< Yeremiya 4 >

1 “Ngati mukufuna kubwerera, inu Aisraeli, bwererani kwa Ine,” akutero Yehova. “Chotsani mafano anu onyansa pamaso panga ndipo musasocherenso.
If thou will return, O Israel, says Jehovah, if thou will return to me, and if thou will put away thine abominations out of my sight, then thou shall not be removed.
2 Muzilumbira mokhulupirika ndiponso mwa chilungamo kuti, ‘Pali Yehova wamoyo.’ Mukatero anthu a mitundu ina yonse adzandipempha kuti ndiwadalitse ndipo adzanditamanda.”
And thou shall swear, As Jehovah lives, in truth, in justice, and in righteousness. And the nations shall bless themselves in him, and in him they shall glory.
3 Zimene Yehova akunena kwa anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu ndi izi: “Limani masala anu musadzale pakati pa minga.
For thus says Jehovah to the men of Judah and to Jerusalem, Break up your fallow ground, and sow not among thorns.
4 Dziperekeni nokha kwa Ine kuti munditumikire ndi mtima wanu wonse, inu anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu. Muzichita zimenezi kuopa kuti mkwiyo wanga ungabuke ngati moto ndi kukutenthani, chifukwa cha ntchito zanu zoyipazo popanda wina wowuzimitsa.
Circumcise yourselves to Jehovah, and take away the foreskins of your heart, ye men of Judah and inhabitants of Jerusalem, lest my wrath go forth like fire, and burn so that none can quench it, because of the evil of your doings.
5 “Lengeza ku Yuda ndi kulalikira mu Yerusalemu kuti, ‘Lizani lipenga mʼdziko lonse!’ Ndipo fuwulani kuti, ‘Sonkhanani! Tiyeni tithawire ku mizinda yotetezedwa!’
Declare ye in Judah, and publish in Jerusalem, and say, Blow ye the trumpet in the land. Cry aloud and say, Assemble yourselves, and let us go into the fortified cities.
6 Kwezani mbendera kuyangʼana ku Ziyoni! Musachedwe, thawani kuti mupulumuke! Pakuti Ine ndikubweretsa chilango kuchokera kumpoto, kudzakhala chiwonongeko choopsa.”
Set up a standard toward Zion. Flee for safety, do not stay. For I will bring evil from the north, and a great destruction.
7 Monga mkango umatulukira mʼngaka yake momwemonso wowononga mayiko wanyamuka ndi kutuluka ku mbuto yake. Watero kuti awononge dziko lanu. Mizinda yanu idzakhala mabwinja popanda wokhalamo.
A lion has gone up from his thicket, and a destroyer of nations. He is on his way, he has gone forth from his place, to make thy land desolate, that thy cities be laid waste, without inhabitant.
8 Choncho valani ziguduli, lirani ndi kubuwula, pakuti mkwiyo waukulu wa Yehova sunatichokere.
For this gird you with sackcloth, lament and wail, for the fierce anger of Jehovah is not turned back from us.
9 “Pa tsiku limenelo, mfumu ndi nduna zake adzataya mtima, ansembe adzachita mantha kwambiri, ndipo aneneri adzathedwa nzeru,” akutero Yehova.
And it shall come to pass at that day, says Jehovah, that the heart of the king shall perish, and the heart of the rulers, and the priests shall be astonished, and the prophets shall wonder.
10 Ndipo ine ndinati, “Haa, Ambuye Yehova, ndithu munawanyenga anthu awa pamodzi ndi Yerusalemu pamene munanena kuti, ‘Mudzakhala pa mtendere,’ chonsecho lupanga lili pakhosi pathu.”
Then I said, Ah, lord Jehovah! Surely thou have greatly deceived this people and Jerusalem, saying, Ye shall have peace, whereas the sword reaches to the life.
11 Nthawi imeneyo anthu awa ndi Yerusalemu adzawawuza kuti, “Mphepo yotentha yochokera ku magomo a mʼchipululu ikuwomba pa anthu anga, osati mphepo yopeta kapena yoyeretsa;
At that time it shall be said to this people and to Jerusalem, A hot wind from the bare heights in the wilderness toward the daughter of my people, not to winnow, nor to cleanse,
12 koma mphepo yamphamvu kwambiri yochokera kwa Ine. Tsono ndi Ineyo amene ndikuwaweruza.”
a full wind from these shall come for me. Now I will also utter judgments against them.
13 Taonani, adani akubwera ngati mitambo, magaleta awo akubwera ngati kamvuluvulu, akavalo awo ndi aliwiro kupambana chiwombankhanga. Tsoka ilo! Tawonongeka!
Behold, he shall come up as clouds, and his chariots as the whirlwind. His horses are swifter than eagles. Woe to us! For we are ruined.
14 Iwe Yerusalemu, tsuka mtima wako kuchotsa zoyipa kuti upulumuke. Kodi maganizo ako oyipawo udzakhala nawo mpaka liti?
O Jerusalem, wash thy heart from wickedness, that thou may be saved. How long shall thine evil thoughts lodge within thee?
15 Pakuti amithenga akulalika mawu mʼdziko la Dani; akulengeza za masautso kuchokera ku mapiri a Efereimu.
For a voice declares from Dan, and publishes evil from the hills of Ephraim:
16 Iwo akuti, “Fotokozani zimenezi kwa anthu a mitundu ina, lengezani zimenezi mu Yerusalemu kuti, ‘Ankhondo akubwera kuchokera ku dziko lakutali, akufuwula ndi kudzazinga mizinda ya Yuda.
Make ye mention to the nations. Behold, publish against Jerusalem, that watchers come from a far country, and give out their voice against the cities of Judah.
17 Azinga Yerusalemu ngati anthu olondera munda, chifukwa Yerusalemu wandiwukira,’” akutero Yehova.
They are as keepers of a field against her round about, because she has been rebellious against me, says Jehovah.
18 “Makhalidwe anu ndi zochita zanu zakubweretserani zimenezi. Chimenechi ndiye chilango chanu. Nʼchowawa kwambiri! Nʼcholasa mpaka mu mtima!”
Thy way and thy doings have procured these things to thee. This is thy wickedness, for it is bitter, for it reaches to thy heart.
19 Mayo, mayo, ndikumva kupweteka! Aa, mtima wanga ukupweteka, ukugunda kuti thi, thi, thi. Sindingathe kukhala chete. Pakuti ndamva kulira kwa lipenga; ndamva mfuwu wankhondo.
My anguish, my anguish! I am pained at my very heart. My heart is disquieted in me. I cannot hold my peace, because thou have heard, O my soul, the sound of the trumpet, the alarm of war.
20 Tsoka limatsata tsoka linzake; dziko lonse lasanduka bwinja. Mwadzidzidzi matenti athu awonongedwa, mwa kanthawi kochepa nsalu zake zotchinga zagwetsedwa.
Destruction upon destruction is cried, for the whole land is laid waste. Suddenly my tents are destroyed, and my curtains in a moment.
21 Kodi ndikhale ndikuona mbendera ya nkhondo, ndi kumva kulira kwa lipenga mpaka liti?
How long shall I see the standard, and hear the sound of the trumpet?
22 Yehova akuti, “Anthu anga ndi zitsiru; iwo sandidziwa. Iwo ndi ana opanda nzeru; samvetsa chilichonse. Ali ndi luso lochita zoyipa, koma sadziwa kuchita zabwino.”
For my people are foolish. They do not know me. They are sottish sons, and they have no understanding. They are wise to do evil, but to do good they have no knowledge.
23 Ndinayangʼana dziko lapansi, ndipo linali lopanda anthu ndi lopanda kanthu; ndinayangʼana thambo, koma linalibe kuwala kulikonse.
I beheld the earth, and, lo, it was waste and void, and the heavens, and they had no light.
24 Ndinayangʼana mapiri, ndipo ankagwedezeka; magomo onse ankangosunthira uku ndi uku.
I beheld the mountains, and, lo, they trembled, and all the hills moved to and fro.
25 Ndinayangʼana, ndipo sindinaone anthu; mbalame iliyonse ya mlengalenga inali itathawa.
I beheld, and, lo, there was no man, and all the birds of the heavens were fled.
26 Ndinayangʼana, dziko lachonde linali litasanduka chipululu; mizinda yake yonse inali itasanduka bwinja pamaso pa Yehova, chifukwa cha mkwiyo wake.
I beheld, and, lo, the fruitful field was a wilderness, and all the cities thereof were broken down at the presence of Jehovah, and before his fierce anger.
27 Yehova akuti, “Dziko lonse lidzasanduka chipululu komabe sindidzaliwononga kotheratu.
For thus says Jehovah: The whole land shall be a desolation, yet I will not make a full end.
28 Chifukwa chake dziko lapansi lidzalira ndipo thambo lidzachita mdima, pakuti ndayankhula ndipo sindidzafewa mtima, ndatsimikiza ndipo sindidzabwerera mʼmbuyo.”
For this the earth shall mourn, and the heavens above be black, because I have spoken it, I have purposed it, and I have not relented, nor will I turn back from it.
29 Pakumva phokoso la okwera pa akavalo ndi la anthu oponya mivi, anthu a mʼmizinda adzathawa. Ena adzabisala ku nkhalango; ena adzakwera mʼmatanthwe mizinda yonse nʼkuyisiya; popanda munthu wokhalamo.
Every city flees for the noise of the horsemen and bowmen. They go into the thickets, and climb up upon the rocks. Every city is forsaken, and not a man dwells in it.
30 Iwe Yerusalemu, ndiwe bwinja! Ukutanthauza chiyani kuvala zovala zofiira ndi kuvalanso zokometsera zagolide? Ngakhale udzikonze maso ako powapaka zokometsera, ukungodzivuta chabe. Zibwenzi zako zikukunyoza; zikufuna kuchotsa moyo wako.
And thou, when thou are made desolate, what will thou do? Though thou clothe thyself with scarlet, though thou deck thee with ornaments of gold, though thou enlarge thine eyes with paint, in vain thou make thyself fair. Thy lovers despise thee, they seek thy life.
31 Ndikumva kulira ngati kwa mayi pa nthawi yake yobereka, kubuwula ngati kwa mayi amene akubereka mwana wake woyamba. Kuliraku ndi kwa anthu a mu Ziyoni, wefuwefu. Atambalitsa manja awo nʼkumati, “Kalanga ife! Tikukomoka. Moyo wathu waperekedwa kwa anthu otipha.”
For I have heard a voice as of a woman in travail, the anguish as of her who brings forth her first child, the voice of the daughter of Zion, who gasps for breath, who spreads her hands, saying, Woe is me now! For my soul faints before the murderers.

< Yeremiya 4 >