< Genesis 16 >

1 Tsono Sarai, mkazi wa Abramu anali asanamuberekere ana Abramuyo. Koma anali ndi wantchito wamkazi wa ku Igupto dzina lake Hagara;
Now Sarai, Abram's wife, bore him no sons. And she had a handmaid, an Egyptian, whose name was Hagar.
2 ndipo Sarai anati kwa Abramu, “Yehova sanalole kuti ine ndikhale ndi ana. Bwanji mulowe mwa wantchito wanga wamkaziyu kuti mwina ndingaone ana kudzera mwa iyeyu.” Abramu anamvera Sarai.
And Sarai said to Abram, Behold now, Jehovah has restrained me from bearing. Go in, I pray thee, to my handmaid. It may be that I will obtain sons by her. And Abram hearkened to the voice of Sarai.
3 Tsono Sarai anatenga Hagara wantchito wake wamkazi wa ku Igupto uja namupereka kwa Abramu mwamuna wake kuti akhale mkazi wake. Izi zinachitika Abramu atakhala ku Kanaani zaka khumi.
And Sarai, Abram's wife, took Hagar the Egyptian, her handmaid, after Abram had dwelt ten years in the land of Canaan, and gave her to Abram her husband to be his wife.
4 Abramu atalowana ndi Hagara, Hagara uja anatenga mimba. Pamene Hagara anadziwa kuti anali woyembekezera anayamba kunyoza mbuye wake Sarai.
And he went in to Hagar, and she conceived. And when she saw that she had conceived, her mistress was despised in her eyes.
5 Pamenepo Sarai anati kwa Abramu, “Inu ndinu amene mwandiputira nkhanza zikundichitikirazi. Ndinakupatsani wantchito wanga wamkazi kuti akhale mkazi wanu, ndiye tsopano wayamba kundinyoza ine chifukwa wadziwa kuti ndi woyembekezera. Yehova ndiye amene aweruze pakati pa inu ndi ine.”
And Sarai said to Abram, My wrong be upon thee. I gave my handmaid into they bosom, and when she saw that she had conceived, I was despised in her eyes. Jehovah judge between me and thee.
6 Abramu anati, “Wantchito wakoyu ali mʼmanja mwako. Chita naye chilichonse chimene ukuganiza kuti ndi chokukomera.” Tsono Sarai anazunza Hagara mpaka anathawa.
But Abram said to Sarai, Behold, thy maid is in thy hand, do to her that which is good in thine eyes. And Sarai dealt harshly with her, and she fled from her face.
7 Mngelo wa Yehova anamupeza Hagara pafupi ndi chitsime mʼchipululu. Chinali chitsime chimene chili mʼmphepete mwa msewu wopita ku Suri.
And the agent of Jehovah found her by a fountain of water in the wilderness, by the fountain in the way to Shur.
8 Ndipo mngeloyo anati, “Hagara, iwe wantchito wa Sarai, ukuchokera kuti ndipo ukupita kuti?” Iye anayankha, “Ndikuthawa mbuye wanga Sarai.”
And he said, Hagar, Sarai's handmaid, from where have thou come? And where are thou going? And she said, I am fleeing from the face of my mistress Sarai.
9 Mngelo wa Yehova anamuwuza kuti, “Bwerera kwa mbuye wako ndipo ukamugonjere.
And the agent of Jehovah said to her, Return to thy mistress, and submit thyself under her hands.
10 Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri zoti munthu sangaziwerenge.”
And the agent of Jehovah said to her, I will greatly multiply thy seed, that it shall not be numbered for multitude.
11 Mngelo wa Yehova uja anamuwuzanso kuti, “Ndiwe woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna. Udzamutcha dzina lake Ismaeli, pakuti Yehova wamva kulira chifukwa cha kuzunzika kwako.
And the agent of Jehovah said to her, Behold, thou are with child, and shall bear a son, and thou shall call his name Ishmael, because Jehovah has heard thy affliction.
12 Iye adzakhala munthu wa khalidwe ngati mʼmbulu wamisala; adzadana ndi aliyense ndipo anthu onse adzadana naye, adzakhala mwaudani pakati pa abale ake onse.”
And he will be a wild donkey among men, his hand against every man, and every man's hand against him, and he shall dwell in the presence of all his brothers.
13 Hagara anatcha Yehova amene anamuyankhula uja dzina loti: “Ndinu Mulungu amene mumandiona,” popeza anati, “Ndakumana ndi Yehova atatha kundikomera mtima.”
And she called the name of Jehovah who spoke to her, Thou are a God who sees, for she said, Have I even here looked behind him who sees me?
14 Nʼchifukwa chake chitsime chija chimene chili pakati pa Kadesi ndi Beredi chinatchedwa Beeri-lahai-roi.
Therefore the well was called Beer-lahai-roi. Behold, it is between Kadesh and Bered.
15 Tsono Hagara anamuberekera Abramu mwana wamwamuna ndipo Abramu anamutcha mwanayo Ismaeli.
And Hagar bore Abram a son. And Abram called the name of his son, whom Hagar bore, Ishmael.
16 Pamene Hagara anamubalira Ismaeli nʼkuti Abramuyo ali ndi zaka 86.
And Abram was eighty-six years old when Hagar bore Ishmael to Abram.

< Genesis 16 >