< Yeremiya 43 >

1 Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze,
And it came to pass that, when Jeremiah had made an end of speaking to all the people all the words of Jehovah their God, with which Jehovah their God had sent him to them, even all these words,
2 Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’
then Azariah the son of Hoshaiah, and Johanan the son of Kareah, and all the proud men, spoke, saying to Jeremiah, Thou speak falsely. Jehovah our God has not sent thee to say, Ye shall not go into Egypt to sojourn there.
3 Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”
But Baruch the son of Neriah set upon thee against us, to deliver us into the hand of the Chaldeans, that they may put us to death, and carry us away captive to Babylon.
4 Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda.
So Johanan the son of Kareah, and all the captains of the forces, and all the people, did not obey the voice of Jehovah, to dwell in the land of Judah.
5 Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako.
But Johanan the son of Kareah, and all the captains of the forces, took all the remnant of Judah, who were returned from all the nations where they had been driven to sojourn in the land of Judah,
6 Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya.
the men, and the women, and the sons, and the king's daughters, and every person that Nebuzaradan the captain of the guard had left with Gedaliah the son of Ahikam, the son of Shaphan, and Jeremiah the prophet, and Baruch the son of Neriah,
7 Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.
and they came into the land of Egypt, for they did not obey the voice of Jehovah. And they came to Tahpanhes.
8 Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti,
Then the word of Jehovah came to Jeremiah in Tahpanhes, saying,
9 “Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona.
Take great stones in thy hand, and hide them in mortar in the brickwork, which is at the entry of Pharaoh's house in Tahpanhes, in the sight of the men of Judah,
10 Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi.
and say to them, Thus says Jehovah of hosts, the God of Israel: Behold, I will send and take Nebuchadrezzar the king of Babylon, my servant, and will set his throne upon these stones that I have hid, and he shall spread his royal pavilion over them.
11 Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
And he shall come, and shall smite the land of Egypt, such as are for death, to death, and such as are for captivity, to captivity, and such as are for the sword, to the sword.
12 Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere.
And I will kindle a fire in the houses of the gods of Egypt, and he shall burn them, and carry them away captive. And he shall array himself with the land of Egypt as a shepherd puts on his garment, and he shall go forth from there in peace.
13 Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’”
He shall also break the pillars of Beth-shemesh that is in the land of Egypt. And the houses of the gods of Egypt he shall burn with fire.

< Yeremiya 43 >