< Masalimo 114 >

1 Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
When Israel went forth out of Egypt, the house of Jacob from a people of strange language,
2 Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
Judah became his sanctuary, Israel his dominion.
3 Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
The sea saw it, and fled. The Jordan was driven back.
4 mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
The mountains skipped like rams, the little hills like lambs.
5 Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
What ails thee, O thou sea, that thou flee? Thou Jordan, that thou turn back?
6 inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
Ye mountains, that ye skip like rams, ye little hills, like lambs?
7 Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
Tremble, thou earth, at the presence of the Lord, at the presence of the God of Jacob,
8 amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.
who turned the rock into a pool of water, the flint into a fountain of waters.

< Masalimo 114 >