< Miyambo 3 >

1 Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
Ka capa, kak awipek ve koeh hilh nawh, nak kawlung awh kym lah.
2 Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
Na hqingnaak khawnghii khawkum ingkaw ngaiqeepnaakkhqi ing ni tawmsap kaw.
3 Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
Qeennaak ingkaw awitak ing nang ce koeh ni hooet seh.
4 Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
Cawhtaw, Khawsa ingkaw thlanghqing mik huh awh mikhaileek ingkaw mingleeknaak ce pang kawp ti.
5 Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
Nak kawlung boeih ing Bawipa ce caang na nawh, Na siimnaak awh koeh hang qu;
6 Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
Na lam hoeiawh amah ce siim poe nawh, na lam ce nim huh kaw.
7 Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
Namah ngaih awh ak cyina koeh ngai qu nawh; Bawipa ce kqih nawh, thawlhnaak ce cehtaak.
8 Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
Nak thangqui ham sadingnaak na awm nawh, na quh ham ak thlikna awm kaw.
9 Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
Na khawhkham ing Khawsa ce kyihcah lah. Na them ak pung law lammacyk boeih ing awm;
10 Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
Cawhtaw nak khai baawp ing bee ngen kawm saw, na misur um ing bee poeng kaw.
11 Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
Ka capa, Bawipa a toelnaak ce koeh husit nawh, A ni toelzyihnaak ce koeh zadam kawp ti.
12 Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
Bawipa ing a lungnak cekhqi ce toel khawi nawh, Pa ing ca a lungnak awh a toelzyih khawi a myihna.
13 Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
Cyihnaak ak hu ak thlang ingkaw kawcyihnaak ak hu ak thlang taw a zoseen hy.
14 pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
Cetaw ngun a phu tlo ingkaw sui a phu tlo ang lakawh a phu tlo ngai hy.
15 Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
Suilung a phu tlo lakawh a phu tlo ngai nawh ngaihnaak ing awm am pha thai hy.
16 Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
Ak tangkut benawh hqinglung sangnaak awm nawh, ak cawngkut benawh khawhthem ingkaw boeimangnaak ce awm hy.
17 Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
A lam ce awmhlynaak lampyina awm nawh, a lam boeihboeih ce ngaiqeepnaak ing bee hy.
18 Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
Ak tuu thlang boeih ham hqingnaak thingkungna awm nawh, ak kym thlang boeih ham zoseennaak ni.
19 Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
Bawipa ing a cyihnaak ing khawmdek ve syyn nawh, ak kawcyih ing khan ce caksak hy;
20 Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
A thoemnaak ing tuinu ce hqaa sak nawh, cingmai ing daamtui baw sak hy.
21 Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
Ka capa, na mik ing khaw koeh hang seh, cyihnaak ingkaw khawkpoek thainaak ce ak cakna tu;
22 Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
Na hqingnaak ham hqingnaakna awm nawh, na haawng ham mikhaileek na awm kaw.
23 Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
Cawhce na lamawh ak dingna cet kawm tik saw, na khaw am tawngtawh kaw.
24 pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
Na ih awm am kqih kawm tik saw, nang zaih nawh na ih awhawm na ih tui kaw.
25 Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
Kqihlyynaak bawtbet awh ak dang law ce koeh kqih nawh, thlang ak mukkhqi a pha law awhawm koeh kqih kawp ti.
26 pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
Bawipa taw na loetnaak na awm nawh, na khaw thang awhkawng ni doen kaw.
27 Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
Themleek ak hu tyngkhqi a do hly kawi themleek koeh haimah, na kutawh dangsak ham na taak khui taw.
28 Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
Na imceng venawh, “Ceh nawh ak changna va sui cang nawh voei law tlaih khawngawi ni pe kawng nyng,” koeh ti, na taak a loeiawh.
29 Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
Na imceng ak khanawh khawboeseet koeh toen, ni yp na nawh na venawh khawksa ni ti na sim loei.
30 Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
Khawboeseetnaak nak khanawh a ma toen awhtaw leehcaihnaak a awm kaana na kut koeh thlak.
31 Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
Khawboeseet ak toen ak thlang koeh ooet nawh a lampyi awh koeh hquut.
32 Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
Ak thymna khaw amak sa taw Bawipa mikhuh awh tyih kawina awm nawh thlakleekkhqi taw pyi nak khqi hy.
33 Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
Bawipa a khawsii taw thlakche khqi imawh awm nawh, thlakdyng khqi cunnaak taw zoseenaak ing bee hy.
34 Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
Thlang ak husitkhqi ce husitkhqi nawh, kawkneemkhqi ce qeennaak ham sak khqi hy.
35 Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.
Kyihcahnaak taw thlakcyi ing ham nawh chahpyihnaak taw thlakqaw ing ham kaw.

< Miyambo 3 >