< Yoswa 4 >

1 Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa,
And it came to pass, when all the nation were clean passed over the Jordan, that Jehovah spoke to Joshua, saying,
2 “Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse.
Take for you twelve men out of the people, a man out of every tribe,
3 Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’”
and command ye them, saying, Take for you here out of the midst of the Jordan, out of the place where the priests' feet stood firm, twelve stones, and carry them over with you, and lay them down in the lodging-place where ye shall lodge this night.
4 Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse,
Then Joshua called the twelve men, whom he had prepared of the sons of Israel, a man out of every tribe.
5 ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli,
And Joshua said to them, Pass over before the ark of Jehovah your God into the midst of the Jordan, and take ye up every man of you a stone upon his shoulder, according to the number of the tribes of the sons of Israel,
6 kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
that this may be a sign among you, that, when your children ask in time to come, saying, What do ye mean by these stones?
7 Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’”
Then ye shall say to them, Because the waters of the Jordan were cut off before the ark of the covenant of Jehovah. When it passed over the Jordan, the waters of the Jordan were cut off. And these stones shall be for a memorial to the sons of Israel forever.
8 Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko.
And the sons of Israel did so as Joshua commanded, and took up twelve stones out of the midst of the Jordan, as Jehovah spoke to Joshua, according to the number of the tribes of the sons of Israel, and they carried them over with them to the place where they lodged, and laid them down there.
9 Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.
And Joshua set up twelve stones in the midst of the Jordan, in the place where the feet of the priests who bore the ark of the covenant stood, and they are there to this day.
10 Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira.
For the priests who bore the ark stood in the midst of the Jordan until everything was finished that Jehovah commanded Joshua to speak to the people, according to all that Moses commanded Joshua. And the people hastened and passed over.
11 Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova.
And it came to pass, when all the people were clean passed over, that the ark of Jehovah passed over, and the priests, in the presence of the people.
12 Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira.
And the sons of Reuben, and the sons of Gad, and the half-tribe of Manasseh, passed over armed before the sons of Israel, as Moses spoke to them.
13 Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.
About forty thousand ready armed for war passed over before Jehovah to battle, to the plains of Jericho.
14 Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.
On that day Jehovah magnified Joshua in the sight of all Israel, and they feared him, as they feared Moses, all the days of his life.
15 Kenaka Yehova anati kwa Yoswa,
And Jehovah spoke to Joshua, saying,
16 “Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”
Command the priests who bear the ark of the testimony, that they come up out of the Jordan.
17 Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.
Joshua therefore commanded the priests, saying, Come ye up out of the Jordan.
18 Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.
And it came to pass, when the priests who bore the ark of the covenant of Jehovah came up out of the midst of the Jordan, and the soles of the priests' feet were lifted up to the dry ground, that the waters of the Jordan returned to their place, and went over all its banks, as formerly.
19 Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko.
And the people came up out of the Jordan on the tenth day of the first month, and encamped in Gilgal on the east border of Jericho.
20 Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija.
And those twelve stones, which they took out of the Jordan, Joshua set up in Gilgal.
21 Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
And he spoke to the sons of Israel, saying, When your sons shall ask their fathers in time to come, saying, What do these stones mean?
22 Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’
Then ye shall let your sons know, saying, Israel came over this Jordan on dry land.
23 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma.
For Jehovah your God dried up the waters of the Jordan from before you, until ye were passed over, as Jehovah your God did to the Red Sea, which he dried up from before us, until we were passed over,
24 Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”
that all the peoples of the earth may know the hand of Jehovah, that it is mighty, that ye may fear Jehovah your God forever.

< Yoswa 4 >