< Numeri 21 >

1 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo.
And the Canaanite, the king of Arad, who dwelt in the South, heard tell that Israel came by the way of Atharim, and he fought against Israel, and took some of them captive.
2 Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.”
And Israel vowed a vow to Jehovah, and said, If thou will indeed deliver this people into my hand, then I will utterly destroy their cities.
3 Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.
And Jehovah hearkened to the voice of Israel, and delivered up the Canaanites. And they utterly destroyed them and their cities. And the name of the place was called Hormah.
4 Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo
And they journeyed from mount Hor by the way to the Red Sea, to encompass the land of Edom. And the soul of the people was much discouraged because of the way.
5 ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”
And the people spoke against God, and against Moses, Why have ye brought us up out of Egypt to die in the wilderness? For there is no bread, and there is no water, and our soul loathes this light bread.
6 Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa.
And Jehovah sent fiery serpents among the people, and they bit the people, and many people of Israel died.
7 Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.
And the people came to Moses, and said, We have sinned, because we have spoken against Jehovah, and against thee. Pray to Jehovah, that he take away the serpents from us. And Moses prayed for the people.
8 Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.”
And Jehovah said to Moses, Make thee a fiery serpent, and set it upon a standard. And it shall come to pass, that everyone who is bitten, when he sees it, shall live.
9 Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.
And Moses made a serpent of brass, and set it upon the standard. And it came to pass, that if a serpent had bitten any man, when he looked to the serpent of brass, he lived.
10 Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti.
And the sons of Israel journeyed, and encamped in Oboth.
11 Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa.
And they journeyed from Oboth, and encamped at Iyeabarim, in the wilderness which is before Moab, toward the sunrise.
12 Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi.
From there they journeyed, and encamped in the valley of Zered.
13 Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori.
From there they journeyed, and encamped on the other side of the Arnon, which is in the wilderness that comes out of the border of the Amorites, for the Arnon is the border of Moab, between Moab and the Amorites.
14 Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati, “Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa, mu zigwa za Arinoni,
Therefore it is said in the book of the Wars of Jehovah, Vaheb in Suphah, and the valleys of the Arnon,
15 ku matsitso a zigwa amene afika mpaka ku Ari nakhudza malire a dziko la Mowabu.”
and the slope of the valleys that inclines toward the dwelling of Ar, and leans upon the border of Moab.
16 Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”
And from there they journeyed to Beer. That is the well of which Jehovah said to Moses, Gather the people together, and I will give them water.
17 Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi: “Tulutsa madzi, chitsime iwe! Chiyimbireni nyimbo,
Then Israel sang this song: Spring up, O well. Sing ye to it,
18 chitsime chomwe anakumba mafumu, chomwe anakumba anthu omveka, ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.” Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana.
the well, which the rulers dug, which the nobles of the people dug, with the scepter, and with their staves. And from the wilderness they journeyed to Mattanah,
19 Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti,
and from Mattanah to Nahaliel, and from Nahaliel to Bamoth,
20 ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.
and from Bamoth to the valley which is in the field of Moab, to the top of Pisgah, which looks down upon the desert.
21 Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,
And Israel sent messengers to Sihon king of the Amorites, saying,
22 “Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
Let me pass through thy land. We will not turn aside into field, or into vineyard. We will not drink of the water of the wells. We will go by the king's highway, until we have passed thy border.
23 Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli.
And Sihon would not allow Israel to pass through his border, but Sihon gathered all his people together, and went out against Israel into the wilderness, and came to Jahaz, and he fought against Israel.
24 Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa.
And Israel smote him with the edge of the sword, and possessed his land from the Arnon to the Jabbok, even to the sons of Ammon, for the border of the sons of Ammon was strong.
25 Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira.
And Israel took all these cities. And Israel dwelt in all the cities of the Amorites, in Heshbon, and in all the towns of it.
26 Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.
For Heshbon was the city of Sihon the king of the Amorites, who had fought against the former king of Moab, and had taken all his land out of his hand, even to the Arnon.
27 Nʼchifukwa chake alakatuli amati: “Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso; mzinda wa Sihoni ukhazikike.
Therefore those who speak in proverbs say, Come ye to Heshbon. Let the city of Sihon be built and established.
28 “Moto unabuka ku Hesiboni, malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni. Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu, nzika za ku malo okwera a Arinoni.
For a fire has gone out of Heshbon, a flame from the city of Sihon. It has devoured Ar of Moab, the lords of the high places of the Arnon.
29 Tsoka kwa iwe Mowabu! Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi! Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa ndipo ana ake aakazi ngati akapolo, akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.
Woe to thee, Moab! Thou are undone, O people of Chemosh. He has given his sons as fugitives, and his daughters into captivity, to Sihon king of the Amorites.
30 “Koma ife tawagonjetsa; Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni. Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa, mzinda womwe umafika ku Medeba.
We have shot at them. Heshbon is perished even to Dibon, and we have laid waste even to Nophah, which reaches to Medeba.
31 “Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”
Thus Israel dwelt in the land of the Amorites.
32 Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko.
And Moses sent to spy out Jazer. And they took the towns of it, and drove out the Amorites that were there.
33 Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.
And they turned and went up by the way of Bashan. And Og the king of Bashan went out against them, he and all his people, to battle at Edrei.
34 Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”
And Jehovah said to Moses, Fear him not, for I have delivered him into thy hand, and all his people, and his land. And thou shall do to him as thou did to Sihon king of the Amorites, who dwelt at Heshbon.
35 Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.
So they smote him, and his sons and all his people, until there was none left to him remaining. And they possessed his land.

< Numeri 21 >