< Levitiko 24 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Lamula Aisraeli kuti akupatse mafuta anyale, a olivi wabwino kwambiri kuti nyalezo ziziyaka nthawi zonse.
Command the sons of Israel, that they bring to thee pure beaten olive oil for the light, to cause a lamp to burn continually.
3 Kunja kwa nsalu yotchinga Bokosi la Chipangano, mʼchihema cha msonkhano, Aaroni azionetsetsa kuti nyale ikukhala chiyakire pamaso pa Yehova kuyambira madzulo mpaka mmawa, nthawi zonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yonse.
Aaron shall keep it outside the veil of the testimony, in the tent of meeting, in order from evening to morning before Jehovah continually. It shall be a statute forever throughout your generations.
4 Aaroni ayatse nyale zimene zili pa choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri kuti zikhale zoyaka nthawi zonse pamaso pa Yehova.
He shall keep the lamps upon the pure lampstand in order before Jehovah continually.
5 “Mutenge ufa wosalala ndipo muphike makeke khumi ndi awiri ndipo keke iliyonse ikhale ya ufa wa makilogalamu awiri.
And thou shall take fine flour, and bake twelve cakes of it. Two tenth parts of an ephah shall be in one cake.
6 Muwayike pa tebulo la golide wabwino kwambiri pamaso pa Yehova mʼmizere iwiri. Mzere uliwonse ukhale wa makeke asanu ndi imodzi.
And thou shall set them in two rows, six on a row, upon the pure table before Jehovah.
7 Pa mzere uliwonse muyikepo lubani wafungo lokoma kuti pamodzi ndi bulediyo akhale wachikumbutso cha nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova.
And thou shall put pure frankincense upon each row, that it may be on the bread for a memorial, even an offering made by fire to Jehovah.
8 Sabata ndi sabata nthawi zonse Aaroni aziyika makeke amenewa pamaso pa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli onse kuti akhale pangano lamuyaya.
Every sabbath day he shall set it in order before Jehovah continually. It is on the behalf of the sons of Israel, an everlasting covenant.
9 Chakudyacho ndi cha Aaroni ndi ana ake ndipo azidyera ku malo wopatulika chifukwa kwa iye chakudyacho ndi chopatulika kwambiri chochokera pa chopereka chopsereza cha Yehova.”
And it shall be for Aaron and his sons. And they shall eat it in a holy place, for it is most holy to him of the offerings of Jehovah made by fire by a perpetual statute.
10 Tsiku lina munthu wina wamwamuna amene amayi ake anali Mwisraeli koma abambo ake anali Mwigupto anapita kwa Aisraeli ndipo anakangana ndi Mwisraeli wina ku msasa.
And the son of an Israelite woman, whose father was an Egyptian, went out among the sons of Israel. And the son of the Israelite woman and a man of Israel strove together in the camp,
11 Munthu uja ananyoza dzina la Yehova ndi kulitemberera. Choncho anabwera naye kwa Mose. Dzina la amayi ake linali Selomiti, mwana wa Dibiri, wa fuko la Dani.
and the son of the Israelite woman blasphemed the Name, and cursed. And they brought him to Moses. And his mother's name was Shelomith, the daughter of Dibri, of the tribe of Dan.
12 Anamuyika mʼndende mpaka atadziwa bwino chofuna cha Yehova.
And they put him in ward, that it might be declared to them at the mouth of Jehovah.
13 Ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
14 “Pita naye kunja kwa msasa munthu wotembererayo. Onse amene anamumva akutemberera asanjike manja awo pamutu pake ndipo gulu lonse la anthu limugende miyala.
Bring forth him who has cursed outside the camp, and let all who heard him lay their hands upon his head, and let all the congregation stone him.
15 Choncho uza Aisraeli kuti, ‘Aliyense wotemberera Mulungu wake alangidwe.
And thou shall speak to the sons of Israel, saying, Whoever curses his God shall bear his sin.
16 Aliyense wonyoza dzina la Yehova, mlendo ngakhale mbadwa, aphedwe. Gulu lonse la anthu limuponye miyala.
And he who blasphemes the name of Jehovah, he shall surely be put to death. All the congregation shall certainly stone him. As well the sojourner, as the home-born, when he blasphemes the Name, shall be put to death.
17 “‘Ngati munthu wina aliyense achotsa moyo wa munthu mnzake, munthuyo ayenera kuphedwa.
And he who smites any man mortally shall surely be put to death.
18 Aliyense wopha chiweto cha mnzake ayenera kulipira china. Moyo kulipa moyo.
And he who smites a beast mortally shall make it good, life for life.
19 Ngati munthu avulaza mnzake, nayenso amuchite zomwe wachitira mnzakeyo:
And if a man causes a blemish in his neighbor, as he has done, so shall it be done to him:
20 kuthyola fupa kulipira kuthyola fupa, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino. Monga momwe anavulazira mnzake, amuvulaze chimodzimodzinso.
injury for injury, eye for eye, tooth for tooth, as he has caused a blemish in a man, so shall it be rendered to him.
21 Aliyense wopha chiweto cha mnzake, alipire chiweto china, koma aliyense wopha munthu ayenera kuphedwa.
And he who kills a beast shall make it good. And he who kills a man shall be put to death.
22 Lamulo la mlendo ndi mbadwa ndi limodzi lomweli. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
Ye shall have one manner of law, as for the sojourner, as for the home-born, for I am Jehovah your God.
23 Pamenepo Mose anawuza Aisraeli zimenezi, ndipo iwo anatulutsira munthu wotembererayo kunja kwa msasa ndi kumugenda miyala. Aisraeli anachita zimene Yehova analamula Mose.
And Moses spoke to the sons of Israel, and they brought forth him who had cursed out of the camp, and stoned him with stones. And the sons of Israel did as Jehovah commanded Moses.

< Levitiko 24 >