< Yesaya 31 >

1 Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
Woe to those who go down to Egypt for help, and rely on horses, and trust in chariots because they are many, and in horsemen because they are very strong, but they look not to the Holy One of Israel, nor seek Jehovah!
2 Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
Yet he also is wise, and will bring evil, and will not call back his words, but will arise against the house of the evildoers, and against the help of those who work iniquity.
3 Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
Now the Egyptians are men, and not God, and their horses flesh, and not spirit. And when Jehovah shall stretch out his hand, both he who helps shall stumble, and he who is helped shall fall, and they shall all be consumed together.
4 Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
For thus says Jehovah to me, As the lion and the young lion growling over his prey, even if a multitude of shepherds are called forth against him, he will not be dismayed at their voice, nor abase himself for the noise of them, so Jehovah of hosts will come down to fight upon mount Zion, and upon the hill of it.
5 Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
As birds hovering, so Jehovah of hosts will protect Jerusalem. He will protect and deliver. He will pass over and preserve.
6 Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
Turn ye to him from whom ye have deeply revolted, O sons of Israel.
7 Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
For in that day they shall cast away every man his idols of silver, and his idols of gold, which your own hands have made to you for a sin.
8 “Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
And the Assyrian shall fall by the sword, not of man, and the sword, not of men, shall devour him. But he shall flee from the sword, and his young men shall become subject to task work.
9 Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.
And his rock shall pass away because of terror, and his rulers shall be dismayed at the ensign, says Jehovah, whose fire is in Zion, and his furnace in Jerusalem.

< Yesaya 31 >