< Yeremiya 30 >

1 Yehova anawuza Yeremiya kuti,
The word that came to Jeremiah from Jehovah, saying,
2 “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza.
Thus speaks Jehovah, the God of Israel, saying, Write thee all the words that I have spoken to thee in a book.
3 Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”
For, lo, the days come, says Jehovah, that I will turn again the captivity of my people Israel and Judah, says Jehovah, and I will cause them to return to the land that I gave to their fathers, and they shall possess it.
4 Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda:
And these are the words that Jehovah spoke concerning Israel and concerning Judah.
5 “Yehova akuti: “Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa, ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.
For thus says Jehovah: We have heard a voice of trembling, of fear, and not of peace.
6 Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti: Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira? Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?
Ask ye now, and see whether a man travails with child. Why do I see every man with his hands on his loins as a woman in travail, and all faces are turned into paleness?
7 Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri! Sipadzakhala lina lofanana nalo. Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo, koma adzapulumuka ku masautsowo.”
Alas! For that day is great, so that none is like it. It is even the time of Jacob's trouble, but he shall be saved out of it.
8 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo, ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo ndipo ndidzadula zingwe zowamanga; Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.
And it shall come to pass in that day, says Jehovah of hosts, that I will break his yoke from off thy neck, and will burst thy bonds. And strangers shall no more make him their bondman,
9 Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo ndiponso Davide mfumu yawo, amene ndidzawasankhira.
but they shall serve Jehovah their God, and David their king, whom I will raise up to them.
10 “‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo; usade nkhawa, iwe Israeli,’ akutero Yehova. ‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali, zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere, ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.
Therefore fear thou not, O Jacob my servant, says Jehovah, nor be dismayed, O Israel. For, lo, I will save thee from afar, and thy seed from the land of their captivity, and Jacob shall return, and shall be quiet and at ease, and none shall make him afraid.
11 Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’ akutero Yehova. ‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu kumene ndinakubalalitsirani, koma inu sindidzakuwonongani kotheratu. Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa. Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’”
For I am with thee, says Jehovah, to save thee. For I will make a full end of all the nations where I have scattered thee, but I will not make a full end of thee. But I will correct thee in measure, and will in no way leave thee unpunished.
12 Yehova akuti, “Chilonda chanu nʼchosachizika, bala lanu ndi lonyeka.
For thus says Jehovah, Thy hurt is incurable, and thy wound grievous.
13 Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu, palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira, palibe mankhwala ochiritsa inu.
There is none to plead thy cause, that thou may be bound up; thou have no healing medicines.
14 Abwenzi anu onse akuyiwalani; sasamalanso za inu. Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira. Ndipo ndakulangani mwa nkhanza, chifukwa machimo anu ndi ambiri, ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.
All who love thee have forgotten thee; they seek thee not. For I have wounded thee with the wound of an enemy, with the chastisement of a cruel one, for the greatness of thine iniquity, because thy sins were increased.
15 Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu? Bala lanu silingapole ayi. Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.
Why do thou cry for thy hurt? Thy pain is incurable, for the greatness of thine iniquity. Because thy sins were increased, I have done these things to thee.
16 “Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa; adani anu onse adzapita ku ukapolo. Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso; onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.
Therefore all those who devour thee shall be devoured, and all thine adversaries, every one of them, shall go into captivity. And those who despoil thee shall be a spoil, and all who prey upon thee I will give for a prey.
17 Ndidzachiza matenda anu ndi kupoletsa zilonda zanu, akutero Yehova, ‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika. Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’”
For I will restore health to thee, and I will heal thee of thy wounds, says Jehovah, because they have called thee an outcast, saying, It is Zion, whom no man seeks after.
18 Yehova akuti, “Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo; mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake, nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.
Thus says Jehovah: Behold, I will turn again the captivity of Jacob's tents, and have compassion on his dwelling-places. And the city shall be built upon its own hill, and the palace shall be inhabited after its own manner.
19 Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo. Ndidzawachulukitsa, ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika; ndidzawapatsa ulemerero, ndipo sadzanyozedwanso.
And out of them shall proceed thanksgiving and the voice of those who make merry. And I will multiply them, and they shall not be few. I will also glorify them, and they shall not be small.
20 Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale, ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga; ndidzalanga onse owazunza.
Their sons also shall be as formerly, and their congregation shall be established before me. And I will punish all who oppress them.
21 Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo. Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo. Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira. Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane popanda kuyitanidwa?” akutero Yehova.
And their prince shall be of themselves, and their ruler shall proceed from the midst of them. And I will cause him to draw near, and he shall approach to me. For who is he who has had boldness to approach to me? says Jehovah.
22 “Choncho inu mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”
And ye shall be my people, and I will be your God.
23 Taonani ukali wa Yehova wowomba ngati mphepo ya mkuntho. Mphepo ya namondwe ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.
Behold, the tempest of Jehovah-wrath-has gone forth, a sweeping tempest. It shall burst upon the head of the wicked.
24 Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka mpaka atakwaniritsa zolinga za mu mtima mwake. Mudzamvetsa zimenezi masiku akubwerawo.
The fierce anger of Jehovah shall not return until he has executed, and till he has performed the intents of his heart. In the latter days ye shall understand it.

< Yeremiya 30 >