< Masalimo 102 >

1 Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
Hear my prayer, O Jehovah, and let my cry come to thee.
2 Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
Hide not thy face from me in the day of my distress. Incline thine ear to me. In the day when I call answer me speedily.
3 Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
For my days consume away like smoke, and my bones are burned as a firebrand.
4 Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
My heart is smitten like grass, and withered, for I forget to eat my bread.
5 Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
Because of the voice of my groaning my bones cling to my flesh.
6 Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
I am like a pelican of the wilderness. I have become as an owl of the waste places.
7 Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
I watch, and have become like a sparrow that is alone upon the house-top.
8 Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
My enemies reproach me all the day. Those who are mad against me do curse by me.
9 Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
For I have eaten ashes like bread, and mingled my drink with weeping,
10 chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
because of thine indignation and thy wrath. For thou have taken me up, and cast me away.
11 Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
My days are like a shadow that declines, and I am withered like grass.
12 Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
But thou, O Jehovah, will abide forever, and thy memorial to all generations.
13 Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
Thou will arise, and have mercy upon Zion, for it is time to have pity upon her, yea, the set time has come.
14 Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
For thy servants take pleasure in her stones, and have pity upon her dust.
15 Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
So the nations shall fear the name of Jehovah, and all the kings of the earth thy glory.
16 Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
For Jehovah has built up Zion. He has appeared in his glory.
17 Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
He has regarded the prayer of the destitute, and has not despised their prayer.
18 Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
This shall be written for the generation to come. And a people which shall be created shall praise Jehovah.
19 “Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
For he has looked down from the height of his sanctuary. From heaven Jehovah beheld the earth,
20 kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
to hear the sighing of the prisoner, to loose those who are appointed to death,
21 Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
that men may declare the name of Jehovah in Zion, and his praise in Jerusalem,
22 pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
when the peoples are gathered together, and the kingdoms, to serve Jehovah.
23 Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
He weakened my strength in the way. He shortened my days.
24 Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
I said, O my God, take me not away in the midst of my days. Thy years are throughout all generations.
25 Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
Of old thou laid the foundation of the earth, and the heavens are the work of thy hands.
26 Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
They shall perish, but thou shall endure. Yea, all of them shall grow old like a garment. As a vesture thou shall change them, and they shall be changed,
27 Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
but thou are the same, and thy years shall have no end.
28 Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”
The sons of thy servants shall continue, and their seed shall be established before thee.

< Masalimo 102 >