< Levitiko 23 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
Speak to the sons of Israel, and say to them, The set feasts of Jehovah, which ye shall proclaim to be holy convocations, even these are my set feasts.
3 “‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
Six days shall work be done, but on the seventh day is a sabbath of solemn rest, a holy convocation. Ye shall do no manner of work. It is a sabbath to Jehovah in all your dwellings.
4 “‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
These are the set feasts of Jehovah, even holy convocations, which ye shall proclaim in their appointed season:
5 Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
In the first month, on the fourteenth day of the month at evening, is Jehovah's Passover.
6 Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
And on the fifteenth day of the same month is the feast of unleavened bread to Jehovah. Ye shall eat unleavened bread seven days.
7 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
In the first day ye shall have a holy convocation. Ye shall do no job work.
8 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
But ye shall offer an offering made by fire to Jehovah seven days. In the seventh day is a holy convocation, ye shall do no job work.
9 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
10 “Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
Speak to the sons of Israel, and say to them, When ye have come into the land which I give to you, and shall reap the harvest of it, then ye shall bring the sheaf of the first-fruits of your harvest to the priest.
11 Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
And he shall wave the sheaf before Jehovah, to be accepted for you. On the morrow after the sabbath the priest shall wave it.
12 Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
And in the day when ye wave the sheaf, ye shall offer a he-lamb without blemish a year old for a burnt offering to Jehovah.
13 Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
And the meal offering of it shall be two tenth parts of an ephah of fine flour mingled with oil, an offering made by fire to Jehovah for a sweet savor. And the drink offering of it shall be of wine, the fourth part of a hin.
14 Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
And ye shall eat neither bread, nor parched grain, nor fresh ears, until this selfsame day, until ye have brought the oblation of your God. It is a statute forever throughout your generations in all your dwellings.
15 “‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
And ye shall count to you from the morrow after the sabbath, from the day that ye brought the sheaf of the wave offering, there shall be complete seven sabbaths.
16 Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
Ye shall number fifty days, even to the morrow after the seventh sabbath, and ye shall offer a new meal offering to Jehovah.
17 Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
Ye shall bring out of your habitations two wave-loaves of two tenth parts of an ephah. They shall be of fine flour. They shall be baked with leaven, for first-fruits to Jehovah.
18 Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
And ye shall present with the bread seven lambs without blemish a year old, and one young bullock, and two rams. They shall be a burnt offering to Jehovah, with their meal offering, and their drink offerings, even an offering made by fire, of a sweet savor to Jehovah.
19 Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
And ye shall offer one he-goat for a sin offering, and two he-lambs a year old for a sacrifice of peace offerings.
20 Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
And the priest shall wave them with the bread of the first-fruits for a wave offering before Jehovah, with the two lambs. They shall be holy to Jehovah for the priest.
21 Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
And ye shall make proclamation on the selfsame day, there shall be a holy convocation to you. Ye shall do no job work. It is a statute forever in all your dwellings throughout your generations.
22 “‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
And when ye reap the harvest of your land, thou shall not wholly reap the corners of thy field, neither shall thou gather the gleaning of thy harvest. Thou shall leave them for the poor man, and for the sojourner. I am Jehovah your God.
23 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
24 “Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
Speak to the sons of Israel, saying, In the seventh month, on the first day of the month, shall be a solemn rest to you, a memorial of blowing of trumpets, a holy convocation.
25 Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
Ye shall do no job work, and ye shall offer an offering made by fire to Jehovah.
26 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
27 “Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
However on the tenth day of this seventh month is the day of atonement. It shall be a holy convocation to you, and ye shall afflict your souls, and ye shall offer an offering made by fire to Jehovah.
28 Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
And ye shall do no manner of work in that same day, for it is a day of atonement, to make atonement for you before Jehovah your God.
29 Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
For whatever soul it be who shall not be afflicted in that same day, he shall be cut off from his people.
30 Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
And whatever soul it be who does any manner of work in that same day, that soul I will destroy from among his people.
31 Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
Ye shall do no manner of work. It is a statute forever throughout your generations in all your dwellings.
32 Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
It shall be to you a sabbath of solemn rest, and ye shall afflict your souls. In the ninth day of the month at evening, from evening to evening, ye shall keep your sabbath.
33 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
34 “Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
Speak to the sons of Israel, saying, On the fifteenth day of this seventh month is the feast of tabernacles for seven days to Jehovah.
35 Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
On the first day shall be a holy convocation. Ye shall do no job work.
36 Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
Seven days ye shall offer an offering made by fire to Jehovah. On the eighth day shall be a holy convocation to you, and ye shall offer an offering made by fire to Jehovah. It is a solemn assembly; ye shall do no job work.
37 (“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
These are the set feasts of Jehovah, which ye shall proclaim to be holy convocations, to offer an offering made by fire to Jehovah, a burnt offering, and a meal offering, a sacrifice, and drink offerings, each on its own day.
38 Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
Besides the sabbaths of Jehovah, and besides your gifts, and besides all your vows, and besides all your freewill offerings, which ye give to Jehovah.
39 “‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
However on the fifteenth day of the seventh month, when ye have gathered in the fruits of the land, ye shall keep the feast of Jehovah seven days. On the first day shall be a solemn rest, and on the eighth day shall be a solemn rest.
40 Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
And ye shall take to you on the first day the fruit of goodly trees, branches of palm trees, and boughs of thick trees, and willows of the brook, and ye shall rejoice before Jehovah your God seven days.
41 Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
And ye shall keep it a feast to Jehovah seven days in the year. It is a statute forever throughout your generations. Ye shall keep it in the seventh month.
42 Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
Ye shall dwell in booths seven days. All who are home-born in Israel shall dwell in booths,
43 kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
that your generations may know that I made the sons of Israel to dwell in booths, when I brought them out of the land of Egypt. I am Jehovah your God.
44 Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.
And Moses declared to the sons of Israel the set feasts of Jehovah.

< Levitiko 23 >