< Oweruza 6 >

1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
And the sons of Israel did that which was evil in the sight of Jehovah, and Jehovah delivered them into the hand of Midian seven years.
2 Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
And the hand of Midian prevailed against Israel. And because of Midian the sons of Israel made for themselves the dens which are in the mountains, and the caves, and the strongholds.
3 Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
And so it was, when Israel had sown, that the Midianites came up, and the Amalekites, and the sons of the east, they came up against them.
4 Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
And they encamped against them, and destroyed the increase of the earth, till thou come to Gaza, and left no sustenance in Israel, neither sheep, nor ox, nor donkey.
5 Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
For they came up with their cattle and their tents. They came in as locusts for multitude. Both they and their camels were without number, and they came into the land to destroy it.
6 Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
And Israel was brought very low because of Midian, and the sons of Israel cried to Jehovah.
7 Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
And it came to pass, when the sons of Israel cried to Jehovah because of Midian,
8 Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
that Jehovah sent a prophet to the sons of Israel. And he said to them, Thus says Jehovah, the God of Israel, I brought you up from Egypt, and brought you forth out of the house of bondage.
9 Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
And I delivered you out of the hand of the Egyptians, and out of the hand of all that oppressed you, and drove them out from before you, and gave you their land.
10 Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
And I said to you, I am Jehovah your God. Ye shall not fear the gods of the Amorites, in whose land ye dwell, but ye have not hearkened to my voice.
11 Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
And the agent of Jehovah came, and sat under the oak which was in Ophrah that pertained to Joash the Abiezrite. And his son Gideon was beating out wheat in the winepress, to hide it from the Midianites.
12 Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
And the agent of Jehovah appeared to him, and said to him, Jehovah is with thee, thou mighty man of valor.
13 Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
And Gideon said to him, Oh, my lord, if Jehovah is with us, then why has all this befallen us? And where are all his wondrous works which our fathers told us of, saying, Did not Jehovah bring us up from Egypt? But now Jehovah has cast us off, and delivered us into the hand of Midian.
14 Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
And Jehovah looked upon him, and said, Go in this thy might, and save Israel from the hand of Midian. Have I not sent thee?
15 Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
And he said to him, Oh, Lord, with what shall I save Israel? Behold, my family is the poorest in Manasseh, and I am the least in my father's house.
16 Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
And Jehovah said to him, Surely I will be with thee, and thou shall smite the Midianites as one man.
17 Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
And he said to him, If now I have found favor in thy sight, then show me a sign that it is thou who talk with me.
18 Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
Depart not from here, I pray thee, until I come to thee, and bring forth my present, and lay it before thee. And he said, I will tarry until thou come again.
19 Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
And Gideon went in, and made ready a kid, and unleavened cakes of an ephah of meal. He put the flesh in a basket, and he put the broth in a pot, and brought it out to him under the oak, and presented it.
20 Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
And the agent of God said to him, Take the flesh and the unleavened cakes, and lay them upon this rock, and pour out the broth. And he did so.
21 Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
Then the agent of Jehovah put forth the end of the staff that was in his hand, and touched the flesh and the unleavened cakes. And there went up fire out of the rock, and consumed the flesh and the unleavened cakes. And the agent of Jehovah departed out of his sight.
22 Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
And Gideon saw that he was the agent of Jehovah. And Gideon said, Alas, O lord Jehovah! Inasmuch as I have seen the agent of Jehovah face to face.
23 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
And Jehovah said to him, Peace be to thee. Fear not; thou shall not die.
24 Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
Then Gideon built an altar there to Jehovah, and called it Jehovah-shalom. To this day it is yet in Ophrah of the Abiezrites.
25 Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
And it came to pass the same night, that Jehovah said to him, Take thy father's bullock, even the second bullock seven years old, and throw down the altar of Baal that thy father has, and cut down the Asherah that is by it.
26 Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
And build an altar to Jehovah thy God upon the top of this stronghold, in the orderly manner, and take the second bullock, and offer a burnt offering with the wood of the Asherah which thou shall cut down.
27 Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
Then Gideon took ten men of his servants, and did as Jehovah had spoken to him. And it came to pass, because he feared his father's household and the men of the city, so that he could not do it by day, that he did it by night.
28 Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
And when the men of the city arose early in the morning, behold, the altar of Baal was broken down, and the Asherah was cut down that was by it, and the second bullock was offered upon the altar that was built.
29 Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
And they said one to another, Who has done this thing? And when they inquired and asked, they said, Gideon the son of Joash has done this thing.
30 Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
Then the men of the city said to Joash, Bring out thy son, that he may die, because he has broken down the altar of Baal, and because he has cut down the Asherah that was by it.
31 Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
And Joash said to all who stood against him, Will ye contend for Baal? Or will ye save him? He who will contend for him, let him be put to death while it is morning. If he be a god, let him contend for himself because he has broken down his altar.
32 Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
Therefore on that day he called him Jerubbaal, saying, Let Baal contend against him because he has broken down his altar.
33 Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
Then all the Midianites and the Amalekites and the sons of the east assembled themselves together. And they passed over, and encamped in the valley of Jezreel.
34 Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
But the Spirit of Jehovah came upon Gideon, and he blew a trumpet, and Abiezer was gathered together after him.
35 Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
And he sent messengers throughout all Manasseh, and they also were gathered together after him. And he sent messengers to Asher, and to Zebulun, and to Naphtali, and they came up to meet them.
36 Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
And Gideon said to God, If thou will save Israel by my hand, as thou have spoken,
37 onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
behold, I will put a fleece of wool on the threshing-floor. If there be dew on the fleece only, and it be dry upon all the ground, then I shall know that thou will save Israel by my hand as thou have spoken.
38 Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
And it was so, for he rose up early on the morrow, and pressed the fleece together, and wrung the dew out of the fleece, a bowlful of water.
39 Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
And Gideon said to God, Let not thine anger be kindled against me, and I will speak but this once. Let me make trial, I pray thee, but this once with the fleece. Let it now be dry only upon the fleece, and upon all the ground let there be dew.
40 Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.
And God did so that night, for it was dry upon the fleece only, and there was dew on all the ground.

< Oweruza 6 >