< Yobu 19 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered and said,
2 “Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti, ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
“How long will you make me suffer and break me into pieces with words?
3 Inuyo mwandinyoza kwambiri; mwanditsutsa mopanda manyazi.
These ten times you have reproached me; you are not ashamed that you have treated me harshly.
4 Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera, cholakwachotu nʼchanga.
If it is indeed true that I have erred, my error remains my own concern.
5 Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga, ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
If indeed you will exalt yourselves above me and use my humiliation against me,
6 pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira ndipo wandizinga ukonde wake.
then you should know that God has done wrong to me and has caught me in his net.
7 “Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha; ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
See, I cry out, “Violence!” but I get no answer. I call out for help, but there is no justice.
8 Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa; waphimba njira zanga ndi mdima.
He has walled up my way so that I cannot pass, and he has set darkness in my path.
9 Iye wandilanda ulemu wanga ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
He has stripped me of my glory, and he has taken the crown from my head.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu; Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
He has broken me down on every side, and I am gone; he has pulled up my hope like a tree.
11 Wandikwiyira ndipo akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
He has also kindled his wrath against me; he regards me as one of his adversaries.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu, akonzekera zodzalimbana nane ndipo azungulira nyumba yanga.
His troops come on together; they cast up siege mounds against me and encamp around my tent.
13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga; wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
He has put my brothers far from me; my acquaintances are wholly alienated from me.
14 Abale anga andithawa; abwenzi anga andiyiwala.
My kinsfolk have failed me; my close friends have forgotten me.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo; ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
Those who once stayed as guests in my house and my female servants regard me as a stranger; I am an alien in their sight.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha, ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
I call to my servant, but he gives me no answer although I entreat him with my mouth.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga; ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
My breath is offensive to my wife; I am even disgusting to those who were born from my mother's womb.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza; akandiona amandinyodola.
Even young children despise me; if I rise to speak, they speak against me.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane; iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
All my familiar friends abhor me; those whom I love have turned against me.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha; ndapulumuka lokumbakumba.
My bones cling to my skin and to my flesh; I survive only by the skin of my teeth.
21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni, pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
Have pity upon me, have pity upon me, my friends, for the hand of God has touched me.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu? Kodi simunatope nalo thupi langa?
Why do you pursue me like God does? Will you ever be satisfied with my flesh?
23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa, achikhala analembedwa mʼbuku,
Oh, that my words were now written down! Oh, that they were inscribed in a book!
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo, akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
Oh, that with an iron pen and lead they were engraved in the rock forever!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo, ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
But as for me, I know that my Redeemer lives, and that at last he will stand on the earth;
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka, mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
after my skin, that is, this body, is destroyed, then in my flesh I will see God.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi. Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!
I will see him with my own eyes—I, and not someone else. My heart fails within me.
28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji, popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
If you say, 'How we will persecute him! The root of his troubles lies in him,'
29 Inu muyenera kuopa lupanga; pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga; zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”
then be afraid of the sword, because wrath brings the punishment of the sword, so that you may know there is a judgment.”

< Yobu 19 >