD, according to your loving kindness.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
All of your words are truth. Every one of your righteous ordinances endures forever.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
SIN and SHIN. Princes have persecuted me without a cause, but my heart stands in awe of your words.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
I rejoice at your word, as one who finds great spoil.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
I hate and abhor falsehood. I love your Law.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Seven times a day, I praise you, because of your righteous ordinances.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Those who love your Law have great peace. Nothing causes them to stumble.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
I have hoped for your salvation, LORD. I have done your commandments.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
My soul has observed your testimonies. I love them exceedingly.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
I have obeyed your precepts and your testimonies, for all my ways are before you.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
TAW. Let my cry come before you, LORD. Give me understanding according to your word.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Let my petition come before you. Deliver me according to your word.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Let my lips utter praise, for you teach me your statutes.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Let my tongue sing of your word, for all your commandments are righteousness.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Let your hand be ready to help me, for I have chosen your precepts.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
I have longed for your salvation, LORD. Your Law is my delight.
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
Let my soul live, that I may praise you. Let your ordinances help me.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
I have gone astray like a lost sheep. Seek your servant, for I do not forget your commandments.

< Masalimo 119 >