< Numeri 22 >

1 Aisraeli anayenda kupita ku zigwa za Mowabu nakamanga misasa yawo tsidya lina la Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
And the sons of Israel journeyed, and encamped in the plains of Moab beyond the Jordan at Jericho.
2 Tsono Balaki mwana wa Zipori anaona zonse zimene Aisraeli anachitira Aamori,
And Balak the son of Zippor saw all that Israel had done to the Amorites.
3 ndipo Amowabu anaopa anthuwo chifukwa analipo ambiri. Amowabuwo anachita mantha kwambiri mpaka ananjenjemera chifukwa cha Aisraeli.
And Moab was exceedingly afraid of the people, because they were many. And Moab was distressed because of the sons of Israel.
4 Iwo anati kwa akuluakulu a ku Midiyani, “Gulu ili lidzabudula zonse zimene zatizungulira monga momwe ngʼombe yothena imathera udzu wa ku tchire.” Tsono Balaki mwana wa Zipori, yemwe anali mfumu ya Mowabu pa nthawi imeneyo,
And Moab said to the elders of Midian, Now will this multitude lick up all that is round about us, as the ox licks up the grass of the field. And Balak the son of Zippor was king of Moab at that time.
5 anatumiza amithenga kwa Balaamu mwana wa Beori, yemwe anali ku Petori, pafupi ndi mtsinje, mʼdziko la kwawo kuti akamuyitane. Balaki anati: “Taonani, anthu ochokera ku Igupto abwera, adzaza dziko lonse ndipo akufuna kuchita nane nkhondo.
And he sent messengers to Balaam the son of Beor, to Pethor, which is by the River, to the land of the sons of his people, to call him, saying, Behold, a people came out from Egypt. Behold, they cover the face of the earth, and they abide opposite me.
6 Tsopano bwera, utemberere anthu amenewa chifukwa ndi amphamvu kwambiri kuposa ine. Mwina ndingadzawagonjetse ndi kuwatulutsira kunja kwa dzikoli chifukwa ndikudziwa kuti amene umawadalitsa amadalitsika, ndipo amene umawatemberera amatembereredwa.”
Come now therefore, I pray thee, curse for me this people, for they are too mighty for me. Perhaps I shall prevail, that we may smite them, and that I may drive them out of the land. For I know that he whom thou bless is blessed, and he whom thou curse is cursed.
7 Akuluakulu a Mowabu ndi akuluakulu a Midiyani ananyamuka atatenga ndalama zokalipirira mawula. Atafika kwa Balaamu, anamuwuza zomwe Balaki ananena.
And the elders of Moab and the elders of Midian departed with the rewards of divination in their hand, and they came to Balaam, and spoke to him the words of Balak.
8 Balaamu anawawuza kuti, “Mugone konkuno usiku uno, ndipo ndikuyankhani zomwe Yehova andiwuze.” Choncho akuluakulu a Amowabu anagona kwa Balaamu.
And he said to them, Lodge here this night, and I will bring you word again, as Jehovah shall speak to me. And the rulers of Moab abode with Balaam.
9 Mulungu anabwera kwa Balaamu namufunsa kuti, “Kodi anthu ali ndi iwewa ndani?”
And God came to Balaam, and said, What men are these with thee?
10 Balaamu anayankha Mulungu kuti, “Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, ananditumizira uthenga uwu:
And Balaam said to God, Balak the son of Zippor, king of Moab, has sent to me, saying,
11 ‘Taonani, anthu amene achokera ku dziko la Igupto adzaza dziko lonse. Tsopano bwera udzawatemberere mʼmalo mwanga. Mwina ndidzatha kumenyana nawo ndi kuwatulutsa.’”
Behold, the people came out of Egypt, it covers the face of the earth. Now, come curse them for me. Perhaps I shall be able to fight against them, and shall drive them out.
12 Koma Mulungu anawuza Balaamu kuti, “Usapite nawo. Usawatemberere anthu amenewo chifukwa ndi odalitsika.”
And God said to Balaam, Thou shall not go with them. Thou shall not curse the people, for they are blessed.
13 Mmawa mwake Balaamu anadzuka ndi kuwuza akuluakulu a Balaki aja kuti, “Bwererani ku dziko la kwanu chifukwa Yehova sanandilole kuti ndipite nanu.”
And Balaam rose up in the morning, and said to the rulers of Balak, Get into your land, for Jehovah refuses to give me leave to go with you.
14 Kotero akuluakulu a Mowabu anabwerera kwa Balaki ndi kukanena kuti, “Balaamu wakana kubwera nafe.”
And the rulers of Moab rose up, and they went to Balak, and said, Balaam refuses to come with us.
15 Kenaka Balaki anatumanso akuluakulu ena ambiri ndi olemekezeka kwambiri kuposa oyamba aja ndipo
And Balak sent yet again rulers, more, and more honorable than they.
16 anafika kwa Balaamu nati; “Zomwe Balaki mwana wa Zipori akunena ndi izi: ‘Usalole kuti china chilichonse chikulepheretse kubwera kwa ine,
And they came to Balaam, and said to him, Thus says Balak the son of Zippor, Let nothing, I pray thee, hinder thee from coming to me.
17 chifukwa ndidzakulipira bwino kwambiri ndipo ndidzakuchitira chilichonse chimene unganene. Bwera ndipo uwatemberere anthu amenewa mʼmalo mwanga.’”
For I will promote thee to very great honor, and whatever thou say to me I will do. Come therefore, I pray thee, curse this people for me.
18 Koma Balaamu anayankha atumiki a Balaki kuti, “Ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingachite chilichonse chachikulu kapena chachingʼono kuposa kuchita lamulo la Yehova Mulungu wanga.
And Balaam answered and said to the servants of Balak, If Balak would give me his house full of silver and gold, I cannot go beyond the word of Jehovah my God, to do less or more.
19 Tsopano mukhale kuno usiku uno monga ena anachitira, ndidzaona chimene Yehova adzandiwuza.”
Now therefore, I pray you, tarry ye also here this night, that I may know what Jehovah will speak to me more.
20 Usiku umenewo Mulungu anabwera kwa Balaamu ndipo anati, “Popeza anthu awa abwera kudzakuyitana, nyamuka, pita nawo koma ukachite zokhazo zimene ndikuwuze.”
And God came to Balaam at night, and said to him, If the men come to call thee, rise up, go with them, but only the word which I speak to thee, that shall thou do.
21 Balaamu anadzuka mmawa, namanga bulu wake wamkazi ndipo anapita ndi akuluakulu a Mowabu.
And Balaam rose up in the morning, and saddled his donkey, and went with the rulers of Moab.
22 Koma Mulungu anakwiya kwambiri pamene ankapita ndipo mngelo wa Yehova anayima pa njira kutsutsana naye. Balaamu anakwera bulu wake wamkazi ndipo antchito ake awiri anali naye.
And God's anger was kindled because he went, and the agent of Jehovah placed himself in the way for an adversary against him. Now he was riding upon his donkey, and his two servants were with him.
23 Pamene buluyo anaona mngelo wa Yehova atayima pa njira ndi lupanga mʼmanja mwake, anapatukira kumbali kwa msewu napita kutchire. Balaamu anamumenya kuti abwerere mu msewu.
And the donkey saw the agent of Jehovah standing in the way, with his sword drawn in his hand, and the donkey turned aside out of the way, and went into the field. And Balaam smote the donkey, to turn her into the way.
24 Kenaka mngelo wa Yehova anayima mʼkanjira kakangʼono pakati pa minda iwiri ya mpesa yokhala ndi makoma mbali zonse
Then the agent of Jehovah stood in a narrow path between the vineyards, a wall being on this side, and a wall on that side.
25 Bulu uja ataona mngelo wa Yehova anadzipanikiza ku khoma, kukhukhuza phazi la Balaamu kukhomako. Ndipo pomwepo Balaamu anamenya buluyo kachiwiri.
And the donkey saw the agent of Jehovah, and she thrust herself to the wall, and crushed Balaam's foot against the wall. And he smote her again.
26 Kenaka mngelo wa Yehova anapita patsogolo ndi kuyima pamalo opanikizika pomwe panalibe poti nʼkutembenukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere.
And the agent of Jehovah went further, and stood in a narrow place, where was no way to turn either to the right hand or to the left.
27 Buluyo ataonanso mngelo wa Yehova uja, anagona pansi Balaamu ali pa msana, ndipo iye anakwiya ndi kumumenya ndi ndodo yake.
And the donkey saw the agent of Jehovah, and she lay down under Balaam. And Balaam's anger was kindled, and he smote the donkey with his staff.
28 Pamenepo Yehova anayankhulitsa bulu uja, ndipo buluyo anati kwa Balaamu, “Ndakuchitirani chiyani kuti mundimenye katatuka?”
And Jehovah opened the mouth of the donkey, and she said to Balaam, What have I done to thee, that thou have smitten me these three times?
29 Balaamu anati kwa buluyo, “Wandipusitsa, ndikanakhala ndi lupanga mʼmanja mwanga, ndikanakupha pomwe pano.”
And Balaam said to the donkey, Because thou have mocked me. I would there were a sword in my hand, for now I would have killed thee.
30 Buluyo anati kwa Balaamu, “Kodi sindine bulu wanu, amene mumakwera nthawi zonse kufikira lero? Kodi ndinakuchitiranipo zoterezi?” Iye anati “Ayi.”
And the donkey said to Balaam, Am not I thy donkey, upon which thou have ridden all thy life long to this day? Was I ever accustomed to do so to thee? And he said, No.
31 Pomwepo Yehova anatsekula maso Balaamu ndipo anaona mngelo wa Yehovayo ali chiyimire pa njira ndi lupanga losolola. Tsono iye anawerama nalambira pamaso pake.
Then Jehovah opened the eyes of Balaam, and he saw the agent of Jehovah standing in the way, with his sword drawn in his hand. And he bowed his head, and fell on his face.
32 Mngelo wa Yehova anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani wamenya bulu wako katatu? Taona, Ine ndabwera kudzakutsutsa chifukwa ulendo wakowu ndi woyipa pamaso panga.
And the agent of Jehovah said to him, Why have thou smitten thy donkey these three times? Behold, I have come forth as an adversary, because thy way is perverse before me.
33 Buluyu anandiona ndi kupatuka katatu aka. Akanakhala kuti sanapatuke, ndikanakupha tsopano, koma buluyu nʼkanamusiya ndi moyo.”
And the donkey saw me, and turned aside before me these three times. Unless she had turned aside from me, surely now I would have even slain thee, and saved her alive.
34 Balaamu anati kwa mngelo wa Yehova uja, “Ndachimwa. Sindinadziwe kuti munayima pa njira kunditsutsa. Tsopano ngati Inu simunakondwe, ineyo ndibwerera.”
And Balaam said to the agent of Jehovah, I have sinned, for I knew not that thou stood in the way against me. Now therefore, if it displease thee, I will get back again.
35 Mngelo wa Yehova anati kwa Balaamu, “Pita ndi anthuwa koma ukayankhule zokhazo zimene ndikakuwuze.” Choncho Balaamu anapita ndi akuluakulu a Balaki.
And the agent of Jehovah said to Balaam, Go with the men, but only the word that I shall speak to thee, that thou shall speak. So Balaam went with the rulers of Balak.
36 Balaki atamva kuti Balaamu akubwera, anapita kukakumana naye ku mzinda wa Mowabu umene unali mʼmalire a Arinoni, mʼmphepete mwa dziko lake.
And when Balak heard that Balaam came, he went out to meet him to the City of Moab, which is on the border of the Arnon, which is in the outmost part of the border.
37 Balaki anati kwa Balaamu, “Kodi sindinakutumizire uthenga woti ubwere msanga? Chifukwa chiyani sunabwere kwa ine? Kodi sindingathe kukulipira mokwanira?”
And Balak said to Balaam, Did I not earnestly send to thee to call thee? Why did thou not come to me? Am I not able indeed to promote thee to honor?
38 Balaamu anayankha Balaki kuti, “Taonani, ndabwera kwa inu lero, kodi ine ndili ndi mphamvu zoti nʼkuyankhula chilichonse? Inetu ndiyenera kuyankhula zokhazo zimene Mulungu wandiwuza.”
And Balaam said to Balak, Lo, I have come to thee. Have I now any power at all to speak anything? The word that God puts in my mouth, that shall I speak.
39 Pamenepo Balaamu anapita pamodzi ndi Balaki ku Kiriati-Huzoti.
And Balaam went with Balak, and they came to Kiriath-huzoth.
40 Balaki anapereka nsembe ngʼombe ndi nkhosa, ndipo anapereka zina kwa Balaamu ndi kwa akuluakulu omwe anali naye.
And Balak sacrificed oxen and sheep, and sent to Balaam, and to the rulers that were with him.
41 Mmawa mwake Balaki anatenga Balaamu napita limodzi ku Bamoti Baala, ndipo kumeneko anakaonako gulu lina la Aisraeliwo.
And it came to pass in the morning, that Balak took Balaam, and brought him up into the high places of Baal, and he saw from there the outmost part of the people.

< Numeri 22 >