< Genesis 28 >

1 Choncho Isake anayitanitsa Yakobo namudalitsa nʼkumuwuzitsa kuti, “Usakwatire mkazi wa kuno ku Kanaani.
And Isaac called Jacob, and blessed him, and ordered him, and said to him, Thou shall not take a wife of the daughters of Canaan.
2 Panopo upite ku Padanaramu, ku nyumba kwa Betueli abambo a amayi akowa, kumeneko ukakwatire mmodzi mwa ana aakazi a Labani, mlongo wa amayi akowa.
Arise, go to Paddan-aram, to the house of Bethuel thy mother's father, and take thee a wife from there of the daughters of Laban thy mother's brother.
3 Mulungu Wamphamvuzonse akudalitse iwe nakupatse ana ambiri mpaka udzasanduke gulu lalikulu la mitundu ya anthu.
And God Almighty bless thee, and make thee fruitful, and multiply thee, that thou may be a company of peoples,
4 Mulunguyo akudalitse iwe monga mmene anamudalitsira Abrahamu kuti zidzukulu zako zidzalandira dziko limene ukukhalamo ngati mlendo kuti lidzakhale lawo. Ili ndi dziko limene Mulungu anapereka kwa Abrahamu.”
and give thee the blessing of Abraham, to thee, and to thy seed with thee, that thou may inherit the land of thy sojourning, which God gave to Abraham.
5 Ndipo Isake anamulola Yakobo kuti anyamuke kupita ku Padanaramu kwa Labani mwana wa Betueli Mwaramu. Labani anali mlongo wa Rebeka, mayi wa Yakobo ndi Esau.
And Isaac sent Jacob away. And he went to Paddan-aram to Laban, son of Bethuel the Syrian, the brother of Rebekah, Jacob's and Esau's mother.
6 Tsopano Esau anadziwa kuti Isake anadalitsa Yakobo ndi kumutumiza ku Padanaramu kuti akakwatire kumeneko. Anawuzidwanso kuti, “Usakwatire mkazi wa ku Kanaani.”
Now Esau saw that Isaac had blessed Jacob and sent him away to Paddan-aram, to take for him a wife from there, and that as he blessed him he gave him an order, saying, Thou shall not take a wife of the daughters of Canaan,
7 Yakobo anamvera abambo ake ndi amayi ake ndi kupita ku Padanaramu.
and that Jacob obeyed his father and his mother, and was gone to Paddan-aram.
8 Ndiye pamenepo Esau anazindikira kuti abambo ake Isake sankakondwera ndi akazi a ku Kanaani;
And Esau saw that the daughters of Canaan did not please Isaac his father.
9 anapita kwa Ismaeli mwana wa Abrahamu nakwatira Mahalati mwana wa Ismaeli, mlongo wake wa Nebayoti. Anatero kuwonjezera akazi amene anali nawo kale.
And Esau went to Ishmael, and took, besides the wives that he had, Mahalath the daughter of Ishmael Abraham's son, the sister of Nebaioth, to be his wife.
10 Yakobo ananyamuka pa ulendo kuchoka ku Beeriseba kupita ku Harani.
And Jacob went out from Beersheba, and went toward Haran.
11 Atafika pa malo pena, anayima kuti agonepo chifukwa dzuwa linali litalowa. Anatenga mwala wina pomwepo natsamiritsapo mutu wake, ndipo anagona.
And he touched upon a certain place, and tarried there all night, because the sun was set. And he took one of the stones of the place, and put it under his head, and lay down in that place to sleep.
12 Mʼmaloto, anaona makwerero oyimikidwa pansi ndipo anakafika kumwamba. Angelo a Mulungu amakwera ndi kutsika pa makwereropo.
And he dreamed, and, behold, a ladder set up on the earth, and the top of it reached to heaven. And, behold, the agents of God ascending and descending on it.
13 Tsono Yehova anayimirira pambali pake, nati, “Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu kholo lake la Isake abambo ako. Ndidzakupatsa iwe ndi zidzukulu zako dziko limene ukugonamolo.
And, behold, Jehovah stood above it, and said, I am Jehovah, the God of Abraham thy father, and the God of Isaac. The land on which thou lie, to thee I will give it, and to thy seed.
14 Zidzukulu zako zidzachuluka ngati fumbi la pa dziko lapansi ndipo zidzabalalikira kumadzulo ndi kummawa, kumpoto ndi kummwera. Anthu onse adzalandira madalitso kudzera mwa iwe ndi zidzukulu zako.
And thy seed shall be as the dust of the earth, and thou shall spread abroad to the west, and to the east, and to the north, and to the south. And in thee and in thy seed shall all the families of the earth be blessed.
15 Ine ndili nawe pamodzi ndipo ndidzakuyangʼanira kulikonse upiteko, ndipo ndidzakubwezera ku dziko lino. Sindidzakusiya mpaka nditachita zimene ndakulonjezazi.”
And, behold, I am with thee, and will keep thee wherever thou go, and will bring thee again into this land. For I will not leave thee, until I have done that which I have spoken to thee of.
16 Yakobo atadzidzimuka, anati, “Zoonadi Yehova ali pa malo ano, ndipo ine sindinadziwe.”
And Jacob awoke out of his sleep, and he said, Surely Jehovah is in this place, and I did not know it.
17 Tsono anachita mantha ndipo anati, “Malo ano ndi woopsa ndithu. Zoonadi pano ndi pa nyumba ya Mulungu ndi khomo la kumwamba.”
And he was afraid, and said, How awesome is this place! This is none other than the house of God, and this is the gate of heaven.
18 Mmamawa mwake Yakobo anatenga mwala umene anatsamira mutu wake uja nawuyimika ngati chipilala ndi kuthira mafuta pamwamba pake
And Jacob rose up early in the morning, and took the stone that he had put under his head, and set it up for a pillar, and poured oil upon the top of it.
19 Iye anawatcha malowo Beteli, ngakhale kuti poyamba mzindawo ankawutcha Luzi.
And he called the name of that place Bethel, but the name of the city was Luz at first.
20 Pamenepo Yakobo analumbira kwa Yehova nati, “Ngati inu Mulungu mukhala ndi ine, kundiyangʼanira pa ulendo wangawu ndi kundipatsa chakudya ndi chovala;
And Jacob vowed a vow, saying, If God will be with me, and will keep me in this way that I go, and will give me bread to eat, and raiment to put on,
21 ngati inu mudzandibweretsa kwathu mu mtendere, ndiye kuti mudzakhala Mulungu wanga,
so that I come again to my father's house in peace, and Jehovah will be my God,
22 ndipo mwala uwu ndawuyimikawu udzakhala Nyumba ya Mulungu. Ine ndidzakupatsani chakhumi cha zinthu zonse zimene mudzandipatse.”
then this stone, which I have set up for a pillar, shall be God's house. And of all that thou shall give me I will surely give the tenth to thee.

< Genesis 28 >