< Yesaya 60 >

1 “Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
Arise, shine, for thy light has come, and the glory of Jehovah has risen upon thee.
2 Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
For, behold, darkness shall cover the earth, and gross darkness the peoples. But Jehovah will arise upon thee, and his glory shall be seen upon thee.
3 Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
And nations shall come to thy light, and kings to the brightness of thy rising.
4 “Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
Lift up thine eyes round about, and see. They all gather themselves together. They come to thee. Thy sons shall come from far, and thy daughters shall be carried in the arms.
5 Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
Then thou shall see and be radiant, and thy heart shall thrill and be enlarged, because the abundance of the sea shall be turned to thee. The wealth of the nations shall come to thee.
6 Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
The multitude of camels shall cover thee. The dromedaries of Midian and Ephah, all those from Sheba shall come. They shall bring gold and frankincense, and shall proclaim the praises of Jehovah.
7 Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
All the flocks of Kedar shall be gathered together to thee. The rams of Nebaioth shall minister to thee. They shall come up with acceptance on my altar, and I will glorify the house of my glory.
8 “Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
Who are these that fly as a cloud, and as the doves to their windows?
9 Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
Surely the isles shall wait for me, and the ships of Tarshish first, to bring thy sons from far, their silver and their gold with them, for the name of Jehovah thy God, and for the Holy One of Israel, because he has glorified thee.
10 “Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
And foreigners shall build up thy walls, and their kings shall minister to thee. For in my wrath I smote thee, but in my favor I have had mercy on thee.
11 Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
Thy gates also shall be open continually. They shall not be shut day nor night, that men may bring to thee the wealth of the nations, and their kings led captive.
12 Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
For that nation and kingdom that will not serve thee shall perish. Yea, those nations shall be utterly wasted.
13 “Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
The glory of Lebanon shall come to thee, the fir tree, the pine, and the box tree together, to beautify the place of my sanctuary. And I will make the place of my feet glorious.
14 Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
And the sons of those who afflicted thee shall come bending to thee. And all those who despised thee shall bow themselves down at the soles of thy feet. And they shall call thee The city of Jehovah, The Zion of the Holy One of Israel.
15 “Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
Whereas thou have been forsaken and hated, so that no man passed through thee, I will make thee an eternal excellency, a joy of many generations.
16 Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
Thou shall also suck the milk of the nations, and shall suck the breast of kings. And thou shall know that I, Jehovah, am thy Savior, and thy Redeemer, the Mighty One of Jacob.
17 Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
For brass I will bring gold, and for iron I will bring silver, and for wood brass, and for stones iron. I will also make thy officers peace, and thine overseers righteousness.
18 Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
Violence shall no more be heard in thy land, desolation nor destruction within thy borders, but thou shall call thy walls Salvation, and thy gates Praise.
19 Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
The sun shall no more be thy light by day, nor for brightness shall the moon give light to thee, but Jehovah will be to thee an everlasting light, and thy God thy glory.
20 Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
Thy sun shall no more go down, nor shall thy moon withdraw itself, for Jehovah will be thine everlasting light. And the days of thy mourning shall be ended.
21 Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
Thy people also shall all be righteous. They shall inherit the land forever, the branch of my planting, the work of my hands, that I may be glorified.
22 Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”
The little one shall become a thousand, and the small one a strong nation. I, Jehovah, will hasten it in its time.

< Yesaya 60 >