< Genesis 29 >

1 Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
Then Jacob went on his journey, and came to the land of the sons of the east.
2 Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
And he looked, and, behold, a well in the field. And, lo, three flocks of sheep were lying there by it, for they watered the flocks out of that well. And the stone upon the well's mouth was great.
3 Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
And all the flocks were gathered there. And they rolled the stone from the well's mouth, and watered the sheep, and put the stone again upon the well's mouth in its place.
4 Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
And Jacob said to them, My brothers, where are ye from? And they said, We are of Haran.
5 Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
And he said to them, Do ye know Laban the son of Nahor? And they said, We know him.
6 Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
And he said to them, Is it well with him? And they said, It is well. And, behold, Rachel his daughter comes with the sheep.
7 Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
And he said, Lo, it is yet high day, neither is it time that the cattle should be gathered together. Water ye the sheep, and go and feed them.
8 Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
And they said, We cannot until all the flocks be gathered together, and they roll the stone from the well's mouth. Then we water the sheep.
9 Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
While he was yet speaking with them, Rachel came with her father's sheep, for she kept them.
10 Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
And it came to pass, when Jacob saw Rachel the daughter of Laban his mother's brother, and the sheep of Laban his mother's brother, that Jacob went near, and rolled the stone from the well's mouth, and watered the flock of Laban his mother's brother.
11 Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
And Jacob kissed Rachel, and lifted up his voice, and wept.
12 Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
And Jacob told Rachel that he was her father's brother, and that he was Rebekah's son. And she ran and told her father.
13 Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
And it came to pass, when Laban heard the news of Jacob his sister's son, that he ran to meet him, and embraced him, and kissed him, and brought him to his house. And he told Laban all these things.
14 Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
And Laban said to him, Surely thou are my bone and my flesh. And he abode with him the space of a month.
15 Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
And Laban said to Jacob, Because thou are my brother, should thou therefore serve me for nothing? Tell me, what shall thy wages be?
16 Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
And Laban had two daughters. The name of the elder was Leah, and the name of the younger was Rachel.
17 Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
And Leah's eyes were weak, but Rachel was beautiful and well favored.
18 Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
And Jacob loved Rachel, and he said, I will serve thee seven years for Rachel thy younger daughter.
19 Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
And Laban said, It is better that I give her to thee, than that I should give her to another man. Abide with me.
20 Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
And Jacob served seven years for Rachel. And they seemed to him but a few days, for the love he had for her.
21 Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
And Jacob said to Laban, Give me my wife, for my days are fulfilled, that I may go in to her.
22 Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
And Laban gathered together all the men of the place, and made a feast.
23 Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
And it came to pass in the evening, that he took Leah his daughter, and brought her to him. And he went in to her.
24 Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
And Laban gave Zilpah his handmaid to his daughter Leah for a handmaid.
25 Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
And it came to pass in the morning that, behold, it was Leah. And he said to Laban, What is this thou have done to me? Did I not serve with thee for Rachel? Why then have thou beguiled me?
26 Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
And Laban said, It is not so done in our place, to give the younger before the firstborn.
27 Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
Fulfill the week of this one, and we will give thee the other also for the service which thou shall serve with me yet seven other years.
28 Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
And Jacob did so, and fulfilled her week. And he gave him Rachel his daughter to wife.
29 Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
And Laban gave to Rachel, his daughter, Bilhah his handmaid to be her handmaid.
30 Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
And he also went in to Rachel, and also he loved Rachel more than Leah, and served with him yet seven other years.
31 Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
And Jehovah saw that Leah was regarded inferior, and he opened her womb, but Rachel was barren.
32 Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
And Leah conceived, and bore a son, and she called his name Reuben. For she said, Because Jehovah has looked upon my affliction, for now my husband will love me.
33 Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
And she conceived again, and bore a son, and said, Because Jehovah has heard that I am regarded inferior, he has therefore given me this son also. And she called his name Simeon.
34 Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
And she conceived again, and bore a son, and said, Now this time my husband will be joined to me, because I have borne him three sons. Therefore his name was called Levi.
35 Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.
And she conceived again, and bore a son. And she said, This time I will praise Jehovah. Therefore she called his name Judah. And she left off bearing.

< Genesis 29 >