< Oweruza 14 >

1 Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
And Samson went down to Timnah, and saw a woman in Timnah of the daughters of the Philistines.
2 Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
And he came up, and told his father and his mother, and said, I have seen a woman in Timnah of the daughters of the Philistines. Now therefore get her for me to wife.
3 Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
Then his father and his mother said to him, Is there never a woman among the daughters of thy brothers, or among all my people, that thou go to take a wife of the uncircumcised Philistines? And Samson said to his father, Get her for me, for she pleases me well.
4 (Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
But his father and his mother knew not that it was of Jehovah, for he sought an occasion against the Philistines. Now at that time the Philistines had rule over Israel.
5 Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
Then Samson went down, and his father and his mother, to Timnah, and came to the vineyards of Timnah. And, behold, a young lion roared against him.
6 Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
And the Spirit of Jehovah came mightily upon him, and he tore him apart as he would have torn a kid, and he had nothing in his hand. But he did not tell his father or his mother what he had done.
7 Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
And he went down, and talked with the woman, and she pleased Samson well.
8 Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
And after a while he returned to take her. And he turned aside to see the carcass of the lion, and, behold, there was a swarm of bees in the body of the lion, and honey.
9 Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
And he took it into his hands, and went on, eating as he went. And he came to his father and mother, and gave to them, and they ate, but he did not tell them that he had taken the honey out of the body of the lion.
10 Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
And his father went down to the woman, and Samson made a feast there, for so the young men used to do.
11 Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
And it came to pass, when they saw him, that they brought thirty companions to be with him.
12 Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
And Samson said to them, Let me now put forth a riddle to you. If ye can declare it to me within the seven days of the feast, and find it out, then I will give you thirty linen garments and thirty changes of raiment,
13 Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
but if ye cannot declare it to me, then ye shall give me thirty linen garments and thirty changes of raiment. And they said to him, Put forth thy riddle, that we may hear it.
14 Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
And he said to them, Out of the eater came forth food, and out of the strong came forth sweetness. And they could not in three days declare the riddle.
15 Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
And it came to pass on the seventh day, that they said to Samson's wife, Entice thy husband, that he may declare to us the riddle, lest we burn thee and thy father's house with fire. Have ye called us to impoverish us? Is it not so?
16 Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
And Samson's wife wept before him, and said, Thou do but hate me, and not love me. Thou have put forth a riddle to the sons of my people, and have not told it to me. And he said to her, Behold, I have not told it to my father nor my mother, and shall I tell thee?
17 Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
And she wept before him the seven days, while their feast lasted. And it came to pass on the seventh day, that he told her because she pressed him greatly. And she told the riddle to the sons of her people.
18 Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
And the men of the city said to him on the seventh day before the sun went down, What is sweeter than honey? and what is stronger than a lion? And he said to them, If ye had not plowed with my heifer, ye would not have found out my riddle.
19 Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
And the Spirit of Jehovah came mightily upon him, and he went down to Ashkelon, and smote thirty men of them, and took their spoil, and gave the changes of raiment to those who declared the riddle. And his anger was kindled, and he went up to his father's house.
20 Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.
But Samson's wife was given to his companion, whom he had used as his friend.

< Oweruza 14 >