< Yesaya 5 >

1 Ndidzamuyimbira bwenzi langa nyimbo yokamba za munda wake wa mpesa: Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa pa phiri la nthaka yachonde.
Let me sing for my well-beloved a song of my beloved concerning his vineyard. My well-beloved had a vineyard in a very fruitful hill.
2 Anatipula nachotsa miyala yonse ndipo anawokamo mipesa yabwino kwambiri. Anamanga nsanja yolondera pakati pa mundawo ndipo anasemanso mopsinyira mphesa mʼmundamo. Ndipo iye anayembekezera kuti mundawo udzabala mphesa zabwino, koma ayi, unabala mphesa zosadya.
And he dug it, and gathered out the stones of it, and planted it with the choicest vine, and built a tower in the midst of it, and also hewed out a winepress in it. And he looked that it should bring forth grapes, and it brought forth wild grapes.
3 “Tsopano, inu amene mumakhala mu Yerusalemu ndi inu anthu a ku Yuda, weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.
And now, O inhabitants of Jerusalem and men of Judah, judge, I pray you, between me and my vineyard.
4 Kodi nʼchiyaninso china chimene ndikanachitira munda wanga wa mpesa kupambana chomwe ndawuchitira kale? Pamene ndinkayembekezera kuti udzabala mphesa zabwino, bwanji unabala mphesa zosadya?
What could have been done more to my vineyard that I have not done in it? Why, when I looked that it should bring forth grapes, it brought forth wild grapes?
5 Tsopano ndikuwuzani chimene ndidzawuchitire munda wanga wa mpesa: ndidzachotsa mpanda wake, ndipo mundawo udzawonongeka; ndidzagwetsa khoma lake, ndipo nyama zidzapondapondamo.
And now I will tell you what I will do to my vineyard. I will take away the hedge of it, and it shall be eaten up. I will break down the wall of it, and it shall be trodden down.
6 Ndidzawusandutsa tsala, udzakhala wosatengulira ndi wosalimira ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina. Ndidzalamula mitambo kuti isagwetse mvula pa mundapo.”
And I will lay it waste. It shall not be pruned nor hoed, but there shall come up briers and thorns. I will also command the clouds that they rain no rain upon it.
7 Munda wamphesa wa Yehova Wamphamvuzonse ndi Aisraeli, ndipo anthu a ku Yuda ndiwo minda yake yomukondweretsa. Ndipo Iye ankayembekezera chiweruzo cholungama, mʼmalo mwake anaona kuphana; mʼmalo mwa chilungamo Iye anamva kulira kwa anthu ozunzika.
For the vineyard of Jehovah of hosts is the house of Israel, and the men of Judah his pleasant plant. And he looked for justice, but behold, oppression, for righteousness, but behold, a cry.
8 Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba, ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda, mpaka mutalanda malo onse kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.
Woe to those who join house to house, who lay field to field, till there is no room, and ye be made to dwell alone in the midst of the land!
9 Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti, “Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja, nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.
In my ears says Jehovah of hosts, of a truth many houses shall be desolate, even great and fair, without inhabitant.
10 Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi, kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”
For ten acres of vineyard shall yield one bath, and a homer of seed shall yield but an ephah.
11 Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa nathamangira chakumwa choledzeretsa, amene amamwa mpaka usiku kufikira ataledzera kotheratu.
Woe to those who rise up early in the morning, that they may follow strong drink, who tarry late into the night, till wine inflame them!
12 Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe, matambolini, zitoliro ndi vinyo, ndipo sasamala ntchito za Yehova, salemekeza ntchito za manja ake.
And the harp and the lute, the tambourine and the pipe, and wine, are in their feasts, but they do not regard the work of Jehovah, nor have they considered the operation of his hands.
13 Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo chifukwa cha kusamvetsa zinthu; atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala, ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.
Therefore my people have gone into captivity for lack of knowledge, and their honorable men are famished, and their multitude are parched with thirst.
14 Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake; mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka; adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko. (Sheol h7585)
Therefore Sheol has enlarged its desire, and opened its mouth without measure. And their glory, and their multitude, and their pomp, and he who rejoices among them, descend into it. (Sheol h7585)
15 Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa, anthu onse adzachepetsedwa, anthu odzikuza adzachita manyazi.
And the common man is bowed down, and the great man is debased, and the eyes of the lofty are humbled,
16 Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama. Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.
but Jehovah of hosts is exalted in justice, and God the Holy One is sanctified in righteousness.
17 Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo; ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.
Then the lambs shall feed as in their pasture, and wanderers shall eat the waste places of the fat ones.
18 Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo, ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,
Woe to those who draw iniquity with cords of falsehood, and sin as it were with a cart rope,
19 amene amanena kuti, “Yehova afulumire, agwire ntchito yake mwamsanga kuti ntchitoyo tiyione. Ntchito zionekere, zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita, zichitike kuti tizione.”
who say, Let him make speed, let him hasten his work, that we may see it. And let the counsel of the Holy One of Israel draw near and come, that we may know it!
20 Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino ndipo zabwino amaziyesa zoyipa, amene mdima amawuyesa kuwala ndipo kuwala amakuyesa mdima, amene zowawasa amaziyesa zotsekemera ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.
Woe to those who call evil good, and good evil, who put darkness for light, and light for darkness, who put bitter for sweet, and sweet for bitter!
21 Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru ndipo amadziyesa ochenjera.
Woe to those who are wise in their own eyes, and prudent in their own sight!
22 Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,
Woe to those who are mighty to drink wine, and men of strength to mingle strong drink,
23 amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.
who justify the wicked for rewards, and take away the justice of the righteous man from him!
24 Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto, momwemonso mizu yawo idzawola ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi; chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse, ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.
Therefore as the tongue of fire devours the stubble, and as the dry grass sinks down in the flame, so their root shall be as rottenness, and their blossom shall go up as dust, because they have rejected the law of Jehovah of hosts, and despised the word of the Holy One of Israel.
25 Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake; watambasula dzanja lake pa anthuwo ndipo akuwakantha Mapiri akugwedezeka, ndipo mitembo ya anthu yangoti mbwee mʼmisewu ngati zinyalala. Komabe ngakhale watero, mkwiyo wake sunaleke, dzanja lake likanali chitambasulire;
Therefore the anger of Jehovah is kindled against his people, and he has stretched forth his hand against them, and has smitten them. And the mountains tremble, and their dead bodies are as refuse in the midst of the streets. For all this his anger is not turned away, but his hand is stretched out still.
26 Yehova wakweza mbendera kuyitana mtundu wa anthu akutali, akuyitana anthuwo ndi likhweru kuti abwere kuchokera ku mathero a dziko lapansi. Awo akubwera, akubweradi mofulumira kwambiri!
And he will lift up an ensign to the nations from far, and will whistle for them from the end of the earth, and, behold, they shall come with speed swiftly.
27 Palibe ndi mmodzi yemwe amene akutopa kapena kupunthwa, palibe amene akusinza kapena kugona; palibe lamba wa mʼchiwuno amene akumasuka, palibe chingwe cha nsapato chimene chaduka.
None shall be weary nor stumble among them. None shall slumber nor sleep, nor shall the belt of their loins be loosed, nor the latchet of their shoes be broken,
28 Mivi yawo ndi yakuthwa, mauta awo onse ndi okoka, ziboda za akavalo awo nʼzolimba ngati mwala wansagalabwi, magaleta awo ndi aliwiro ngati kamvuluvulu.
whose arrows are sharp, and all their bows bent. Their horses' hoofs shall be accounted as flint, and their wheels as a whirlwind.
29 Kufuwula kwawo kuli ngati kubangula kwa mkango, amabangula ngati misona ya mkango; imadzuma pamene ikugwira nyama ndipo imapita nayo popanda ndi mmodzi yemwe woyipulumutsa.
Their roaring shall be like a lioness. They shall roar like young lions. Yea, they shall roar, and lay hold of the prey, and carry it away safe, and there shall be none to deliver.
30 Tsiku limenelo mitundu ya anthu idzabangula ngati mkokomo wa madzi a mʼnyanja. Ndipo wina akakayangʼana dzikolo adzangoona mdima ndi zovuta; ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.
And they shall roar against them in that day like the roaring of the sea. And if a man looks to the land, behold, darkness and distress, and the light is darkened in the clouds of it.

< Yesaya 5 >