< Hoseya 6 >

1 “Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova. Iye watikhadzula, koma adzatichiritsa. Iye wativulaza, koma adzamanga mabala athu.
Come, and let us return to Jehovah, for he has torn, and he will heal us. He has smitten, and he will bind us up.
2 Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa; pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.
After two days he will revive us. On the third day he will raise us up, and we shall live before him.
3 Tiyeni timudziwe Yehova, tiyeni tilimbike kumudziwa Iye. Adzabwera kwa ife mosakayikira konse ngati kutuluka kwa dzuwa; adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe, ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”
And let us know, let us follow on to know Jehovah. His going forth is sure as the morning, and he will come to us as the rain, as the latter rain that waters the earth.
4 Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani? Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda? Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa, ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.
O Ephraim, what shall I do to thee? O Judah, what shall I do to thee? For your goodness is as a morning cloud, and as the dew that goes away early.
5 Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga, ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga; chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.
Therefore I have hewed them by the prophets. I have slain them by the words of my mouth. And thy judgments are as the light that goes forth.
6 Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe, ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.
For I desire mercy, and not sacrifice, and the knowledge of God more than burnt offerings.
7 Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa, iwo sanakhulupirike kwa Ine.
But like Adam they have transgressed the covenant. There they have dealt treacherously against me.
8 Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa, okhala ndi zizindikiro za kuphana.
Gilead is a city of those who work iniquity; it is stained with blood.
9 Monga momwe mbala zimadikirira anthu, magulu a ansembe amachitanso motero; iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu, kupalamula milandu yochititsa manyazi.
And as troops of robbers wait for a man, so the company of priests murder in the way toward Shechem. Yea, they have committed iniquity.
10 Ndaona chinthu choopsa kwambiri mʼnyumba ya Israeli. Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere, ndipo Israeli wadzidetsa.
I have seen a horrible thing in the house of Israel. Whoredom is there in Ephraim; Israel is defiled.
11 “Kunenanso za iwe Yuda, udzakolola chilango. “Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”
Also, O Judah, there is a harvest appointed for thee when I bring back the captivity of my people.

< Hoseya 6 >