< Levitiko 16 >

1 Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
And Jehovah spoke to Moses, after the death of the two sons of Aaron, when they drew near before Jehovah, and died,
2 Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
and Jehovah said to Moses, Speak to Aaron thy brother, that he not come at all times into the holy place within the veil, before the mercy-seat which is upon the ark, that he not die, for I will appear in the cloud upon the mercy-seat.
3 “Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
Aaron shall come into the holy place this way: with a young bullock for a sin offering, and a ram for a burnt offering.
4 Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
He shall put on the holy linen tunic, and he shall have the linen breeches upon his flesh, and shall be girded with the linen sash, and he shall be attired with the linen miter. They are the holy garments, and he shall bathe his flesh in water, and put them on.
5 Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
And he shall take from the congregation of the sons of Israel two he-goats for a sin offering, and one ram for a burnt offering.
6 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
And Aaron shall present the bullock of the sin offering, which is for himself, and make atonement for himself, and for his house.
7 Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
And he shall take the two goats, and set them before Jehovah at the door of the tent of meeting.
8 Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
And Aaron shall cast lots upon the two goats, one lot for Jehovah, and the other lot for the scapegoat.
9 Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
And Aaron shall present the goat upon which the lot fell for Jehovah, and offer him for a sin offering.
10 Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
But the goat, on which the lot fell for the scapegoat, shall be set alive before Jehovah, to make atonement for him, to send him away for the scapegoat into the wilderness.
11 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
And Aaron shall present the bullock of the sin offering, which is for himself, and shall make atonement for himself, and for his house, and shall kill the bullock of the sin offering which is for himself.
12 Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
And he shall take a censer full of coals of fire from off the altar before Jehovah, and his hands full of sweet incense beaten small, and bring it within the veil.
13 Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
And he shall put the incense upon the fire before Jehovah, that the cloud of the incense may cover the mercy-seat that is upon the testimony, that he not die.
14 Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
And he shall take of the blood of the bullock, and sprinkle it with his finger upon the mercy-seat on the east. And he shall sprinkle of the blood with his finger seven times before the mercy-seat.
15 “Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
Then he shall kill the goat of the sin offering, that is for the people, and bring his blood within the veil, and do with his blood as he did with the blood of the bullock, and sprinkle it upon the mercy-seat, and before the mercy-seat.
16 Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
And he shall make atonement for the holy place, because of the uncleannesses of the sons of Israel, and because of their transgressions, even all their sins. And so he shall do for the tent of meeting that dwells with them in the midst of their uncleannesses.
17 Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
And there shall be no man in the tent of meeting when he goes in to make atonement in the holy place until he comes out, and has made atonement for himself, and for his household, and for all the assembly of Israel.
18 “Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
And he shall go out to the altar that is before Jehovah, and make atonement for it. And shall take of the blood of the bullock, and of the blood of the goat, and put it upon the horns of the altar round about.
19 Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
And he shall sprinkle of the blood upon it with his finger seven times, and cleanse it, and hallow it from the uncleannesses of the sons of Israel.
20 “Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
And when he has made an end of atoning for the holy place, and the tent of meeting, and the altar, he shall present the live goat.
21 Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
And Aaron shall lay both his hands upon the head of the live goat, and confess over him all the iniquities of the sons of Israel, and all their transgressions, even all their sins. And he shall put them upon the head of the goat, and shall send him away by the hand of a man who is in readiness into the wilderness.
22 Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
And the goat shall bear upon him all their iniquities to a solitary land. And he shall let the goat go in the wilderness.
23 “Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
And Aaron shall come into the tent of meeting, and shall put off the linen garments, which he put on when he went into the holy place, and shall leave them there.
24 Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
And he shall bathe his flesh in water in a holy place, and put on his garments, and come forth, and offer his burnt offering and the burnt offering of the people, and make atonement for himself and for the people.
25 Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
And he shall burn upon the altar the fat of the sin offering.
26 “Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
And he who lets the goat go for the scapegoat shall wash his clothes, and bathe his flesh in water, and afterward he shall come into the camp.
27 Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
And the bullock of the sin offering, and the goat of the sin offering, whose blood was brought in to make atonement in the holy place, shall be carried forth outside the camp, and they shall burn in the fire their skins, and their flesh, and their dung.
28 Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
And he who burns them shall wash his clothes, and bathe his flesh in water, and afterward he shall come into the camp.
29 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
And it shall be a statute forever to you. In the seventh month, on the tenth day of the month, ye shall afflict your souls, and shall do no manner of work, the home-born, or the stranger who sojourns among you.
30 chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
For on this day atonement shall be made for you, to cleanse you. Ye shall be clean from all your sins before Jehovah.
31 Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
It is a sabbath of solemn rest to you, and ye shall afflict your souls. It is a statute forever.
32 Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
And the priest, who shall be anointed and who shall be consecrated to be priest in his father's stead, shall make the atonement. And he shall put on the linen garments, even the holy garments,
33 Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
and shall make atonement for the holy sanctuary, and he shall make atonement for the tent of meeting and for the altar, and he shall make atonement for the priests and for all the people of the assembly.
34 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.
And this shall be an everlasting statute to you, to make atonement for the sons of Israel because of all their sins once in the year. And he did as Jehovah commanded Moses.

< Levitiko 16 >