< Yoswa 19 >

1 Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
And the second lot came out for Simeon, even for the tribe of the sons of Simeon according to their families. And their inheritance was in the midst of the inheritance of the sons of Judah.
2 Dzikolo linaphatikiza zigawo izi: Beeriseba (ndi Seba), Molada,
And they had for their inheritance Beersheba, or Sheba, and Moladah,
3 Hazari-Suwali, Bala, Ezemu,
and Hazar-shual, and Balah, and Ezem,
4 Elitoladi, Betuli, Horima,
and Eltolad, and Bethul, and Hormah,
5 Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa,
and Ziklag, and Beth-marcaboth, and Hazar-susah,
6 Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.
and Beth-lebaoth, and Sharuhen; thirteen cities with their villages.
7 Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo.
Ain, Rimmon, and Ether, and Ashan; four cities with their villages;
8 Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera. Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo.
and all the villages that were round about these cities to Baalath-beer, Ramah of the South. This is the inheritance of the tribe of the sons of Simeon according to their families.
9 Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.
The inheritance of the sons of Simeon was out of the part of the sons of Judah, for the portion of the sons of Judah was too much for them. Therefore the sons of Simeon had inheritance in the midst of their inheritance.
10 Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni: Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi.
And the third lot came up for the sons of Zebulun according to their families. And the border of their inheritance was to Sarid,
11 Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu.
and their border went up westward, even to Maralah, and reached to Dabbesheth, and it reached to the brook that is before Jokneam,
12 Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya.
and it turned from Sarid eastward toward the sunrising to the border of Chisloth-tabor, and it went out to Daberath, and went up to Japhia.
13 Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni.
And from there it passed along eastward to Gath-hepher, to Eth-kazin, and it went out at Rimmon which stretches to Neah,
14 Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli.
and the border turned about it on the north to Hannathon. And the goings out of it were at the valley of Iph-tah-el,
15 Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.
and Kattath, and Nahalal, and Shimron, and Idalah, and Bethlehem; twelve cities with their villages.
16 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.
This is the inheritance of the sons of Zebulun according to their families, these cities with their villages.
17 Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara.
The fourth lot came out for Issachar, even for the sons of Issachar according to their families.
18 Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi: Yezireeli, Kesuloti, Sunemu,
And their border was to Jezreel, and Chesulloth, and Shunem,
19 Hafaraimu, Sioni, Anaharati,
and Hapharaim, and Shion, and Anaharath,
20 Rabiti, Kisoni, Ebezi,
and Rabbith, and Kishion, and Ebez,
21 Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi.
and Remeth, and Engannim, and En-haddah, and Beth-pazzez,
22 Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.
and the border reached to Tabor, and Shahazumah, and Beth-shemesh. And the goings out of their border were at the Jordan; sixteen cities with their villages.
23 Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.
This is the inheritance of the tribe of the sons of Issachar according to their families, the cities with their villages.
24 Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri.
And the fifth lot came out for the tribe of the sons of Asher according to their families.
25 Gawo lawo linaphatikiza Helikati, Hali, Beteni, Akisafu,
And their border was Helkath, and Hali, and Beten, and Achshaph,
26 Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati.
and Allammelech, and Amad, and Mishal, and it reached to Carmel westward, and to Shihor-libnath,
27 Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli,
and it turned toward the sunrising to Beth-dagon, and reached to Zebulun, and to the valley of Iph-tah-el northward to Beth-emek and Neiel, and it went out to Cabul on the left hand,
28 Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu.
and Ebron, and Rehob, and Hammon, and Kanah, even to great Sidon,
29 Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu,
and the border turned to Ramah, and to the fortified city of Tyre, and the border turned to Hosah. And the goings out of it were at the sea by the region of Achzib,
30 Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.
also Ummah, and Aphek, and Rehob; twenty-two cities with their villages.
31 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.
This is the inheritance of the tribe of the sons of Asher according to their families, these cities with their villages.
32 Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.
The sixth lot came out for the sons of Naphtali, even for the sons of Naphtali according to their families.
33 Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani.
And their border was from Heleph, from the oak in Zaanannim, and Adam-inekeb, and Jabneel, to Lakkum. And the goings out of it were at the Jordan.
34 Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa.
And the border turned westward to Aznoth-tabor, and went out from there to Hukkok, and it reached to Zebulun on the south, and reached to Asher on the west, and to Judah at the Jordan toward the sunrising.
35 Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti,
And the fortified cities were Ziddim, Zer, and Hammath, Rakkath, and Chinnereth,
36 Adama, Rama, Hazori,
and Adamah, and Ramah, and Hazor,
37 Kedesi, Ederi, Eni Hazori,
and Kedesh, and Edrei, and En-hazor,
38 Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.
and Iron, and Migdal-el, Horem, and Beth-anath, and Beth-shemesh; nineteen cities with their villages.
39 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.
This is the inheritance of the tribe of the sons of Naphtali according to their families, the cities with their villages.
40 Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani.
The seventh lot came out for the tribe of the sons of Dan according to their families.
41 Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi: Zora, Esitaoli, Iri Semesi,
And the border of their inheritance was Zorah, and Eshtaol, and Ir-shemesh,
42 Saalabini, Ayaloni, Itira,
and Shaalabbin, and Aijalon, and Ithlah,
43 Eloni, Timna, Ekroni,
and Elon, and Timnah, and Ekron,
44 Eliteke, Gibetoni, Baalati,
and Eltekeh, and Gibbethon, and Baalath,
45 Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni,
and Jehud, and Bene-berak, and Gath-rimmon,
46 Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.
and Me-jarkon, and Rakkon, with the border opposite Joppa.
47 Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.
And the border of the sons of Dan went out beyond them, for the sons of Dan went up and fought against Leshem, and took it, and smote it with the edge of the sword, and possessed it, and dwelt in it, and called Leshem, Dan, after the name of Dan their father.
48 Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.
This is the inheritance of the tribe of the sons of Dan according to their families, these cities with their villages.
49 Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake.
So they made an end of distributing the land for inheritance by the borders of it. And the sons of Israel gave an inheritance to Joshua the son of Nun in the midst of them.
50 Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.
According to the commandment of Jehovah they gave him the city which he asked, even Timnath-serah in the hill-country of Ephraim. And he built the city, and dwelt in it.
51 Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.
These are the inheritances, which Eleazar the priest, and Joshua the son of Nun, and the heads of the fathers of the tribes of the sons of Israel, distributed for inheritance by lot in Shiloh before Jehovah, at the door of the tent of meeting. So they made an end of dividing the land.

< Yoswa 19 >