< Numeri 32 >

1 Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.
Now the sons of Reuben and the sons of Gad had a very great multitude of cattle. And when they saw the land of Jazer, and the land of Gilead, that, behold, the place was a place for cattle,
2 Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti,
the sons of Gad and the sons of Reuben came and spoke to Moses, and to Eleazar the priest, and to the rulers of the congregation, saying,
3 “Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,
Ataroth, and Dibon, and Jazer, and Nimrah, and Heshbon, and Elealeh, and Sebam, and Nebo, and Beon,
4 dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto.
the land which Jehovah smote before the congregation of Israel, is a land for cattle, and thy servants have cattle.
5 Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’”
And they said, If we have found favor in thy sight, let this land be given to thy servants for a possession. Bring us not over the Jordan.
6 Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?
And Moses said to the sons of Gad, and to the sons of Reuben, Shall your brothers go to the war, and shall ye sit here?
7 Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?
And why do ye discourage the heart of the sons of Israel from going over into the land which Jehovah has given them?
8 Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo.
Thus did your fathers when I sent them from Kadesh-barnea to see the land.
9 Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa.
For when they went up to the valley of Eshcol, and saw the land, they discouraged the heart of the sons of Israel, that they should not go into the land which Jehovah had given them.
10 Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti,
And Jehovah's anger was kindled in that day, and he swore, saying,
11 ‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
Surely none of the men who came up out of Egypt, from twenty years old and upward, shall see the land which I swore to Abraham, to Isaac, and to Jacob; because they have not wholly followed me,
12 Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’
except Caleb the son of Jephunneh the Kenizzite, and Joshua the son of Nun, because they have wholly followed Jehovah.
13 Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
And Jehovah's anger was kindled against Israel, and he made them wander to and fro in the wilderness forty years, until all the generation that had done evil in the sight of Jehovah was consumed.
14 “Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri.
And, behold, ye are risen up in your fathers' stead, an increase of sinful men, to augment yet the fierce anger of Jehovah toward Israel.
15 Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
For if ye turn away from after him, he will yet again leave them in the wilderness, and ye will destroy all this people.
16 Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.
And they came near to him, and said, We will build sheepfolds here for our cattle, and cities for our little ones,
17 Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli.
but we ourselves will be ready armed to go before the sons of Israel, until we have brought them to their place. And our little ones shall dwell in the fortified cities because of the inhabitants of the land.
18 Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake.
We will not return to our houses until the sons of Israel have inherited every man his inheritance.
19 Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
For we will not inherit with them on the other side of the Jordan, and forward, because our inheritance is fallen to us on this side of the Jordan eastward.
20 Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo,
And Moses said to them, If ye will do this thing, if ye will arm yourselves to go before Jehovah to the war,
21 ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake,
and every armed man of you will pass over the Jordan before Jehovah, until he has driven out his enemies from before him,
22 dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
and the land is subdued before Jehovah, then afterward ye shall return, and be guiltless towards Jehovah, and towards Israel, and this land shall be to you for a possession before Jehovah.
23 “Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani.
But if ye will not do so, behold, ye have sinned against Jehovah, and be sure your sin will find you out.
24 Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
Build for you cities for your little ones, and folds for your sheep, and do that which has proceeded out of your mouth.
25 Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira.
And the sons of Gad and the sons of Reuben spoke to Moses, saying, Thy servants will do as my lord commands.
26 Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi,
Our little ones, our wives, our flocks, and all our cattle, shall be there in the cities of Gilead,
27 koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
but thy servants will pass over, every man who is armed for war, before Jehovah to battle, as my lord says.
28 Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli.
So Moses gave charge concerning them to Eleazar the priest, and to Joshua the son of Nun, and to the heads of the fathers of the tribes of the sons of Israel.
29 Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo.
And Moses said to them, If the sons of Gad and the sons of Reuben will pass with you over the Jordan, every man that is armed to battle, before Jehovah, and the land shall be subdued before you, then ye shall give them the land of Gilead for a possession,
30 Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
but if they will not pass over with you armed, they shall have possessions among you in the land of Canaan.
31 Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena.
And the sons of Gad and the sons of Reuben answered, saying, As Jehovah has said to thy servants, so we will do.
32 Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
We will pass over armed before Jehovah into the land of Canaan, and the possession of our inheritance is with us beyond the Jordan.
33 Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
And Moses gave to them, even to the sons of Gad, and to the sons of Reuben, and to the half-tribe of Manasseh the son of Joseph, the kingdom of Sihon king of the Amorites, and the kingdom of Og king of Bashan, the land, according to the cities of it with their borders, even the cities of the land round about.
34 Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri,
And the sons of Gad built Dibon, and Ataroth, and Aroer,
35 Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,
and Atrothshophan, and Jazer, and Jogbehah,
36 Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo.
and Beth-nimrah, and Beth-haran: fortified cities, and folds for sheep.
37 Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu,
And the sons of Reuben built Heshbon, and Elealeh, and Kiriathaim,
38 Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
and Nebo, and Baal-meon, (their names being changed, ) and Sibmah. And they gave other names to the cities which they built.
39 Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko.
And the sons of Machir the son of Manasseh went to Gilead, and took it, and dispossessed the Amorites that were in it.
40 Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko.
And Moses gave Gilead to Machir the son of Manasseh, and he dwelt in it.
41 Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi.
And Jair the son of Manasseh went and took the towns of it, and called them Havvoth-jair.
42 Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.
And Nobah went and took Kenath, and the villages of it, and called it Nobah, after his own name.

< Numeri 32 >