< Numeri 7 >

1 Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
And when Moses had put up the House completely, and had put oil on it and made it holy, with all the things in it, and had made the altar and all its vessels holy with oil;
2 Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
Then the chiefs of Israel, the heads of their fathers' houses, made offerings; these were the chiefs of the tribes, who were over those who were numbered.
3 Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
And they came with their offerings before the Lord, six covered carts and twelve oxen; a cart for every two of the chiefs, and for every one an ox.
4 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord said to Moses,
5 “Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
Take the things from them, to be used for the work of the Tent of meeting; and give them to the Levites, to every man what is needed for his work.
6 Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
So Moses took the carts and the oxen and gave them to the Levites.
7 Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
Two carts and four oxen he gave to the sons of Gershon for their work;
8 ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
And four carts and eight oxen he gave to the sons of Merari for their work, under the direction of Ithamar, the son of Aaron the priest.
9 Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
But to the sons of Kohath he gave nothing; because they had the care of the holy place, taking it about on their backs.
10 Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
And the chiefs gave an offering for the altar on the day when the holy oil was put on it; they made their offering before the altar.
11 Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
And the Lord said to Moses, Let every chief on his day give his offering to make the altar holy.
12 Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
And he who made his offering on the first day was Nahshon, the son of Amminadab, of the tribe of Judah:
13 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
And his offering was one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
14 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice for burning;
15 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
16 mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
17 ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Nahshon, the son of Amminadab.
18 Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
On the second day Nethanel, the son of Zuar, chief of Issachar, made his offering:
19 Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
He gave one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
20 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
21 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
22 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
23 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Nethanel, the son of Zuar.
24 Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
On the third day Eliab, the son of Helon, chief of the children of Zebulun:
25 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
His offering was one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
26 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
27 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
28 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
29 ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Eliab, the son of Helon.
30 Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
On the fourth day Elizur, the son of Shedeur, chief of the children of Reuben:
31 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
His offering was one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
32 Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
33 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
34 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
35 ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Elizur, the son of Shedeur.
36 Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
On the fifth day Shelumiel, the son of Zurishaddai, chief of the children of Simeon:
37 Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
His offering was one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
38 mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
39 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
40 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
41 ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Shelumiel, the son of Zurishaddai.
42 Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
On the sixth day Eliasaph, the son of Reuel, chief of the children of Gad:
43 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
His offering was one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
44 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
45 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
46 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
47 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Eliasaph, the son of Reuel
48 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
On the seventh day Elishama, the son of Ammihud, chief of the children of Ephraim:
49 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
His offering was one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
50 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
51 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
52 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
53 ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Elishama, the son of Ammihud.
54 Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
On the eighth day Gamaliel, the son of Pedahzur, chief of the children of Manasseh:
55 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
His offering was one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
56 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
57 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
58 mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
59 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Gamaliel, the son of Pedahzur.
60 Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
On the ninth day Abidan, the son of Gideoni, chief of the children of Benjamin:
61 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
His offering was one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
62 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
63 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year for a burned offering;
64 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
65 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Abidan, the son of Gideoni.
66 Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
On the tenth day Ahiezer; the son of Ammishaddai, chief of the children of Dan:
67 Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
His offering was one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
68 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
69 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
70 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
71 ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Ahiezer, the son of Ammishaddai.
72 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
On the eleventh day Pagiel, the son of Ochran, chief of the children of Asher:
73 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
His offering was one silver plate; a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
74 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
75 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
76 mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
77 ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Pagiel, the son of Ochran.
78 Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
On the twelfth day Ahira, the son of Enan, chief of the children of Naphtali:
79 Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
His offering was one silver plate, a hundred and thirty shekels in weight, one silver basin of seventy shekels, by the scale of the holy place; the two of them full of the best meal mixed with oil for a meal offering;
80 mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
One gold spoon of ten shekels, full of spice;
81 mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
One young ox, one male sheep, one he-lamb of the first year, for a burned offering;
82 mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
One male of the goats for a sin-offering;
83 ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
And for the peace-offerings, two oxen, five male sheep, five he-goats, five he-lambs of the first year: this was the offering of Ahira, the son of Enan.
84 Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
These were the offerings given for the altar by the chiefs of Israel, when the holy oil was put on it: twelve silver plates, twelve silver basins, twelve gold spoons;
85 Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
The weight of every silver plate was a hundred and thirty shekels, and of every basin seventy; the weight of all the silver of the vessels was two thousand and four hundred shekels, by the scale of the holy place;
86 Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
The weight of the twelve gold spoons of spice for burning was ten shekels for every one, by the scale of the holy place; all the gold of the spoons was a hundred and twenty shekels;
87 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
All the oxen, for the burned offering were twelve, the male sheep twelve, the he-lambs of the first year twelve, with their meal offering; and the males of the goats for sin-offering twelve;
88 Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
And all the oxen for the peace-offerings, twenty-four oxen, the male sheep sixty, and the he-goats sixty, the he-lambs of the first year sixty. This was given for the altar after the holy oil was put on it.
89 Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.
And when Moses went into the Tent of meeting to have talk with him, then the Voice came to his ears from over the cover which was on the ark of witness, from between the two winged ones. And he had talk with him.

< Numeri 7 >