< Yobu 20 >

1 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
Then Zophar the Naamathite answered and said,
2 “Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
“My thoughts make me answer quickly because of the worry that is in me.
3 Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
I hear a rebuke that dishonors me, but a spirit from my understanding answers me.
4 “Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
Do you not know this fact from ancient times, when God placed man on earth:
5 kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
the triumph of a wicked man is short, and the joy of a godless man lasts only for a moment?
6 Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
Though his height reaches up to the heavens, and his head reaches to the clouds,
7 iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
yet such a person will perish permanently like his own feces; those who have seen him will say, 'Where is he?'
8 Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
He will fly away like a dream and will not be found; indeed, he will be chased away like a vision of the night.
9 Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
The eye that saw him will see him no more; his place will see him no longer.
10 Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
His children will apologize to poor people; his hands will have to give back his wealth.
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
His bones are full of youthful strength, but it will lie down with him in the dust.
12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
Although wickedness is sweet in his mouth, although he hides it under his tongue,
13 ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
although he holds it there and does not let it go but keeps it still in his mouth—
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
the food in his intestines turns bitter; it becomes the poison of asps inside him.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
He swallows down riches, but he will vomit them up again; God will cast them out of his stomach.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
He will suck the poison of asps; the viper's tongue will kill him.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
He will not enjoy the streams, the torrents of honey and butter.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
He will give back the fruit of his labor and will not be able to eat it; he will not enjoy the wealth earned by his commerce.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
For he has oppressed and neglected poor people; he has violently taken away houses that he did not build.
20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
Because he has known no satisfaction himself, he will not be able to save anything in which he takes pleasure.
21 Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
There is nothing left that he did not devour; therefore his prosperity will not be permanent.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
In the abundance of his wealth he will fall into trouble; the hand of everyone who is in poverty will come against him.
23 Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
When he is about to fill his stomach, God will throw the fierceness of his wrath on him; God will rain it down on him while he is eating.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
Although that man will flee from the iron weapon, a bow of bronze will shoot him.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
He pulls it out of his back and the gleaming point comes out of his liver. Terrors come over him.
26 mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
Complete darkness is reserved for his treasures; a fire not fanned will devour him; it will consume what is left in his tent.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
The heavens will reveal his iniquity, and the earth will rise up against him as a witness.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
The wealth of his house will vanish; his goods will flow away on the day of God's wrath.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”
This is the wicked man's portion from God, the heritage reserved for him by God.”

< Yobu 20 >