< Genesis 32 >

1 Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
And Jacob went on his way, and the agents of God met him.
2 Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
And Jacob said when he saw them, This is God's camp. And he called the name of that place Mahanaim.
3 Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
And Jacob sent messengers before him to Esau his brother to the land of Seir, the field of Edom.
4 Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
And he commanded them, saying, Thus shall ye say to my lord Esau, Thus says thy servant Jacob, I have sojourned with Laban, and stayed until now.
5 Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
And I have oxen, and donkeys, flocks, and men-servants, and maid-servants. And I have sent to tell my lord, that I may find favor in thy sight.
6 Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
And the messengers returned to Jacob, saying, We came to thy brother Esau, and moreover he comes to meet thee, and four hundred men with him.
7 Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
Then Jacob was greatly afraid and was distressed. And he divided the people that were with him, and the flocks, and the herds, and the camels, into two companies.
8 Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
And he said, If Esau comes to the one company, and smites it, then the company which is left shall escape.
9 Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
And Jacob said, O God of my father Abraham, and God of my father Isaac, O Jehovah, who said to me, Return to thy country, and to thy kindred, and I will do thee good,
10 Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
I am not worthy of the least of all the loving kindnesses, and of all the truth, which thou have shown to thy servant, for with my staff I passed over this Jordan, and now I have become two companies.
11 Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
Deliver me, I pray thee, from the hand of my brother, from the hand of Esau. For I fear him, lest he comes and smites me, the mother with the sons.
12 Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
And thou said, I will surely do thee good, and make thy seed as the sand of the sea, which cannot be numbered for multitude.
13 Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
And he lodged there that night, and took of that which he had with him a present for Esau his brother:
14 Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
two hundred she-goats and twenty he-goats, two hundred ewes and twenty rams,
15 ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
thirty milk camels and their colts, forty cows and ten bulls, twenty she-donkeys and ten foals.
16 Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
And he delivered them into the hand of his servants, every herd by itself, and said to his servants, Pass over before me, and put a space between herd and herd.
17 Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
And he commanded the foremost, saying, When Esau my brother meets thee, and asks thee, saying, Whose are thou? And where do thou go? And whose are these before thee?
18 Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
Then thou shall say, Thy servant Jacob's. It is a present sent to my lord Esau. And, behold, he also is behind us.
19 Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
And he commanded also the second, and the third, and all who followed the herds, saying, On this manner shall ye speak to Esau when ye find him,
20 Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
and ye shall say, Moreover, behold, thy servant Jacob is behind us. For he said, I will appease him with the present that goes before me, and afterward I will see his face. Perhaps he will accept me.
21 Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
So the present passed over before him, and he himself lodged that night in the company.
22 Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
And he rose up that night, and took his two wives, and his two handmaids, and his eleven sons, and passed over the ford of the Jabbok.
23 Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
And he took them, and sent them over the stream, and sent over that which he had.
24 Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
And Jacob was left alone, and a man wrestled with him until the breaking of the day.
25 Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
And when he saw that he did not prevail against him, he touched the hollow of his thigh, and the hollow of Jacob's thigh was strained as he wrestled with him.
26 Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
And he said, Let me go, for the day breaks. And he said, I will not let thee go unless thou bless me.
27 Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
And he said to him, What is thy name? And he said, Jacob.
28 Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
And he said, Thy name shall no more be called Jacob, but Israel, for thou have striven with God and with men, and have prevailed.
29 Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
And Jacob asked him, and said, Tell me, I pray thee, thy name. And he said, Why is it that thou ask for my name? And he blessed him there.
30 Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
And Jacob called the name of the place Peniel, for, I have seen God face to face, and my life is preserved.
31 Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
And the sun rose upon him as he passed over Penuel, and he limped upon his thigh.
32 Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.
Therefore the sons of Israel do not eat the sinew of the hip which is upon the hollow of the thigh, to this day, because he touched the hollow of Jacob's thigh in the sinew of the hip.

< Genesis 32 >