< Genesis 18 >

1 Yehova anadza kwa Abrahamu pafupi ndi mitengo ikuluikulu ya thundu ya ku Mamre. Abrahamu nʼkuti atakhala pansi pa khoma la tenti yake masana, dzuwa likutentha.
And Jehovah appeared to him by the oaks of Mamre, as he sat in the tent door in the heat of the day.
2 Tsono Abrahamu atakweza maso ake patali anangoona anthu atatu atayima cha potero. Atawaona, ananyamuka mofulumira kuti awachingamire. Atafika anaweramitsa mutu pansi mwa ulemu nati,
And he lifted up his eyes and looked, and, lo, three men stood by him. And when he saw them, he ran to meet them from the tent door, and bowed himself to the earth,
3 “Ngati mwandikomera mtima, mbuye wanga, musamulambalale mtumiki wanu.
and said, My lord, if now I have found favor in thy sight, pass not away, I pray thee, from thy servant.
4 Ndikupatseniko timadzi pangʼono kuti nonse musambitse mapazi anu ndi kupumula pansi pa mtengo uwu.
Let now a little water be fetched, and wash your feet, and rest yourselves under the tree.
5 Tsono ndikutengereniko kachakudya kuti mudye kuti mwina nʼkupezako mphamvu zopitirizira ulendo wanu. Inu mwafika kumalo kwa mtumiki wanu.” Ndipo iwo anamuyankha nati, “Zikomo kwambiri, chita monga wanenera.”
And I will fetch a morsel of bread, and strengthen ye your heart. After that ye shall pass on, inasmuch as ye came to your servant. And they said, Do so as thou have said.
6 Choncho Abrahamu anafulumira kupita kwa Sara mʼtenti nati, “Tafulumira, tenga mabeseni atatu a ufa wosalala, ukande ndi kupanga buledi.”
And Abraham hastened into the tent to Sarah, and said, Make ready quickly three measures of fine meal, knead it, and make cakes.
7 Kenaka Abrahamu anakatenga mwana wangʼombe wonenepa ndi wofewa bwino ndi kupatsa wantchito wake amene anachita changu kukonza ndiwoyo.
And Abraham ran to the herd, and fetched a calf tender and good, and gave it to the servant. And he hastened to dress it.
8 Tsono Abrahamu anatenga chambiko, mkaka ndi mwana wangʼombe wokonzedwa uja nazipereka kwa anthu aja. Alendowo akudya, Abrahamu ankawayangʼana atayimirira pansi pa mtengo.
And he took butter, and milk, and the calf which he had dressed, and set it before them. And he stood by them under the tree, and they ate.
9 Anthuwo anafunsa Abrahamu kuti, “Mkazi wako Sara ali kuti?” Iye anati, “Ali mu tentimu.”
And they said to him, Where is Sarah thy wife? And he said, Behold, in the tent.
10 Tsono mmodzi mwa iwo anati, “Mosakayikira ndidzabweranso pa nthawi ngati yomwe ino chaka chamawa, ndipo Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna.” Koma Sara amene anali kumbuyo kwa Abrahamu pa khoma la tenti ankamva zonsezi.
And he said, I will certainly return to thee when the season comes round, and, lo, Sarah thy wife shall have a son. And Sarah heard in the tent door, which was behind him.
11 Abrahamu ndi Sara anali okalamba kale ndipo anali ndi zaka zambiri. Sara nʼkuti atapyola kale pa msinkhu oti nʼkubereka.
Now Abraham and Sarah were old, and well stricken in age. It had ceased to be with Sarah after the manner of women.
12 Choncho anangoseka nati mu mtima mwake, “Kodi munthu wothayitha ngati ine ndingasangalalenso kugona pamodzi ndi mbuye wanga? Mwamuna wanga nayenso ndi wokalamba.”
And Sarah laughed within herself, saying, After I have become old shall I have pleasure, my lord also being old?
13 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Nʼchifukwa chiyani Sara anaseka nʼkumati, ‘Moti ine nʼkudzakhaladi ndi mwana mmene ndakalambiramu?’
And Jehovah said to Abraham, Why did Sarah laugh, saying, Shall I who am old certainly bear a child?
14 Kodi pali chimene chikhoza kumukanika Yehova? Pa nthawi yake, ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzabala mwana wamwamuna.”
Is anything too hard for Jehovah? At the set time I will return to thee, when the season comes round, and Sarah shall have a son.
15 Koma Sara ndi mantha ananama nati, “Sindinaseke.” Koma Iye anati, “Inde iwe unaseka.”
Then Sarah denied, saying, I did not laugh, for she was afraid. And he said, No, but thou did laugh.
16 Kenaka anthu aja ananyamuka ndi kumapita, molunjika ku Sodomu. Ndipo Abrahamu anayenda nawo pamodzi kuwaperekeza.
And the men rose up from there, and looked toward Sodom. And Abraham went with them to bring them on the way.
17 Tsono Yehova anati mu mtima mwake, “Kodi ndingamubisire Abrahamu chimene ndikuti ndichite posachedwa?
And Jehovah said, Shall I hide from Abraham that which I do,
18 Abrahamu adzakhaladi mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa iye.
since Abraham shall surely become a great and mighty nation, and all the nations of the earth shall be blessed in him?
19 Pakuti ndasankha iyeyu kuti adzatsogolere ana ake ndi a pa banja lake, kuti asunge mawu a Yehova pochita zoyenera ndi zachilungamo. Choncho Yehova adzachita kwa Abrahamu chimene anamulonjeza iye.”
For I have known him, to the end that he may command his children and his household after him, that they may keep the way of Jehovah, to do righteousness and justice, to the end that Jehovah may bring upon Abraham that which he has spoken of him.
20 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, “Kulirira Gomora kwakula ndipo tchimo lawo lafika poyipa kwambiri
And Jehovah said, Because the cry of Sodom and Gomorrah is great, and because their sin is very grievous,
21 choncho ndikuti ndipiteko ndikaone ngati zimene achita zilidi zoyipa monga mmene madandawulo andipezera Ine. Ngati sizili choncho, ndikadziwa.”
I will go down now, and see whether they have done altogether according to the cry of it, which comes to me. And if not, I will know.
22 Anthu aja anatembenuka nʼkumapita, kulowera ku Sodomu, koma Abrahamu anali chiyimirire pamaso pa Yehova.
And the men turned from there, and went toward Sodom, but Abraham yet stood before Jehovah.
23 Kenaka Abrahamu anasendera kufupi ndi Iye nati, “Kodi mudzawonongera kumodzi wolungama ndi woyipa?
And Abraham drew near, and said, Will thou consume righteous men with wicked men?
24 Nanga bwanji patakhala anthu makumi asanu olungama mu mzindamo? Kodi mudzawonongadi onse osausiyako mzindawo chifukwa cha anthu makumi asanu olungama omwe ali mʼmenemo?
Perhaps there are fifty righteous men within the city. Will thou consume and not spare the place for the fifty righteous men that are in it?
25 Ndithu simungachite zimenezi, kupha anthu olungama pamodzi ndi oyipa. Nʼzosatheka kuti inu nʼkufananitsa olungama ndi oyipa. Kodi woweruza wa dziko lapansi nʼkulephera kuchita chilungamo?”
That be far from thee to do after this manner, to slay a righteous man with a wicked man, that so the righteous man should be as the wicked man. Far be it from thee. Shall not the Judge of all the earth do right?
26 Yehova anati, “Nditapeza anthu makumi asanu olungama mu mzinda wa Sodomu, ndidzasiya malo onsewo osawawononga chifukwa cha iwo.”
And Jehovah said, If I find in Sodom fifty righteous men within the city, then I will spare all the place for their sake.
27 Ndipo Abrahamu anayankhulanso nati, “Tsono poti ndalimba mtima kuyankhula ndi Ambuye, ngakhale kuti ndine fumbi ndi phulusa chabe,
And Abraham answered and said, Behold now, I have taken upon me to speak to the Lord, who am but dust and ashes.
28 bwanji anthu olungama atacheperapo ndi asanu pa anthu makumi asanu? Kodi mudzawononga mzinda wonse chifukwa cha asanuwo?” Iye anati, “Nditapezamo anthu 45, sindidzawuwononga.”
Perhaps there shall lack five of the fifty righteous men. Will thou destroy all the city for lack of five? And he said, I will not destroy it, if I find there forty-five.
29 Kenakanso anayankhula kwa Iye nati, “Bwanji atangopezekamo anthu 40 okha?” Iye anayankha, “Chifukwa cha anthu 40 amenewa, sindidzatero.”
And he spoke to him yet again, and said, Perhaps there shall be forty found there. And he said, I will not do it for the forty's sake.
30 Ndipo Abrahamu anati, “Pepanitu musandipsere mtima Ambuye, koma mundilole kuti ndiyankhule. Nanga mutapezekamo anthu makumi atatu okha?” Iye anayankha, “Sindidzatero ngati atapezekamo anthu makumi atatu.”
And he said, Oh let not the Lord be angry, and I will speak. Perhaps there shall be thirty found there. And he said, I will not do it, if I find thirty there.
31 Abrahamu anati, “Tsono poti ndalimba mtima chonchi kumayankhula ndi Ambuye, bwanji atangopezeka anthu makumi awiri okha?” Iye anati, “Chifukwa cha anthu makumi awiriwo, sindidzawuwononga.”
And he said, Behold now, I have taken upon me to speak to the Lord. Perhaps there shall be twenty found there. And he said, I will not destroy it for the twenty's sake.
32 Kenaka Abrahamu anati, “Pepani Ambuye musandipsere mtima, ndingoyankhula kamodzi kokhaka basi. Bwanji atangopezeka khumi okha mʼmenemo?” Iye anayankha nati, “Chifukwa cha khumiwo, sindidzawuwononga.”
And he said, Oh let not the Lord be angry, and I will speak yet but this once. Perhaps ten shall be found there. And he said, I will not destroy it for the ten's sake.
33 Yehova atatsiriza kuyankhula ndi Abrahamu, anachoka ndipo Abrahamu anabwerera ku nyumba yake.
And Jehovah went his way as soon as he had left off conversing with Abraham, and Abraham returned to his place.

< Genesis 18 >