< Oweruza 11 >

1 Yefita wa ku Giliyadi anali wankhondo wa mphamvu. Iyeyu amayi ake anali mkazi wachiwerewere, ndipo abambo ake anali Giliyadi.
Now Jephthah the Gileadite was a mighty man of valor, and he was the son of a harlot, and Gilead begot Jephthah.
2 Mkazi wake wa Giliyadi anabereka naye ana aamuna. Tsono ana amenewa atakula anapirikitsa Yefita ndi kumuwuza kuti, “Sudzalandirako cholowa mʼnyumba ya abambo athu chifukwa ndiwe mwana wa mkazi wina.”
And Gilead's wife bore sons to him. And when his wife's sons grew up, they drove out Jephthah, and said to him, Thou shall not inherit in our father's house, for thou are the son of another woman.
3 Choncho Yefita anathawa kuchoka kwa abale ake ndi kukakhala mʼdziko la Tobu. Kumeneko anakakopa ndi kusonkhanitsa anthu achabechabe ndipo anatuluka pamodzi kukasakaza zinthu.
Then Jephthah fled from his brothers, and dwelt in the land of Tob. And vain fellows were gathered to Jephthah, and they went out with him.
4 Patapita nthawi Aamoni anadzachita nkhondo ndi Israeli.
And it came to pass after a while, that the sons of Ammon made war against Israel.
5 Tsono pamene Aamoni ankathira nkhondo Aisraeli, akuluakulu a ku Giliyadi anapita kukamutenga Yefita ku dziko la Tobu.
And it was so, that, when the sons of Ammon made war against Israel, the elders of Gilead went to fetch Jephthah out of the land of Tob.
6 Iwo anati kwa iye, “Bwera ukhale mkulu wathu wankhondo kuti timenyane ndi Amoni.”
And they said to Jephthah, Come and be our chief, that we may fight with the sons of Ammon.
7 Yefita anawawuza Agiliyadi kuti, “Kodi inu suja munkadana nane ndi kundithamangitsa ku nyumba ya abambo anga? Nʼchifukwa chiyani lero mwabwera kwa ine pamene muli pa mavuto?”
And Jephthah said to the elders of Gilead, Did ye not hate me, and drive me out of my father's house? And why have ye come to me now when ye are in distress?
8 Akuluakulu a ku Giliyadi aja anamuyankha kuti, “Chimene tabwerera kwa iwe ndi chakuti upite nafe kukamenyana ndi Aamoni, ndipo udzakhala wolamulira wa onse okhala mu Giliyadi.”
And the elders of Gilead said to Jephthah, For that reason we turned again to thee now, that thou may go with us, and fight with the sons of Ammon. And thou shall be our head over all the inhabitants of Gilead.
9 Yefita anawayankha akuluakulu a ku Giliyadi kuti, “Ngati mundibwezeranso kwathu kuti ndikachite nkhondo ndi Aamoni ndipo Yehova nʼkukandithandiza kuwagonjetsa, ndidzakhaladi wokulamulirani?”
And Jephthah said to the elders of Gilead, If ye bring me home again to fight with the sons of Ammon, and Jehovah delivers them before me, shall I be your head?
10 Akuluakulu a ku Giliyadi anamuyankha kuti, “Yehova akhale mboni pakati pa inu ndi ife, ngati sitidzachita monga mwa mawu anu.”
And the elders of Gilead said to Jephthah, Jehovah shall be witness between us. Surely according to thy word so will we do.
11 Choncho Yefita anapita nawo akuluakulu a ku Giliyadi aja, ndipo anthu a kumeneko anamusandutsa kukhala wowalamulira ndi mkulu wankhondo. Tsono Yefita anabwerezanso mawu omwewa pamaso pa Yehova ku Mizipa.
Then Jephthah went with the elders of Gilead, and the people made him head and chief over them. And Jephthah spoke all his words before Jehovah in Mizpah.
12 Kenaka Yefita anatuma amithenga kwa mfumu ya Aamoni ndi funso lakuti, “Kodi ife takuchimwirani chiyani kuti muzichita nkhondo ndi dziko langa?”
And Jephthah sent messengers to the king of the sons of Ammon, saying, What have thou to do with me, that thou have come to me to fight against my land?
13 Ndipo mfumu ya Aamoni inayankha amithenga a Yefita aja kuti, “Pamene Israeli amatuluka kuchokera mu Igupto, analanda dziko langa kuyambira ku mtsinje wa Arinoni mpaka ku mtsinje wa Yaboki mpakanso ku mtsinje wa Yorodani. Tsopano mundibwezere dziko langa mwamtendere.”
And the king of the sons of Ammon answered to the messengers of Jephthah, Because Israel took away my land when he came up out of Egypt, from the Arnon even to the Jabbok, and to the Jordan. Now therefore restore those lands again peaceably.
14 Yefita anatumizanso amithenga akewo kwa mfumu ya Aamoni
And Jephthah sent messengers again to the king of the sons of Ammon.
15 kukanena kuti, Yefita akuti, “Israeli sanalande dziko la Mowabu kapena dziko la Aamoni.
And he said to him, Thus says Jephthah: Israel did not take away the land of Moab, nor the land of the sons of Ammon,
16 Koma pamene Aisraeli ankachoka ku Igupto anadzera njira ya ku chipululu mpaka ku Nyanja Yofiira nakafika ku Kadesi.
but when they came up from Egypt, and Israel went through the wilderness to the Red Sea, and came to Kadesh,
17 Kenaka Israeli anatumiza amithenga kwa mfumu ya ku Edomu kuti, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu,’ Koma mfumu ya ku Edomu sinamvere zimenezo. Aisraeli anatumizanso amithenga kwa mfumu ya ku Mowabu, ndipo iyo inakananso. Choncho Israeli anakhala ku Kadesi.
then Israel sent messengers to the king of Edom, saying, Let me, I pray thee, pass through thy land, but the king of Edom did not hearken. And in like manner he sent to the king of Moab, but he would not. And Israel abode in Kadesh.
18 “Pambuyo pake, Aisraeli ananyamuka ulendo kudzera ku chipululu nazungulira dziko la Edomu ndi dziko la Mowabu, ndipo anafika ku mmawa kwa dziko la Mowabu ndi kumanga zinthando zawo ku mbali ina ya mtsinje wa Arinoni. Iwo sanalowe mʼdziko la Mowabu, chifukwa mtsinje wa Arinoni ndiwo unali malire a dziko la Mowabu.
Then they went through the wilderness, and went around the land of Edom, and the land of Moab, and came by the east side of the land of Moab. And they encamped on the other side of the Arnon, but they did not come within the border of Moab, for the Arnon was the border of Moab.
19 “Pambuyo pake Israeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, amene amalamulira ku Hesiboni ndipo anati kwa iye, ‘Chonde tiloleni kuti tidutse mʼdziko lanu popita kwathu.’
And Israel sent messengers to Sihon king of the Amorites, the king of Heshbon. And Israel said to him, Let us pass, we pray thee, through thy land to my place.
20 Koma Sihoni sanalole Israeli kuti adzere mʼdziko mwake. Mʼmalo mwake Sihoni anasonkhanitsa ankhondo ake onse nakamanga msasa ku Yahazi ndipo anachita nkhondo ndi Israeli.
But Sihon did not trust Israel to pass through his border, but Sihon gathered all his people together, and encamped in Jahaz, and fought against Israel.
21 “Koma Yehova Mulungu wa Israeli anamupereka Sihoni pamodzi ndi anthu ake onse mʼmanja mwa Israeli, ndipo anawagonjetsa. Choncho Aisraeli analanda dziko lonse la Aamori amene amakhala mʼdzikolo.
And Jehovah, the God of Israel, delivered Sihon and all his people into the hand of Israel, and they smote them. So Israel possessed all the land of the Amorites, the inhabitants of that country.
22 Analanda dziko lonse kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki ndiponso kuchokera ku chipululu mpaka ku mtsinje wa Yorodani.
And they possessed all the border of the Amorites, from the Arnon even to the Jabbok, and from the wilderness even to the Jordan.
23 “Ndiye kuti Yehova Mulungu wa Aisraeli ndiye analanda dziko la Aamori, kuwalandirira anthu ake. Kodi inu mukufuna kutilanda dzikolo?
So now Jehovah, the God of Israel, has dispossessed the Amorites from before his people Israel, and should thou possess them?
24 Bwanji inu osakhazikika mʼdziko limene Kemosi mulungu wanu anakupatsani, ifenso tikhazikike mʼdziko limene Yehova Mulungu wathu anatipatsa?
Will thou not possess that which Chemosh thy god gives thee to possess? So whomever Jehovah our God has dispossessed from before us, them will we possess.
25 Kodi ndinu abwino kuposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu? Kodi iye anakanganapo kapena kuchita nkhondo ndi Israeli?
And now are thou anything better than Balak the son of Zippor, king of Moab? Did he ever strive against Israel, or did he ever fight against them?
26 Pamene Aisraeli ankakhala mʼdziko la Hesiboni ndi mʼmidzi yake, mʼdziko la Aroeri ndi midzi yake, komanso mʼmizinda yonse imene ili mʼmbali mwa mtsinje wa Arinoni kwa zaka 300, nʼchifukwa chiyani inu simunalande malowo nthawi imeneyo?
While Israel dwelt in Heshbon and its towns, and in Aroer and its towns, and in all the cities that are along by the side of the Arnon, three hundred years, why did ye not recover them within that time?
27 Choncho ine sindinakuchimwireni. Koma inu mukundilakwira pomenyana nane. Yehova woweruza, ndiye aweruze lero mlandu wa pakati pa Aisraeli ndi Aamoni.”
I therefore have not sinned against thee, but thou do me wrong to war against me. Jehovah, the Judge, be judge this day between the sons of Israel and the sons of Ammon.
28 Koma mfumu ya Aamori, sinasamale mawu amene Yefita anatumiza kwa iyo.
However the king of the sons of Ammon did not hearken to the words of Jephthah which he sent him.
29 Tsono Mzimu wa Yehova unatsikira pa Yefita. Ndipo iye ananyamuka nadzera ku Giliyadi ndi ku Manase. Anafika ku Mizipa mʼdziko la Giliyadi, ndipo kuchokera kumeneko anapita kukalimbana ndi Aamoni.
Then the Spirit of Jehovah came upon Jephthah, and he passed over Gilead and Manasseh, and passed over Mizpeh of Gilead, and from Mizpeh of Gilead he passed over to the sons of Ammon.
30 Yefita analumbira kwa Yehova kuti, “Ngati mupereka Aamoni mʼmanja mwanga,
And Jephthah vowed a vow to Jehovah, and said, If thou will indeed deliver the sons of Ammon into my hand,
31 aliyense amene atuluke pa khomo la nyumba yanga kudzandichingamira pobwerera nditagonjetsa Aamoni adzakhala wake wa Yehova, ndipo ndidzamupereka kuti akhale nsembe yopsereza.”
then it shall be, that whatever comes forth from the doors of my house to meet me, when I return in peace from the sons of Ammon, it shall be Jehovah's, and I will offer it up for a burnt offering.
32 Kenaka Yefita anawolokera kwa Aamoni kukamenya nawo nkhondo, ndipo Yehova anawaperekadi mʼmanja mwake.
So Jephthah passed over to the sons of Ammon to fight against them, and Jehovah delivered them into his hand.
33 Iye anawononga mizinda makumi awiri kuchokera ku Ariori mpaka pafupi ndi mzinda wa Miniti. Anapitirira mpaka ku Abeli-Keranimu. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamoni.
And he smote them from Aroer until thou come to Minnith, even twenty cities, and to Abelcheramim, with a very great slaughter. So the sons of Ammon were subdued before the sons of Israel.
34 Pambuyo pake Yefita anabwerera ku nyumba yake. Tsono anangoona mwana wake wamkazi akutuluka kudzamuchingamira akuyimba ngʼoma ndi kuvina. Uyu anali mwana yekhayo wa Yefita. Analibenso mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.
And Jephthah came to Mizpah to his house, and, behold, his daughter came out to meet him with timbrels and with dances. And she was his only child. Besides her he had neither son nor daughter.
35 Yefita ataona mwana wake uja, anangʼamba zovala zake ndi kulira, “Kalanga ine! Mwana wanga! Wandivulaza kwambiri ndipo iwe ndi gwero la mavuto anga. Ine ndinalumbira kwa Yehova ndi pakamwa pangapa ndipo sindingathe kubweza malumbiro angawo.”
And it came to pass, when he saw her, that he tore his clothes, and said, Alas, my daughter! Thou have brought me very low, and thou are one of those who trouble me, for I have opened my mouth to Jehovah, and I cannot go back.
36 Mwanayo anayankha kuti, “Abambo, ngati munalonjeza kwa Yehova ndi pakamwa panu, chitani zimene munalonjezera pakuti Yehova wakuthandizani kulipsira adani anu Amowabu.”
And she said to him, My father, thou have opened thy mouth to Jehovah. Do to me according to that which has proceeded out of thy mouth, inasmuch as Jehovah has taken vengeance for thee on thine enemies, even on the sons of Ammon.
37 Anatinso kwa abambo ake, “Ndikupempheni chinthu ichi: Mundilole ndikayendeyende ku mapiri miyezi iwiri ndizikalira pamodzi ndi anzanga chifukwa ndikufa ndikanali namwali wosadziwa mwamuna.”
And she said to her father, Let this thing be done for me: Let me alone two months, that I may depart and go down upon the mountains, and bewail my virginity, I and my companions.
38 Yefita anamuyankha kuti, “Pita.” Ndipo anamulola kuti apite miyezi iwiri. Tsono anapita kumapiri ndi atsikana anzake kukalira chifukwa cha unamwali wake.
And he said, Go. And he sent her away for two months. And she departed, she and her companions, and bewailed her virginity upon the mountains.
39 Miyezi iwiri itatha iye anabwerera kwa abambo ake, ndipo anachitadi zimene analonjeza. Motero unakhala mwambo wa Aisraeli,
And it came to pass at the end of two months, that she returned to her father, who did with her according to his vow which he had vowed, and she knew no man. And it was a custom in Israel,
40 kuti atsikana a Israeli ankapita chaka chilichonse kukalira maliro a mwana wa mkazi wa Yefita, Mgiliyadi uja masiku makumi anayi pa chaka.
that the daughters of Israel went yearly to celebrate the daughter of Jephthah the Gileadite four days in a year.

< Oweruza 11 >