< Levitiko 17 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And Jehovah spoke to Moses, saying,
2 “Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi:
Speak to Aaron, and to his sons, and to all the sons of Israel, and say to them, This is the thing which Jehovah has commanded, saying,
3 Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa,
Whatever man there is of the house of Israel, who kills an ox, or lamb, or goat, in the camp, or who kills it outside the camp,
4 mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
and has not brought it to the door of the tent of meeting, to offer it as an oblation to Jehovah before the tabernacle of Jehovah, blood shall be imputed to that man. He has shed blood, and that man shall be cut off from among his people,
5 Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano.
to the end that the sons of Israel may bring their sacrifices, which they sacrifice in the open field, even that they may bring them to Jehovah, to the door of the tent of meeting, to the priest, and sacrifice them for sacrifices of peace offerings to Jehovah.
6 Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova.
And the priest shall sprinkle the blood upon the altar of Jehovah at the door of the tent of meeting, and burn the fat for a sweet savor to Jehovah.
7 Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’”
And they shall no more sacrifice their sacrifices to the he-goats, after which they play the harlot. This shall be a statute forever to them throughout their generations.
8 “Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse
And thou shall say to them, Whatever man there is of the house of Israel, or of the strangers that sojourn among them, who offers a burnt offering or sacrifice,
9 popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’”
and does not bring it to the door of the tent of meeting, to sacrifice it to Jehovah, that man shall be cut off from his people.
10 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake.
And whatever man there is of the house of Israel, or of the strangers that sojourn among them, who eats any manner of blood, I will set my face against that soul who eats blood, and will cut him off from among his people.
11 Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo.
For the life of the flesh is in the blood, and I have given it to you upon the altar to make atonement for your souls, for it is the blood that makes atonement by reason of the life.
12 Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’”
Therefore I said to the sons of Israel, No soul of you shall eat blood, nor shall any stranger that sojourns among you eat blood.
13 “Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi,
And whatever man there is of the sons of Israel, or of the strangers that sojourn among them, who takes any beast or bird in hunting that may be eaten, he shall pour out the blood of it, and cover it with dust.
14 chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.
For as to the life of all flesh, the blood of it is with the life of it. Therefore I said to the sons of Israel, Ye shall eat the blood of no manner of flesh, for the life of all flesh is the blood of it. Whoever eats it shall be cut off.
15 “‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa.
And every soul who eats that which dies of itself, or that which is torn of beasts, whether he be home-born or a sojourner, he shall wash his clothes, and bathe himself in water, and be unclean until the evening, then he shall be clean.
16 Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’”
But if he does not wash them, nor bathe his flesh, then he shall bear his iniquity.

< Levitiko 17 >