< Genesis 31 >

1 Yakobo anamva zimene ana aamuna a Labani ankanena kuti, “Yakobo watenga chilichonse cha abambo athu ndipo wapeza chuma chonsechi pogwiritsa ntchito chuma cha abambo athu.”
And he heard the words of Laban's sons, saying, Jacob has taken away all that was our father's, and he has gotten all this glory of that which was our father's.
2 Choncho Yakobo anaona kuti Labani sankamuonetsanso nkhope yabwino monga kale.
And Jacob beheld the countenance of Laban, and, behold, it was not toward him as beforetime.
3 Pamenepo Yehova anati kwa Yakobo, “Bwerera ku dziko la makolo ako ndi kwa abale ako, ndipo Ine ndidzakhala nawe.”
And Jehovah said to Jacob, Return to the land of thy fathers, and to thy kindred, and I will be with thee.
4 Choncho Yakobo anatumiza mawu kukayitana Rakele ndi Leya kuti abwere ku busa kumene ankaweta ziweto zake.
And Jacob sent and called Rachel and Leah to the field to his flock,
5 Iye anawawuza kuti, “Abambo anu sakundionetsanso nkhope yabwino monga kale, koma Mulungu wa makolo anga wakhala ali nane.
and said to them, I see your father's countenance, that it is not toward me as beforetime, but the God of my father has been with me.
6 Inu mukudziwa kuti ndagwirira ntchito abambo anu ndi mphamvu zanga zonse,
And ye know that with all my power I have served your father.
7 chonsecho abambo anu akhala akundinyenga posintha malipiro anga kakhumi konse. Komabe Mulungu sanalole kuti andichitire choyipa
And your father has deceived me, and changed my wages ten times, but God did not allow him to hurt me.
8 Pamene abambo anu anati, ‘Zamawangamawanga zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana amawangamawanga; ndipo pamene anati, ‘Zamichocholozi zidzakhala malipiro ako,’ ziweto zonse zinaswa ana a michocholozi.
If he said thus, The speckled shall be thy wages, then all the flock bore speckled, and if he said thus, The ringstreaked shall be thy wages, then all the flock bore ringstreaked.
9 Motero Mulungu walanda abambo anu ziweto zawo ndi kundipatsa.
Thus God has taken away the cattle of your father, and given them to me.
10 “Pa nthawi imene ziweto zimatenga mawere ndinalota maloto, ndipo ndinaona kuti atonde onse amene ankakwerawo anali amichocholozi, amawangamawanga kapena amathothomathotho
And it came to pass at the time that the flock conceive, that I lifted up my eyes, and saw in a dream, and, behold, the he-goats which leaped upon the flock were ringstreaked, speckled, and grizzled.
11 Kutulo komweko, mngelo wa Mulungu anati, ‘Yakobo.’ Ine ndinayankha, ‘Ee, Ambuye.’
And the agent of God said to me in the dream, Jacob. And I said, Here I am.
12 Ndipo iye anati, ‘Tayangʼana ndipo taona kuti atonde onse okwerana ndi ziweto ali amichocholozi, amawangamawanga kapena a mathothomathotho, popeza ndaona zonse zimene Labani wakhala akukuchitira.
And he said, Lift up now thine eyes, and see, all the he-goats which leap upon the flock are ringstreaked, speckled, and grizzled, for I have seen all that Laban does to thee.
13 Ine ndine Mulungu amene ndinadza kwa iwe pa Beteli paja. Beteli ndi kumalo kuja kumene unayimika mwala ndi kuwudzoza mafuta, komanso kulumbira kwa Ine. Tsopano choka mʼdziko lino msanga ndi kubwerera ku dziko la kwanu.’”
I am the God of Bethel, where thou anointed a pillar, where thou vowed a vow to me. Now arise, get thee out from this land, and return to the land of thy nativity.
14 Pamenepo Rakele ndi Leya anayankha, “Kodi ngati ife tilinso ndi gawo ngati cholowa pa chuma cha abambo athu?
And Rachel and Leah answered and said to him, Is there yet any portion or inheritance for us in our father's house?
15 Kodi abambo athu samationa ife ngati alendo? Iwo anatigulitsa ndi kuwononga ndalama zonse anazipeza pa ifezo.
Are we not accounted by him as foreigners? For he has sold us, and has also quite devoured our money.
16 Chuma chonse chimene Mulungu walanda abambo athu, ndi chathu ndi ana athu. Tsono inu chitani zimene Mulungu wakuwuzani.”
For all the riches which God has taken away from our father, that is ours and our children's. Now then, whatever God has said to thee, do.
17 Pamenepo Yakobo anakonzeka nakweza ana ake ndi akazi ake pa ngamira,
Then Jacob rose up, and set his sons and his wives upon the camels.
18 anakusa ziweto zake zonse patsogolo natenga katundu wake yense amene anamupeza ku Padanaramu, ndipo ananyamuka kupita ku Kanaani, ku dziko la abambo ake, Isake.
And he carried away all his cattle, and all his substance which he had gathered, the cattle of his getting, which he had gathered in Paddan-aram, to go to Isaac his father to the land of Canaan.
19 Labani atachoka pa khomo kupita kukameta nkhosa, mʼmbuyomu Rakele anaba timafano ta milungu ta abambo ake.
Now Laban was gone to shear his sheep, and Rachel stole the teraphim that were her father's.
20 Komanso nthawi iyi nʼkuti Yakobo atamunamiza Labani Mwaramu posamuwuza zoona kuti afuna kuthawa.
And Jacob slipped away unawares to Laban the Syrian, in that he did not tell him that he fled.
21 Choncho anathawa ndi zonse anali nazo. Ananyamuka nawoloka mtsinje wa Yufurate kupita cha ku Giliyadi, dziko la mapiri.
So he fled with all that he had. And he rose up, and passed over the River, and set his face toward the mountain of Gilead.
22 Patapita masiku atatu, Labani anawuzidwa kuti Yakobo wathawa.
And it was told Laban on the third day that Jacob had fled.
23 Pomwepo anatengana ndi abale ake namulondola Yakobo kwa masiku asanu ndi awiri ndipo anakamupezera ku Giliyadi, dziko la mapiri.
And he took his brothers with him, and pursued after him seven days' journey, and he overtook him in the mountain of Gilead.
24 Koma Mulungu anabwera kwa Labani, Mwaramu kutulo usiku nati kwa iye, “Samala kuti usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.”
And God came to Laban the Syrian in a dream of the night, and said to him, Take heed to thyself that thou not speak to Jacob either good or bad.
25 Pamene Labani amamupeza Yakobo, nʼkuti Yakobo atamanga matenti ake ku mapiri a dziko la Giliyadi. Nayenso Labani ndi abale ake anamanga matenti awo komweko.
And Laban came up with Jacob. Now Jacob had pitched his tent in the mountain. And Laban encamped with his brothers in the mountain of Gilead.
26 Tsono Labani anati kwa Yakobo, “Kodi ndakuchita chiyani kuti iwe undinamize ndi kutenga ana anga ngati anthu ogwidwa ku nkhondo?
And Laban said to Jacob, What have thou done, that thou have slipped away unawares to me, and carried away my daughters as captives of the sword?
27 Chifukwa chiyani unandinamiza ndi kuthawa mozemba wosandiwuza? Ukanandiwuza, bwezi titatsanzikana mwa chisangalalo ndi kuyimba nyimbo ndi zisekese ndi azeze.
Why did thou flee secretly, and creep away from me, and did not tell me, that I might have sent thee away with mirth and with songs, with tambourine and with harp,
28 Sunandilole kuti ndingopsompsona adzukulu anga ndi ana anga aakazi motsanzikana nawo. Unachita zopusa.
and did not allow me to kiss my sons and my daughters? Now thou have done foolishly.
29 Ndili nayo mphamvu yakukuchita choyipa; koma usiku wapitawu, Mulungu wa abambo ako wandiwuza ine kuti, ‘Usamuopseze Yakobo mwa njira iliyonse.’
It is in the power of my hand to do you harm, but the God of your father spoke to me last night, saying, Take heed to thyself that thou not speak to Jacob either good or bad.
30 Ndikudziwa kuti unachoka chifukwa unapukwa kufuna kubwerera kwanu kwa abambo ako. Koma nʼchifukwa chiyani unaba milungu yanga?”
And now, though thou have certainly gone, because thou have been very desirous for thy father's house, yet why have thou stolen my gods?
31 Yakobo anayankha Labani kuti, “Ine ndinkaopa chifukwa ndinkaganiza kuti mukhoza kundilanda anawa.
And Jacob answered and said to Laban, Because I was afraid, for I said, Lest thou should take thy daughters from me by force.
32 Koma mukapeza wina aliyense ndi milungu yanu, ameneyo sakhala ndi moyo. Anthu onse akupenya, lozani chilichonse chanu chimene chili ndi ine, ndipo ngati muchipeze tengani. Koma Yakobo sankadziwa kuti Rakele anabadi milunguyo.”
With whomever thou find thy gods, he shall not live. Before our brothers discern thou what is thine with me, and take it to thee. For Jacob did not know that Rachel had stolen them.
33 Choncho Labani analowadi mu tenti ya Yakobo, ya Leya ndi mʼmatenti a adzakazi awiri aja, koma sanapeze kalikonse. Atatuluka mu tenti ya Leya, analowa ya Rakele.
And Laban went into Jacob's tent, and into Leah's tent, and into the tent of the two maid-servants, but he did not find them. And he went out of Leah's tent, and entered into Rachel's tent.
34 Koma Rakele anatengadi milungu ija ndi kuyiika mʼkati mwa chokhalira cha pa ngamira, iye nʼkukhalapo. Choncho Labani anafunafuna mu tenti monse koma wosapeza kanthu.
Now Rachel had taken the teraphim, and put them in the camel's saddle, and sat upon them. And Laban felt around all the tent, but did not find them.
35 Rakele anati kwa abambo ake, “Pepanitu musandikwiyire mbuye wanga chifukwa choti sinditha kuyimirira pamaso panu chifukwa ndili kumwezi.” Choncho Labani anafunafuna koma sanayipeze milungu ija.
And she said to her father, Let not my lord be angry that I cannot rise up before thee, for the manner of women is upon me. And he searched, but did not find the teraphim.
36 Yakobo anapsa mtima nafunsa Labani mwaukali kuti, “Kodi ndalakwa chiyani? Ndi tchimo lanji limene ndachita kuti muchite kundisaka chonchi?
And Jacob was angry, and chided with Laban. And Jacob answered and said to Laban, What is my trespass? What is my sin that thou have hotly pursued after me?
37 Chifukwa chiyani mwafunyulula katundu wanga? Ndipo mwapeza chiyani cha inu pamenepa? Chimene mwapezapo chiyikeni poyera pamaso pa abale anu ndi anga kuti atiweruze.
Whereas thou have felt around all my stuff, what have thou found of all thy household stuff? Set it here before my brothers and thy brothers, that they may judge between us two.
38 “Ndakhala nanu kwa zaka makumi awiri tsopano ndipo nkhosa ndi mbuzi zanu sizinapoloze, kapena ine kudyapo nkhosa za mʼkhola mwanu.
These twenty years I have been with thee, thy ewes and thy she-goats have not cast their young, and I have not eaten the rams of thy flocks.
39 Chiweto chikakhadzulidwa ndi chirombo, sindinkabwera nacho kwa inu. Ineyo ndinkalipira. Inuyo munkandilipiritsa kalikonse kobedwa masana kapena usiku.
I did not bring to thee that which was torn by beasts; I bore the loss of it, of my hand thou required it, whether stolen by day or stolen by night.
40 Moyo wanga unali wotere: Dzuwa limanditentha masana ndipo usiku ndimazunzika ndi kuzizira. Tulo sindimalipeza konse.
Thus I was; in the day the drought consumed me, and the frost by night, and my sleep fled from my eyes.
41 Zinthu zinali chonchi kwa zaka makumi awiri zimene ndinali mʼnyumba mwanu. Ndinakugwirirani ntchito kwa zaka khumi ndi zinayi chifukwa cha ana anu aakazi awiri ndipo zaka zina zisanu ndi chimodzi chifukwa cha ziweto zanu, ndipo munandisinthira malipiro kakhumi konse.
These twenty years I have been in thy house. I served thee fourteen years for thy two daughters, and six years for thy flock. And thou have changed my wages ten times.
42 Akanapanda kukhala nane Mulungu wa abambo anga, Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu amene Isake ankamuopa, mosakayika inu mukanandichotsa chimanjamanja. Koma Mulungu waona zovuta zanga ndi kulimbikira ntchito kwanga, ndipo usiku wapitawu anakudzudzulani.”
Unless the God of my father, the God of Abraham, and the fear of Isaac, had been with me, surely now thou would have sent me away empty. God has seen my affliction and the labor of my hands, and rebuked thee last night.
43 Labani anayankha Yakobo nati, “Ana aakaziwa ndi anga, ana awo ndi anganso. Ziwetozi ndi zanga. Chilichonse ukuona apa ndi changa. Koma tsopano ndingachite chiyani ndi ana anga aakaziwa kapena ndi ana awo?
And Laban answered and said to Jacob, The daughters are my daughters, and the sons are my sons, and the flocks are my flocks, and all that thou see is mine. And what can I do this day to these my daughters, or to their sons whom they have borne?
44 Tsono, tiye tichite pangano pakati pa iwe ndi ine, ndipo likhale mboni pakati pathu.”
And now come, let us make a covenant, I and thou, and let it be for a witness between me and thee.
45 Choncho Yakobo anayimiritsa mwala ngati chipilala.
And Jacob took a stone, and set it up for a pillar.
46 Nati kwa abale ake, “Tutani miyala ina.” Choncho anawunjika miyalayo, ndipo anadya chakudya atakhala pa mbali pa muluwo.
And Jacob said to his brothers, Gather stones, and they took stones, and made a heap. And they ate there by the heap.
47 Labani anawutcha muluwo Yegara-sahaduta, ndipo Yakobo anawutcha Galeeda.
And Laban called it Jegar-saha-dutha, but Jacob called it Galeed.
48 Labani anati, “Mulu uwu ndi mboni pakati pa inu ndi ine lero.” Ndi chifukwa chake unatchedwa Galeeda.
And Laban said, This heap is witness between me and thee this day. Therefore the name of it was called Galeed,
49 Unatchedwanso Mizipa, chifukwa iye anati, “Yehova aonetsetsa kuti palibe mmodzi mwa ife adzaswe panganoli ngakhale titatalikirana.
and Mizpah. For he said, May Jehovah watch between me and thee, when we are absent one from another,
50 Ngati ukazunza ana anga kapena kukwatira akazi enanso, ngakhale kuti palibe wina amene ali nafe pano, koma kumbukira kuti Mulungu ndiye mboni pakati pathu.”
if thou will afflict my daughters, and if thou will take wives besides my daughters, no man is with us, see, God is witness between me and thee.
51 Labani anatinso kwa Yakobo, “Taona pano pali miyala ndi chipilala chimene ndayimika pakati pa iwe ndi ine.
And Laban said to Jacob, Behold this heap, and behold the pillar, which I have set between me and thee.
52 Mulu wa miyala uwu ndi chipilalachi ndi mboni. Ine sindidzadutsa mulu wa miyalawu kudzalimbana ndi iwe. Iwenso usadzadutse mulu wa miyalawu kudzalimbana nane.
This heap is witness, and the pillar is witness, that I will not pass over this heap to thee, and that thou shall not pass over this heap and this pillar to me, for harm.
53 Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu wa Nahori ndiye adzatiweruze.” Choncho Yakobo analumbira mʼdzina la Mulungu amene Isake, abambo ake ankamuopa.
The God of Abraham, and the God of Nahor, the God of their father, judge between us. And Jacob swore by the fear of his father Isaac.
54 Yakobo anapereka nsembe pa phiri paja, ndipo anayitana abale ake kuti adzadye chakudya. Atadya chakudya anagona pa phiri pomwepo.
And Jacob offered a sacrifice on the mountain, and called his brothers to eat bread. And they ate bread, and tarried all night on the mountain.
55 Mmamawa wake, Labani anapsompsona zidzukulu zake ndi ana ake nawadalitsa. Kenaka ananyamuka kubwerera ku mudzi.
And early in the morning Laban rose up, and kissed his sons and his daughters, and blessed them. And Laban departed and returned to his place.

< Genesis 31 >