< Numeri 29 >

1 “‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
And in the seventh month, on the first day of the month, ye shall have a holy convocation. Ye shall do no job work. It is a day of blowing of trumpets to you.
2 Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
And ye shall offer a burnt offering for a sweet savor to Jehovah: one young bullock, one ram, seven he-lambs a year old without blemish,
3 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
and their meal offering, fine flour mingled with oil, three tenth parts for the bullock, two tenth parts for the ram,
4 Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
and one tenth part for every lamb of the seven lambs,
5 Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
and one he-goat for a sin offering, to make atonement for you,
6 Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
besides the burnt offering of the new moon, and the meal offering of it, and the continual burnt offering and the meal offering of it, and their drink offerings, according to their ordinance, for a sweet savor, an offering made by fire to Jehovah.
7 “‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
And on the tenth day of this seventh month ye shall have a holy convocation, and ye shall afflict your souls. Ye shall do no manner of work.
8 Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
But ye shall offer a burnt offering to Jehovah for a sweet savor: one young bullock, one ram, seven he-lambs a year old (they shall be to you without blemish),
9 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
and their meal offering, fine flour mingled with oil, three tenth parts for the bullock, two tenth parts for the one ram,
10 kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
a tenth part for every lamb of the seven lambs,
11 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
one he-goat for a sin offering, besides the sin offering of atonement, and the continual burnt offering, and the meal offering of it, and their drink offerings.
12 “‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
And on the fifteenth day of the seventh month ye shall have a holy convocation. Ye shall do no job work, and ye shall keep a feast to Jehovah seven days.
13 Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And ye shall offer a burnt offering, an offering made by fire, of a sweet savor to Jehovah: thirteen young bullocks, two rams, fourteen he-lambs a year old (they shall be without blemish),
14 Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
and their meal offering, fine flour mingled with oil, three tenth parts for every bullock of the thirteen bullocks, two tenth parts for each ram of the two rams,
15 Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
and a tenth part for every lamb of the fourteen lambs,
16 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one he-goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, the meal offering of it, and the drink offering of it.
17 “‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
And on the second day, twelve young bullocks, two rams, fourteen he-lambs a year old without blemish,
18 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
and their meal offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, according to their number, after the ordinance,
19 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one he-goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, and the meal offering of it, and their drink offerings.
20 “‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And on the third day, eleven bullocks, two rams, fourteen he-lambs a year old without blemish,
21 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
and their meal offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, according to their number, after the ordinance,
22 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one he-goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, and the meal offering of it, and the drink offering of it.
23 “‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And on the fourth day, ten bullocks, two rams, fourteen he-lambs a year old without blemish,
24 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
their meal offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, according to their number, after the ordinance,
25 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one he-goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, the meal offering of it, and the drink offering of it.
26 “‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And on the fifth day, nine bullocks, two rams, fourteen he-lambs a year old without blemish,
27 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
and their meal offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, according to their number, after the ordinance,
28 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one he-goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, and the meal offering of it, and the drink offering of it.
29 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And on the sixth day, eight bullocks, two rams, fourteen he-lambs a year old without blemish,
30 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
and their meal offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, according to their number, after the ordinance,
31 Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one he-goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, the meal offering of it, and the drink offerings of it.
32 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And on the seventh day, seven bullocks, two rams, fourteen he-lambs a year old without blemish,
33 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
and their meal offering and their drink offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, according to their number, after the ordinance,
34 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one he-goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, the meal offering of it, and the drink offering of it.
35 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
On the eighth day, ye shall have a solemn assembly. Ye shall do no job work.
36 Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
But ye shall offer a burnt offering, an offering made by fire, of a sweet savor to Jehovah: one bullock, one ram, seven he-lambs a year old without blemish,
37 Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
their meal offering and their drink offerings for the bullock, for the ram, and for the lambs, shall be according to their number, after the ordinance,
38 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one he-goat for a sin offering, besides the continual burnt offering, and the meal offering of it, and the drink offering of it.
39 “‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
These ye shall offer to Jehovah in your set feasts, besides your vows, and your freewill offerings, for your burnt offerings, and for your meal offerings, and for your drink offerings, and for your peace offerings.
40 Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.
And Moses told the sons of Israel according to all that Jehovah commanded Moses.

< Numeri 29 >