< Yeremiya 29 >

1 Yeremiya anatumiza kalata kuchokera ku Yerusalemu kupita kwa akuluakulu amene anali ku ukapolo, ndiponso kwa ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse amene Nebukadinezara anawatenga ku Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Now these are the words of the letter that Jeremiah the prophet sent from Jerusalem to the residue of the elders of the captivity, and to the priests, and to the prophets, and to all the people, whom Nebuchadnezzar had carried away captive from Jerusalem to Babylon,
2 Zimenezi zinachitika mfumu Yekoniya, amayi a mfumu, nduna za mfumu ndiponso atsogoleri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, anthu aluso ndi amisiri atatengedwa ku Yerusalemu kupita ku ukapolo.
(after Jeconiah the king, and the queen-mother, and the eunuchs, and the rulers of Judah and Jerusalem, and the craftsmen, and the smiths, were departed from Jerusalem),
3 Yeremiya anapatsira kalatayo Eleasa mwana wa Safani ndi Gemariya mwana wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatumiza kwa Mfumu Nebukadinezara ku Babuloni. Mʼkalatamo analembamo kuti:
by the hand of Elasah the son of Shaphan, and Gemariah the son of Hilkiah, (whom Zedekiah king of Judah sent to Babylon to Nebuchadnezzar king of Babylon), saying,
4 Anthu onse amene anatengedwa ukapolo kuchokera ku Yerusalemu kupita ku Babuloni, Yehova akuwawuza kuti,
Thus says Jehovah of hosts, the God of Israel, to all the captivity whom I have caused to be carried away captive from Jerusalem to Babylon:
5 “Mangani nyumba ndipo muzikhalamo. Limani minda ndipo mudye zipatso zake.
Build ye houses, and dwell in them, and plant gardens, and eat the fruit of them.
6 Kwatirani ndipo mubereke ana aamuna ndi aakazi. Ana anu aamuna muwasankhire akazi ndipo muwasankhire amuna ana anu aakaziwo, kuti nawonso abale ana aamuna ndi aakazi. Muchulukane kumeneko. Chiwerengero chanu chisachepe.
Take ye wives, and beget sons and daughters. And take wives for your sons, and give your daughters to husbands, that they may bear sons and daughters, and multiply ye there, and be not diminished.
7 Ndiponso muzifunafuna mtendere ndi ubwino wa mzinda umene ndinakupirikitsirani ku ukapoloko. Muzipempherera mzindawo kwa Yehova, kuti zikuyendereni bwino.”
And seek the peace of the city where I have caused you to be carried away captive, and pray to Jehovah for it, for in the peace of it ye shall have peace.
8 Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, “Musalole kuti aneneri ndi owombeza amene ali pakati panu akunyengeni. Musamvere maloto awo.
For thus says Jehovah of hosts, the God of Israel: Let not your prophets who are in the midst of you, and your diviners, deceive you, nor hearken ye to your dreams which ye cause to be dreamed.
9 Iwo akunenera zabodza kwa inu mʼdzina langa ngakhale Ine sindinawatume,” akutero Yehova.
For they prophesy falsely to you in my name. I have not sent them, says Jehovah.
10 Yehova akuti, “Zaka 70 za ku Babuloni zikadzatha, ndidzabwera kudzakuchitirani zabwino zonse zimene ndinakulonjezani zija, ndipo ndidzakubwezerani ku malo ano.
For thus says Jehovah, After seventy years are accomplished for Babylon, I will visit you, and perform my good word toward you in causing you to return to this place.
11 Pakuti Ine ndikudziwa zimene ndinakukonzerani,” akutero Yehova, “ndimalingalira zabwino zokhazokha za inu osati zoyipa, ayi. Ndimalingalira zinthu zokupatsani chiyembekezo chenicheni pa za mʼtsogolo.
For I know the thoughts that I think toward you, says Jehovah, thoughts of peace, and not of evil, to give you hope in your latter end.
12 Nthawi imeneyo mudzandiyitana, ndi kunditama mopemba ndipo ndidzakumverani.
And ye shall call upon me, and ye shall go and pray to me, and I will hearken to you.
13 Mudzandifunafuna ndipo mudzandipeza. Mukadzandifuna ndi mtima wanu wonse
And ye shall seek me, and find me when ye shall search for me with all your heart.
14 mudzandipezadi,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubwezerani zabwino zanu. Ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku mayiko onse ndi kumalo konse kumene munali,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubweretsani kumalo kumene munali ndisanakuchotseni kukupititsani ku ukapolo.”
And I will be found by you, says Jehovah, and I will turn again your captivity. And I will gather you from all the nations, and from all the places where I have driven you, says Jehovah, and I will bring you again to the place from where I caused you to be carried away captive.
15 Inu mumati, “Yehova watiwutsira aneneri athu ku Babuloni,”
Because ye have said, Jehovah has raised us up prophets in Babylon,
16 koma zimene Yehova akunena za mfumu imene ikukhala pa mpando waufumu wa Davide pamodzi ndi anthu onse amene anatsala mu mzinda muno, abale anu amene sanapite nanu ku ukapolo ndi izi,
thus says Jehovah concerning the king who sits upon the throne of David, and concerning all the people who dwell in this city, your brothers who have not gone forth with you into captivity,
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawapha ndi nkhondo, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa ngati nkhuyu zowola kwambiri, zosati nʼkudya.
thus says Jehovah of hosts: Behold, I will send upon them the sword, the famine, and the pestilence, and will make them like vile figs, that cannot be eaten they are so bad.
18 Ndidzawalondola ndi lupanga, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa anthu amayiko onse a pa dziko lapansi. Adzakhala otembereredwa, ochititsa mantha, onyozeka ndiponso ochitidwa chipongwe pakati pa anthu a mitundu yonse kumene ndawapirikitsirako.
And I will pursue after them with the sword, with the famine, and with the pestilence, and will deliver them to be tossed to and fro among all the kingdoms of the earth, to be an execration, and an astonishment, and a hissing, and a reproach, among all the nations where I have driven them,
19 Zidzatero chifukwa sanamvere mawu anga amene ndinkawatumizira kudzera mwa atumiki anga, aneneri. Ngakhale inu amene muli ku ukapolo simunamverenso,” akutero Yehova.
because they have not hearkened to my words, says Jehovah, with which I sent to them my servants the prophets, rising up early and sending them. But ye would not hear, says Jehovah.
20 Choncho, imvani mawu a Yehova, inu akapolo nonse amene ndinakuchotsani mu Yerusalemu ndi kukupititsani ku Babuloni.
Hear ye therefore the word of Jehovah, all ye of the captivity whom I have sent away from Jerusalem to Babylon.
21 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti zokhudza Ahabu mwana wa Kolaya ndi Zedekiya mwana wa Maseya, amene akulosera zabodza kwa inu mʼdzina langa: “Taonani ndidzawapereka kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzawapha inu mukupenya.
Thus says Jehovah of hosts, the God of Israel, concerning Ahab the son of Kolaiah, and concerning Zedekiah the son of Maaseiah, who prophesy a lie to you in my name. Behold, I will deliver them into the hand of Nebuchadrezzar king of Babylon, and he shall kill them before your eyes.
22 Chifukwa cha anthu awiriwo, akapolo onse ochokera ku Yuda amene ali ku Babuloni adzagwiritsa ntchito mawu awa potemberera: ‘Yehova achite nawe monga mmene anachitira ndi Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babuloni inawatentha.’
And of them shall be taken up a curse by all the captives of Judah that are in Babylon, saying, Jehovah make thee like Zedekiah and like Ahab, whom the king of Babylon roasted in the fire,
23 Pakuti anthu amenewa achita zoyipa kwambiri mu Israeli; achita chigololo ndi akazi a eni ake ndipo mʼdzina langa ankayankhula zabodza zimene sindinawawuze kuti atero. Ine ndikuzidziwa ndipo ndine mboni ya zimenezi,” akutero Yehova.
because they have wrought folly in Israel, and have committed adultery with their neighbors' wives, and have spoken words in my name falsely, which I did not command them. And I am he who knows, and am witness, says Jehovah.
24 Ukamuwuze Semaya wa ku Nehelamu kuti,
And concerning Shemaiah the Nehelamite thou shall speak, saying,
25 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Iwe unatumiza kalata mʼdzina lako kwa anthu onse a mu Yerusalemu, kwa Zefaniya mwana wa wansembe Maseya, ndi kwa ansembe onse. Unalemba mu kalatayo kuti,
Thus speaks Jehovah of hosts, the God of Israel, saying, Because thou have sent letters in thine own name to all the people who are at Jerusalem, and to Zephaniah the son of Maaseiah, the priest, and to all the priests, saying,
26 ‘Yehova wakusankha kukhala wansembe mʼmalo mwa Yehoyada kuti ukhale wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Yehova. Munthu aliyense wamisala amene akudziyesa kuti ndi mneneri uzimuponya mʼndende ndi kumuveka goli lachitsulo.
Jehovah has made thee priest in the stead of Jehoiada the priest, that there may be officers in the house of Jehovah, for every man who is mad, and makes himself a prophet, that thou should put him in the stocks and in shackles.
27 Nanga tsono chifukwa chiyani simunamuchitire zimenezi Yeremiya wa ku Anatoti, amene amakhala ngati mneneri pakati panu?
Now therefore, why have thou not rebuked Jeremiah of Anathoth, who makes himself a prophet to you,
28 Yeremiyayo watitumizira uthenga uwu kuno ku Babuloni: Ukapolo wanu ukhala wa nthawi yayitali. Choncho mangani nyumba ndipo muzikhalamo; limani minda ndipo mudye zipatso zake.’”
inasmuch as he has sent to us in Babylon, saying, It is long. Build ye houses, and dwell in them, and plant gardens, and eat the fruit of them?
29 Koma wansembe Zefaniya anayiwerenga kalatayo pamaso pa mneneri Yeremiya.
And Zephaniah the priest read this letter in the ears of Jeremiah the prophet.
30 Ndipo Yehova anawuza Yeremiya kuti,
Then the word of Jehovah came to Jeremiah, saying,
31 “Tumiza uthenga uwu kwa akapolo onse: ‘Yehova akuti zokhudza Semaya wa ku Nehelamu: Semaya wakuloserani, ngakhale kuti Ine sindinamutume, ndipo wakunyengani kuti muzikhulupirira bodza.
Send to all those of the captivity, saying, Thus says Jehovah concerning Shemaiah the Nehelamite: Because Shemaiah has prophesied to you, and I did not send him, and he has caused you to trust in a lie,
32 Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti: Mʼbanja lakelo sipadzakhala munthu pakati pa mtundu uno wa anthu amene adzaone zinthu zabwino zimene ndidzachitira anthu anga chifukwa analalika zondiwukira,’” akutero Yehova.
therefore thus says Jehovah: Behold, I will punish Shemaiah the Nehelamite, and his seed. He shall not have a man to dwell among this people, nor shall he behold the good that I will do to my people, says Jehovah, because he has spoken rebellion against Jehovah.

< Yeremiya 29 >