< Genesis 13 >

1 Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo.
And Abram went up out of Egypt, he, and his wife, and all that he had, and Lot with him, into the South.
2 Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.
And Abram was very rich in cattle, in silver, and in gold.
3 Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba,
And he went on his journeys from the South even to Bethel, to the place where his tent had been at the beginning, between Bethel and Ai,
4 ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.
to the place of the altar, which he had made there at the first. And Abram called on the name of Jehovah there.
5 Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti.
And Lot also, who went with Abram, had flocks, and herds, and tents.
6 Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi.
And the land was not able to bear them, that they might dwell together. For their substance was great, so that they could not dwell together.
7 Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.
And there was a strife between the herdsmen of Abram's cattle and the herdsmen of Lot's cattle. And the Canaanite and the Perizzite then dwelt in the land.
8 Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale.
And Abram said to Lot, Let there be no strife, I pray thee, between me and thee, and between my herdsmen and thy herdsmen, for we are brothers.
9 Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”
Is not the whole land before thee? Separate thyself, I pray thee, from me. If the left hand, then I will go to the right. Or if the right hand, then I will go to the left.
10 Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora).
And Lot lifted up his eyes, and beheld all the Plain of the Jordan, that it was well watered everywhere (before Jehovah destroyed Sodom and Gomorrah) like the garden of Jehovah, like the land of Egypt, as thou go to Zoar.
11 Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana.
So Lot chose for himself all the Plain of the Jordan. And Lot journeyed east, and they separated themselves the one from the other.
12 Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu.
Abram dwelt in the land of Canaan. And Lot dwelt in the cities of the Plain, and moved his tent as far as Sodom.
13 Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.
Now the men of Sodom were exceedingly wicked and sinners against Jehovah.
14 Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo.
And Jehovah said to Abram, after Lot was separated from him, Lift up now thine eyes, and look from the place where thou are, northward and southward and eastward and westward.
15 Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.
For all the land which thou see, to thee I will give it, and to thy seed forever.
16 Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako.
And I will make thy seed as the dust of the earth. So that if a man can number the dust of the earth, then may thy seed also be numbered.
17 Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”
Arise, walk through the land in the length of it and in the breadth of it, for to thee I will give it.
18 Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.
And Abram moved his tent, and came and dwelt by the oaks of Mamre, which are in Hebron, and built an altar there to Jehovah.

< Genesis 13 >