< Numeri 33 >

1 Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
These are the journeys of the sons of Israel when they went forth out of the land of Egypt by their armies under the hand of Moses and Aaron.
2 Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
And Moses wrote their goings out according to their journeys by the commandment of Jehovah. And these are their journeys according to their goings out.
3 Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
And they journeyed from Rameses in the first month, on the fifteenth day of the first month. On the morrow after the Passover the sons of Israel went out with a high hand in the sight of all the Egyptians,
4 pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
while the Egyptians were burying all their firstborn whom Jehovah had smitten among them; upon their gods also Jehovah executed judgments.
5 Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
And the sons of Israel journeyed from Rameses, and encamped in Succoth.
6 Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
And they journeyed from Succoth, and encamped in Etham, which is in the edge of the wilderness.
7 Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
And they journeyed from Etham, and turned back to Pihahiroth, which is before Baal-zephon, and they encamped before Migdol.
8 Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
And they journeyed from before Hahiroth, and passed through the midst of the sea into the wilderness. And they went three days' journey in the wilderness of Etham, and encamped in Marah.
9 Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
And they journeyed from Marah, and came to Elim. And in Elim were twelve springs of water, and seventy palm trees, and they encamped there.
10 Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
And they journeyed from Elim, and encamped by the Red Sea.
11 Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
And they journeyed from the Red Sea, and encamped in the wilderness of Sin.
12 Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
And they journeyed from the wilderness of Sin, and encamped in Dophkah.
13 Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
And they journeyed from Dophkah, and encamped in Alush.
14 Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
And they journeyed from Alush, and encamped in Rephidim, where was no water for the people to drink.
15 Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
And they journeyed from Rephidim, and encamped in the wilderness of Sinai.
16 Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
And they journeyed from the wilderness of Sinai, and encamped in Kibroth-hattaavah.
17 Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
And they journeyed from Kibroth-hattaavah, and encamped in Hazeroth.
18 Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
And they journeyed from Hazeroth, and encamped in Rithmah.
19 Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
And they journeyed from Rithmah, and encamped in Rimmon-perez.
20 Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
And they journeyed from Rimmon-perez, and encamped in Libnah.
21 Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
And they journeyed from Libnah, and encamped in Rissah.
22 Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
And they journeyed from Rissah, and encamped in Kehelathah.
23 Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
And they journeyed from Kehelathah, and encamped in mount Shepher.
24 Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
And they journeyed from mount Shepher, and encamped in Haradah.
25 Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
And they journeyed from Haradah, and encamped in Makheloth.
26 Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
And they journeyed from Makheloth, and encamped in Tahath.
27 Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
And they journeyed from Tahath, and encamped in Terah.
28 Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
And they journeyed from Terah, and encamped in Mithkah.
29 Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
And they journeyed from Mithkah, and encamped in Hashmonah.
30 Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
And they journeyed from Hashmonah, and encamped in Moseroth.
31 Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
And they journeyed from Moseroth, and encamped in Bene-jaakan.
32 Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
And they journeyed from Bene-jaakan, and encamped in Hor-haggidgad.
33 Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
And they journeyed from Hor-haggidgad, and encamped in Jotbathah.
34 Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
And they journeyed from Jotbathah, and encamped in Abronah.
35 Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
And they journeyed from Abronah, and encamped in Ezion-geber.
36 Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
And they journeyed from Ezion-geber, and encamped in the wilderness of Zin (the same is Kadesh).
37 Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
And they journeyed from Kadesh, and encamped at mount Hor, in the edge of the land of Edom.
38 Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
(And Aaron the priest went up onto mount Hor at the commandment of Jehovah, and died there, in the fortieth year after the sons of Israel came out of the land of Egypt, in the fifth month, on the first day of the month.
39 Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
And Aaron was a hundred and twenty-three years old when he died in mount Hor.
40 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
And the Canaanite, the king of Arad, who dwelt in the South in the land of Canaan, heard of the coming of the sons of Israel.)
41 Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
And they journeyed from mount Hor, and encamped in Zalmonah.
42 Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
And they journeyed from Zalmonah, and encamped in Punon.
43 Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
And they journeyed from Punon, and encamped in Oboth.
44 Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
And they journeyed from Oboth, and encamped in Iye-abarim, in the border of Moab.
45 Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
And they journeyed from Iyim, and encamped in Dibon-gad.
46 Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
And they journeyed from Dibon-gad, and encamped in Almon-diblathaim.
47 Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
And they journeyed from Almon-diblathaim, and encamped in the mountains of Abarim, before Nebo.
48 Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
And they journeyed from the mountains of Abarim, and encamped in the plains of Moab by the Jordan at Jericho.
49 Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
And they encamped by the Jordan, from Beth-jeshimoth even to Abel-shittim in the plains of Moab.
50 Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses in the plains of Moab by the Jordan at Jericho, saying,
51 “Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
Speak to the sons of Israel, and say to them, When ye pass over the Jordan into the land of Canaan,
52 mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
then ye shall drive out all the inhabitants of the land from before you, and destroy all their figured stones, and destroy all their molten images, and demolish all their high places.
53 Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
And ye shall take possession of the land, and dwell in it, for to you I have given the land to possess it.
54 Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
And ye shall inherit the land by lot according to your families. To the more ye shall give more inheritance, and to the few thou shall give less inheritance. Wherever the lot falls to any man, that shall be his. Ye shall inherit according to the tribes of your fathers.
55 “‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
But if ye will not drive out the inhabitants of the land from before you, then those that ye let remain of them shall be as pricks in your eyes, and as thorns in your sides, and they shall vex you in the land in which ye dwell.
56 Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’”
And it shall come to pass, that, as I thought to do to them, so I will do to you.

< Numeri 33 >