< Hoseya 5 >

1 “Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
Hear this, O ye priests, and hearken, O house of Israel, and give ear, O house of the king, for to you pertains the judgment. For ye have been a snare at Mizpah, and a net spread upon Tabor.
2 Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
And the revolters have gone deep in making slaughter, but I am a rebuker of them all.
3 Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
I know Ephraim, and Israel is not hid from me. For now, O Ephraim, thou have played the harlot; Israel is defiled.
4 “Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
Their doings will not allow them to turn to their God, for the spirit of whoredom is within them, and they do not know Jehovah.
5 Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
And the pride of Israel testifies to his face. Therefore Israel and Ephraim shall stumble in their iniquity. Judah also shall stumble with them.
6 Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
They shall go with their flocks and with their herds to seek Jehovah, but they shall not find him. He has withdrawn himself from them.
7 Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
They have dealt treacherously against Jehovah, for they have borne strange sons. Now the new moon shall devour them with their fields.
8 “Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
Blow ye the cornet in Gibeah, and the trumpet in Ramah. Sound an alarm at Beth-aven, behind thee, O Benjamin.
9 Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
Ephraim shall become a desolation in the day of rebuke. I have made known that which shall surely be among the tribes of Israel.
10 Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
The rulers of Judah are like those who remove the landmark. I will pour out my wrath upon them like water.
11 Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
Ephraim is oppressed. He is crushed in judgment, because he was content to walk after man's command.
12 Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
Therefore I am to Ephraim as a moth, and to the house of Judah as rottenness.
13 “Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
When Ephraim saw his sickness, and Judah saw his wound, then Ephraim went to Assyria, and sent to king Jareb. But he is not able to heal you, nor will he cure you of your wound.
14 Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
For I will be to Ephraim as a lion, and as a young lion to the house of Judah. I, even I, will tear and go away, I will carry off, and there shall be none to deliver.
15 Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”
I will go and return to my place, till they acknowledge their offense, and seek my face. In their affliction they will seek me earnestly.

< Hoseya 5 >