< Masalimo 104 >

1 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
Bless Jehovah, O my soul. O Jehovah my God, thou are very great. Thou are clothed with honor and majesty,
2 Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
who covers thyself with light as with a garment, who stretches out the heavens like a curtain,
3 ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
who lays the beams of his chambers in the waters, who makes the clouds his chariot, who walks upon the wings of the wind,
4 Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
who makes his agents spirits, his ministers a flame of fire,
5 Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
who laid the foundations of the earth that it should not be moved forever.
6 Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
Thou covered it with the deep as with a vesture. The waters stood above the mountains.
7 Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
At thy rebuke they fled. At the voice of thy thunder they hastened away.
8 Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
The mountains rose, the valleys sank down to the place which thou had founded for them.
9 Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
Thou have set a bound that they may not pass over, that they turn not again to cover the earth.
10 Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
He sends forth springs into the valleys. They run among the mountains.
11 Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
They give drink to every beast of the field. The wild donkeys quench their thirst.
12 Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
By them the birds of the heavens have their habitation. They sing among the branches.
13 Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
He waters the mountains from his chambers. The earth is filled with the fruit of thy works.
14 Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
He causes the grass to grow for the cattle, and herbage for the service of man, that he may bring forth food out of the earth,
15 vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
and wine that makes glad the heart of man, and oil to make his face to shine, and bread that strengthens man's heart.
16 Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
The trees of Jehovah are full, the cedars of Lebanon, which he has planted,
17 Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
where the birds make their nests. As for the stork, the fir trees are her house.
18 Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
The high mountains are for the wild goats. The rocks are a refuge for the conies.
19 Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
He appointed the moon for seasons. The sun knows his going down.
20 Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
Thou make darkness, and it is night, during which all the beasts of the forest creep forth.
21 Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
The young lions roar after their prey, and seek their food from God.
22 Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
The sun arises; they get away, and lie down in their dens.
23 Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
Man goes forth to his work and to his labor until the evening.
24 Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
O Jehovah, how manifold are thy works! In wisdom have thou made them all. The earth is full of thy riches.
25 Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
Yonder is the sea, great and wide, in which are innumerable creeping things, both small and great beasts.
26 Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
There go the ships. There is leviathan, whom thou have formed to play in it.
27 Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
These all wait for thee, that thou may give them their food in due season.
28 Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
Thou give to them, they gather. Thou open thy hand, they are satisfied with good.
29 Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
Thou hide thy face, they are troubled. Thou take away their breath, they die, and return to their dust.
30 Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
Thou send forth thy Spirit, they are created, and thou renew the face of the ground.
31 Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
Let the glory of Jehovah endure forever. Let Jehovah rejoice in his works,
32 Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
who looks on the earth, and it trembles. He touches the mountains, and they smoke.
33 Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
I will sing to Jehovah as long as I live. I will sing praise to my God while I have any being.
34 Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
Let thy meditation be sweet to him. I will rejoice in Jehovah.
35 Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.
Let sinners be consumed out of the earth, and let the wicked be no more. Bless Jehovah, O my soul. Praise ye Jehovah.

< Masalimo 104 >