< Masalimo 119 >

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa, amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
Alleluia. Blessed are the blameless in the way, who walk in the law of the Lord.
2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake, amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
Blessed are they that search out his testimonies: they will diligently seek him with the whole heart.
3 Sachita cholakwa chilichonse; amayenda mʼnjira zake.
For they that work iniquity have not walked in his ways.
4 Inu mwapereka malangizo ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
Thou hast commanded [us] diligently to keep thy precepts.
5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika pa kumvera zophunzitsa zanu!
O that my ways were directed to keep thine ordinances.
6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi, poganizira malamulo anu onse.
Then shall I not be ashamed, when I have respect to all thy commandments.
7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama, pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
I will give thee thanks with uprightness of heart, when I have learnt the judgments of thy righteousness.
8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu; musanditaye kwathunthu.
I will keep thine ordinances: O forsake me not greatly.
9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake? Akawasamala potsata mawu anu.
Wherewith shall a young man direct his way? by keeping thy words.
10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse; musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
With my whole heart have I diligently sought thee: cast me not away from thy commandments.
11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga kuti ndisakuchimwireni.
I have hidden thine oracles in my heart, that I might not sin against thee.
12 Mutamandike Inu Yehova; phunzitseni malamulo anu.
Blessed art thou, O Lord: teach me thine ordinances.
13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse amene amachokera pakamwa panu.
With my lips have I declared all the judgments of thy mouth.
14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
I have delighted in the way of thy testimonies, [as much] as in all riches.
15 Ndimalingalira malangizo anu ndipo ndimaganizira njira zanu.
I will meditate on thy commandments, and consider thy ways.
16 Ndimakondwera ndi malamulo anu; sindidzayiwala konse mawu anu.
I will meditate on thine ordinances: I will not forget thy words.
17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; kuti tsono ndisunge mawu anu.
Render a recompense to thy servant: [so] shall I live, and keep thy words.
18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
Unveil thou mine eyes, and I shall perceive wondrous things of thy law.
19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; musandibisire malamulo anu.
I am a stranger in the earth: hide not thy commandments from me.
20 Moyo wanga wafowoka polakalaka malamulo anu nthawi zonse.
My soul has longed exceedingly for thy judgments at all times.
21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa, amene achoka pa malamulo anu.
Thou has rebuked the proud: cursed are they that turn aside from thy commandments.
22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo pakuti ndimasunga malamulo anu.
Remove from me reproach and contempt; for I have sought out thy testimonies.
23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza, mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
For princes sat and spoke against me: but thy servant was meditating on thine ordinances.
24 Malamulo anu amandikondweretsa; ndiwo amene amandilangiza.
For thy testimonies are my (meditation) and thine ordinances are my counsellors.
25 Moyo wanga wakangamira fumbi; tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
My soul has cleaved to the ground; quicken thou me according to thy word.
26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha; phunzitseni malamulo anu.
I declared my ways, and thou didst hear me: teach me thine ordinances.
27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu; pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
Instruct me in the way of thine ordinances; and I will meditate on thy wondrous works.
28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni; limbikitseni monga mwa mawu anu.
My soul has slumbered for sorrow; strengthen thou me with thy words.
29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo; mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
Remove from me the way of iniquity; and be merciful to me by thy law.
30 Ndasankha njira ya choonadi; ndayika malamulo anu pa mtima panga.
I have chosen the way of truth; and have not forgotten thy judgments.
31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
I have cleaved to thy testimonies, O Lord; put me not to shame.
32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu, pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
I ran the way of thy commandments, when thou didst enlarge my heart.
33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu; ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
Teach me, O Lord, the way of thine ordinances, and I will seek it out continually.
34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
Instruct me, and I will search out thy law, and will keep it with my whole heart.
35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu, pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
Guide me in the path of thy commandments; for I have delighted in it.
36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu, osati chuma.
Incline mine heart to thy testimonies, and not to covetousness.
37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe; sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
Turn away mine eyes that I may not behold vanity: quicken thou me in thy way.
38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu, kuti Inu muopedwe.
Confirm thine oracle to thy servant, that he may fear thee.
39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa, pakuti malamulo anu ndi abwino.
Take away my reproach which I have feared: for thy judgments are good.
40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu! Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Behold, I have desired thy commandments: quicken me in thy righteousness.
41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova, chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
And let thy mercy come upon me, O Lord; [even] thy salvation, according to thy word.
42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza, popeza ndimadalira mawu anu.
And [so] I shall render an answer to them that reproach me: for I have trusted in thy words.
43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga, pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
And take not the word of truth utterly out of my mouth; for I have hoped in thy judgments. So shall I keep thy law continually, for ever and ever.
44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse, ku nthawi za nthawi.
45 Ndidzayendayenda mwaufulu, chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
I walked also at large: for I sought out thy commandments.
46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
And I spoke of thy testimonies before kings, and was not ashamed.
47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu chifukwa ndimawakonda.
And I meditated on thy commandments, which I loved exceedingly.
48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda, ndipo ndimalingalira malangizo anu.
And I lifted up my hands to thy commandments which I loved; and I meditated in thine ordinances.
49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu, popeza mwandipatsa chiyembekezo.
Remember thy words to thy servant, wherein thou hast made me hope.
50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi: lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
This has comforted me in mine affliction: for thine oracle has quickened me.
51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa, koma sindichoka pa malamulo anu.
The proud have transgressed exceedingly; but I swerved not from thy law.
52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale, ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
I remembered thy judgments of old, O Lord; and was comforted.
53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa amene ataya malamulo anu.
Despair took hold upon me, because of the sinners who forsake thy law.
54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga kulikonse kumene ndigonako.
Thine ordinances were my songs in the place of my sojourning.
55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova, ndipo ndidzasunga malamulo anu.
I remembered thy name, O Lord, in the night, and kept thy law.
56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita: ndimasunga malangizo anu.
This I had, because I diligently sought thine ordinances.
57 Yehova, Inu ndiye gawo langa; ndalonjeza kumvera mawu anu.
Thou art my portion, O Lord: I said that I would keep thy law.
58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse; mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
I besought thy favour with my whole heart: have mercy upon me according to thy word.
59 Ndinalingalira za njira zanga ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
I thought on thy ways, and turned my feet to thy testimonies.
60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza kumvera malamulo anu.
I prepared myself, (and was not terrified, ) to keep thy commandments.
61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe, sindidzayiwala lamulo lanu.
The snares of sinners entangled me: but I forgot not thy law.
62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu chifukwa cha malamulo anu olungama.
At midnight I arose, to give thanks to thee for the judgments of thy righteousness.
63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani, kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
I am a companion of all them that fear thee, and of them that keep thy commandments.
64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika, phunzitseni malamulo anu.
O Lord, the earth is full of thy mercy: teach me thine ordinances.
65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu molingana ndi mawu anu.
Thou hast wrought kindly with thy servant, o Lord, according to thy word.
66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino, pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
Teach me kindness, and instruction, and knowledge: for I have believed thy commandments.
67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera, koma tsopano ndimamvera mawu anu.
Before I was afflicted, I transgressed; therefore have I kept thy word.
68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino; phunzitseni malamulo anu.
Good art thou, O Lord; therefore in thy goodness teach me thine ordinances.
69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza, ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
The injustice of the proud has been multiplied against me: but I will search out thy commandments with all my heart.
70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa, koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
Their heart has been curdled like milk; but I have meditated on thy law.
71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
[It is] good for me that thou hast afflicted me; that I might learn thine ordinances.
72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
The law of thy mouth is better to me than thousands of gold and silver.
73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
Thy hands have made me, and fashioned me: instruct me, that I may learn thy commandments.
74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona, chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
They that fear thee will see me and rejoice: for I have hoped in thy words.
75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
I know, O Lord, that thy judgments are righteousness, and [that] thou in truthfulness hast afflicted me.
76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa, molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
Let, I pray thee, thy mercy be to comfort me, according to thy word to thy servant.
77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo, popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
Let thy compassions come to me, that I may live: for thy law is my (meditation)
78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa; koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
Let the proud be ashamed; for they transgressed against me unjustly: but I will meditate in thy commandments.
79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine, iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
Let those that fear thee, and those that know thy testimonies, turn to me.
80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu kuti ndisachititsidwe manyazi.
Let mine heart be blameless in thine ordinances, that I may not be ashamed.
81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu, koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
My soul faints for thy salvation: I have hoped in thy words.
82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu; Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
Mine eyes failed [in waiting] for thy word, saying, When wilt thou comfort me?
83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi sindiyiwala zophunzitsa zanu.
For I am become as a bottle in the frost: [yet] I have not forgotten thine ordinances.
84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti? Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
How many are the days of thy servant? when wilt thou execute judgment for me on them that persecute me?
85 Anthu osalabadira za Mulungu, odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
Transgressors told me [idle tales]; but not according to thy law, O Lord.
86 Malamulo anu onse ndi odalirika; thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
All thy commandments are truth; they persecuted me unjustly; help thou me.
87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi koma sindinataye malangizo anu.
They nearly made an end of me in the earth; but I forsook not thy commandments.
88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Quicken me according to thy mercy; so shall I keep the testimonies of thy mouth.
89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya; akhazikika kumwambako.
Thy word, O Lord, abides in heaven for ever.
90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse; Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
Thy truth [endures] to all generations; thou hast founded the earth, and it abides.
91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino, pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
The day continues by thy arrangement; for all things are thy servants.
92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa, ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
Were it not that thy law is my (meditation) then I should have perished in mine affliction.
93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu, pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
I will never forget thine ordinances; for with them thou hast quickened me.
94 Ndine wanu, ndipulumutseni; pakuti ndasamala malangizo anu.
I am thine, save me; for I have sought out thine ordinances.
95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge, koma ndidzalingalira umboni wanu.
Sinners laid wait for me to destroy me; [but] I understood thy testimonies.
96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire, koma malamulo anu alibe malire konse.
have seen an end of all perfection; [but] thy commandment is very broad.
97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu! Ndimalingaliramo tsiku lonse.
How I have loved thy law, O Lord! it is my meditation all the day.
98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga, popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
Thou hast made me wiser than mine enemies [in] thy commandment; for it is mine for ever.
99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse popeza ndimalingalira umboni wanu.
I have more understanding than all my teachers; for thy testimonies are my medication.
100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba, popeza ndimamvera malangizo anu.
I understand more that the aged; because I have sought out thy commandments.
101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa kuti ndithe kumvera mawu anu.
I have kept back my feet from every evil way, that I might keep thy words.
102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu, pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
I have not declined from thy judgments; for thou hast instructed me.
103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa, otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
How sweet are thine oracles to my throat! more so than honey to my mouth!
104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu; kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
I gain understanding by thy commandments: therefore I have hated every way of unrighteousness.
105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
Thy law is a lamp to my feet, and a light to my paths.
106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza, kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
I have sworn and determined to keep the judgments of thy righteousness.
107 Ndazunzika kwambiri; Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
I have been very greatly afflicted, O Lord: quicken me, according to thy word.
108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga, ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
Accept, I pray thee, O Lord, the freewill-offerings of my mouth, and teach me thy judgments.
109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi, sindidzayiwala malamulo anu.
My soul is continually in thine hands; and I have not forgotten thy law.
110 Anthu oyipa anditchera msampha, koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
Sinners spread a snare for me; but I erred not from thy commandments.
111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya; Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
I have inherited thy testimonies for ever; for they are the joy of my heart.
112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu mpaka kumapeto kwenikweni.
I have inclined my heart to perform thine ordinances for ever, in return [for thy mercies].
113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri, koma ndimakonda malamulo anu.
I have hated transgressors; but I have loved thy law.
114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
Thou art my helper and my supporter; I have hoped in thy words.
115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa, kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
Depart from me, ye evil-doers; for I will search out the commandments of my God.
116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo; musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
Uphold me according to thy word, and quicken me; and make me not ashamed of my expectation.
117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa; nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
Help me, and I shall be saved; and I will meditate in thine ordinances continually.
118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu, pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
Thou hast brought to nought all that depart from thine ordinances; for their inward thought is unrighteous.
119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala; nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
I have reckoned all the sinners of the earth as transgressors; therefore have I loved thy testimonies.
120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu; ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Penetrate my flesh with thy fear; for I am afraid of thy judgments.
121 Ndachita zolungama ndi zabwino; musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
I have done judgment and justice; deliver me not up to them that injure me.
122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino, musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
Receive thy servant for good: let not the proud accuse me falsely.
123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu, kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
Mine eyes have failed for thy salvation, and for the word of thy righteousness.
124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika, ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Deal with thy servant according to thy mercy, and teach me thine ordinances.
125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa, kuti ndimvetsetse umboni wanu.
I am thy servant; instruct me, and I shall know thy testimonies.
126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu; malamulo anu akuswedwa.
[It is] time for the Lord to work: they have utterly broken thy law.
127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
Therefore have I loved thy commandments more than gold, or the topaz.
128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka, ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Therefore I directed myself [according] to all thy commandments: I have hated every unjust way.
129 Maumboni anu ndi odabwitsa nʼchifukwa chake ndimawamvera.
Thy testimonies are wonderful: therefore my soul has sought them out.
130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika; ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
The manifestation of thy words will enlighten, and instruct the simple.
131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu, kufunafuna malamulo anu.
I opened my mouth, and drew breath: for I earnestly longed after thy commandments.
132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo, monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
Look upon me and have mercy upon me, after the manner of them that love thy name.
133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu; musalole kuti tchimo lizindilamulira.
Order my steps according to thy word: and let not any iniquity have dominion over me.
134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza, kuti ndithe kumvera malangizo anu.
Deliver me from the false accusation of men: so will I keep thy commandments.
135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
Cause thy face to shine upon thy servant: and teach me thine ordinances.
136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga, chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Mine eyes have been bathed in streams of water, because I kept not thy law.
137 Yehova ndinu wolungama, ndipo malamulo anu ndi abwino.
Righteous art thou, O Lord, and upright are thy judgments.
138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama; ndi odalirika ndithu.
Thou has commanded righteousness and perfect truth, [as] thy testimonies.
139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
Thy zeal has quite wasted me: because mine enemies have forgotten thy words.
140 Mawu anu ndi woyera kwambiri nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
Thy word [has been] very fully tried; and thy servant loves it.
141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka, sindiyiwala malangizo anu.
I am young and despised: [yet] I have not forgotten thine ordinances.
142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya, ndipo malamulo anu nʼchoona.
Thy righteousness is an everlasting righteousness, and thy law is truth.
143 Mavuto ndi masautso zandigwera, koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
Afflictions and distresses found me: [but] thy commandments [were] my (meditation)
144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse; patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Thy testimonies [are] an everlasting righteousness: instruct me, and I shall live.
145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova, ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
I cried with my whole heart; hear me, O Lord: I will search out thine ordinances.
146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni ndipo ndidzasunga umboni wanu.
I cried to thee; save me, and I will keep thy testimonies.
147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo; chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
I arose before the dawn, and cried: I hoped in thy words.
148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku, kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
Mine eyes prevented the dawn, that I might meditate on thine oracles.
149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
Hear my voice, O Lord, according to thy mercy; quicken me according to thy judgment.
150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira, koma ali kutali ndi malamulo anu.
They have drawn nigh who persecuted me unlawfully; and they are far removed from thy law.
151 Koma Inu Yehova muli pafupi, malamulo anu onse ndi woona.
Thou art near, O Lord; and all thy ways are truth.
152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
I have known of old concerning thy testimonies, that thou hast founded them for ever.
153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Look upon mine affliction, and rescue me; for I have not forgotten thy law.
154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola; sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
Plead my cause, and ransom me: quicken me because of thy word.
155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa, pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
Salvation is far from sinners: for they have not searched out thine ordinances.
156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu; sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
Thy mercies, O Lord, are many: quicken me according to thy judgment.
157 Adani amene akundizunza ndi ambiri, koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
Many are they that persecute me and oppress me: [but] I have not declined from thy testimonies.
158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro, popeza samvera mawu anu.
I beheld men acting foolishly, and I pined away; for they kept not thine oracles.
159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu; sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
Behold, I have loved thy commandments, O Lord: quicken me in thy mercy.
160 Mawu anu onse ndi owona; malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
The beginning of thy words is truth; and all the judgments of thy righteousness [endure] for ever.
161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa, koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
Princes persecuted me without a cause, but my heart feared because of thy words.
162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu, ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
I will exult because of thine oracles, as one that finds much spoil.
163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho, koma ndimakonda malamulo anu.
I hate and abhor unrighteousness; but I love thy law.
164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku pakuti malamulo anu ndi olungama.
Seven times in a day have I praised thee because of the judgments of thy righteousness.
165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu, ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
Great peace have they that love thy law: and there is no stumbling-block to them.
166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova, ndipo ndimatsatira malamulo anu.
I waited for thy salvation, O Lord, and have loved thy commandments.
167 Ndimamvera umboni wanu pakuti ndimawukonda kwambiri.
My soul has kept thy testimonies, and loved them exceedingly.
168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu, pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
I have kept thy commandments and thy testimonies; for all my ways are before thee, O Lord.
169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova; patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
Let my supplication come near before thee, o Lord; instruct me according to thine oracle.
170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu; pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
Let my petition come in before thee, O Lord; deliver me according to thine oracle.
171 Matamando asefukire pa milomo yanga, pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
Let my lips utter a hymn, when thou shalt have taught me thine ordinances.
172 Lilime langa liyimbe mawu anu, popeza malamulo anu onse ndi olungama.
Let my tongue utter thine oracles; for all thy commandments are righteous.
173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza pakuti ndasankha malangizo anu.
Let thine hand be [prompt] to save me; for I have chosen thy commandments.
174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova, ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
I have longed after thy salvation, O Lord; and thy law is my (meditation)
175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni, ndipo malamulo anu andichirikize.
My soul shall live, and shall praise thee; and thy judgments shall help me.
176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika, funafunani mtumiki wanu, pakuti sindinayiwale malamulo anu.
I have gone astray like a lost sheep; seek thy servant; for I have not forgotten thy commandments.

< Masalimo 119 >