< Ezekieli 27 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
The word of Jehovah came again to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
And thou, son of man, take up a lamentation over Tyre,
3 Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti, “Iwe Turo, umanena kuti, ‘Ndine wokongola kwambiri.’
and say to Tyre, O thou that dwells at the entry of the sea, that is the merchant of the peoples to many isles, thus says the lord Jehovah: Thou, O Tyre, have said, I am perfect in beauty.
4 Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja; amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
Thy borders are in the heart of the seas. Thy builders have perfected thy beauty.
5 Anakupanga ndi matabwa a payini ochokera ku Seniri; anatenga mikungudza ya ku Lebanoni kupangira mlongoti wako.
They have made all thy planks of fir trees from Senir. They have taken a cedar from Lebanon to make a mast for thee.
6 Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani anapanga zopalasira zako; ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu. Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
Of the oaks of Bashan they have made thine oars. They have made thy benches of ivory inlaid in boxwood, from the isles of Kittim.
7 Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako, ndipo inakhala ngati mbendera. Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo zochokera ku zilumba za Elisa.
Of fine linen with broidered work from Egypt was thy sail, that it might be to thee for an ensign. Blue and purple from the isles of Elishah was thine awning.
8 Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako. Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
The inhabitants of Sidon and Arvad were thy rowers. Thy wise men, O Tyre, were in thee; they were thy pilots.
9 Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako, ngati okonza zibowo zako. Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
The old men of Gebal and the wise men thereof were thy caulkers in thee. All the ships of the sea with their mariners were in thee to deal in thy merchandise.
10 “Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo. Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako, kubweretsa kwa iwe ulemerero.
Persia and Lud and Put were in thine army, thy men of war. They hung the shield and helmet in thee. They set forth thy comeliness.
11 Anthu a ku Arivadi ndi Heleki ankalondera mbali zonse za mpanda wako; anthu a ku Gamadi anali mu nsanja zako, Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse. Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
The men of Arvad with thine army were upon thy walls round about, and valorous men were in thy towers. They hung their shields upon thy walls round about. They have perfected thy beauty.
12 “Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Tarshish was thy merchant because of the multitude of all kinds of riches, with silver, iron, tin, and lead. They traded for thy wares.
13 “Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Javan, Tubal, and Meshech, they were thy merchants. They traded the persons of men, and vessels of brass for thy merchandise.
14 “Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
Those of the house of Togarmah traded for thy wares with horses and war-horses and mules.
15 “Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
The men of Dedan were thy merchants. Many isles were the mart of thy hand. They brought thee in exchange horns of ivory and ebony.
16 “Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
Syria was thy merchant because of the multitude of thy handiworks. They traded for thy wares with emeralds, purple, and embroidered work, and fine linen, and coral, and rubies.
17 “Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
Judah, and the land of Israel, they were thy merchants. They traded for thy merchandise wheat of Minnith, and pannag, and honey, and oil, and balm.
18 “Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
Damascus was thy merchant for the multitude of thy handiworks, because of the multitude of all kinds of riches, with the wine of Helbon, and white wool.
19 Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
Vedan and Javan traded with yarn for thy wares. Bright iron, cassia, and calamus, were among thy merchandise.
20 “Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
Dedan was thy merchant in precious cloths for riding.
21 “Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
Arabia, and all the rulers of Kedar, they were the merchants of thy hand, in lambs, and rams, and goats. In these they were thy merchants.
22 “Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
The merchants of Sheba and Raamah, they were thy merchants. They traded for thy wares with the chief of all spices, and with all precious stones, and gold.
23 “Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
Haran and Canneh and Eden, the merchants of Sheba, Asshur and Chilmad, were thy merchants.
24 Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
These were thy merchants in choice wares, in wrappings of blue and embroidered work, and in chests of rich apparel, bound with cords and made of cedar, among thy merchandise.
25 “Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali zonyamula malonda ako. Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi yodzaza ndi katundu wolemera.
The ships of Tarshish were thy caravans for thy merchandise. And thou were replenished, and made very glorious in the heart of the seas.
26 Anthu opalasa ako amakupititsa pa nyanja yozama. Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola pakati pa nyanja.
Thy rowers have brought thee into great waters. The east wind has broken thee in the heart of the seas.
27 Chuma chako, katundu wako, malonda ako, okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi, anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo adzamira mʼnyanja tsiku limene udzawonongeka.
Thy riches, and thy wares, thy merchandise, thy mariners, and thy pilots, thy caulkers, and the dealers in thy merchandise, and all thy men of war, who are in thee, with all thy company which is in the midst of thee, shall fall into the heart of the seas in the day of thy ruin.
28 Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
At the sound of the cry of thy pilots the suburbs shall shake.
29 Onse amene amapalasa sitima zapamadzi, adzatuluka mʼsitima zawo; oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
And all who handled the oar, the mariners, and all the pilots of the sea, shall come down from their ships. They shall stand upon the land,
30 Iwo akufuwula, kukulira iwe kwambiri; akudzithira fumbi kumutu, ndi kudzigubuduza pa phulusa.
and shall cause their voice to be heard over thee, and shall cry bitterly, and shall cast up dust upon their heads. They shall wallow themselves in the ashes.
31 Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe ndipo akuvala ziguduli. Akukulira iweyo ndi mitima yowawa kwambiri.
And they shall make themselves bald for thee, and gird with sackcloth, and they shall weep for thee in bitterness of soul with bitter mourning.
32 Akuyimba nyimbo yokudandaulira nʼkumati: ‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo pakati pa nyanja?’
And in their wailing they shall take up a lamentation for thee, and lament over thee, saying, Who is there like Tyre, like her that is brought to silence in the midst of the sea?
33 Pamene malonda ako ankawoloka nyanja unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu. Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako komanso ndi malonda ako.
When thy wares went forth out of the seas, thou filled many peoples. Thou enriched the kings of the earth with the multitude of thy riches and of thy merchandise.
34 Koma tsopano wathyokera mʼnyanja, pansi penipeni pa nyanja. Katundu wako ndi onse amene anali nawe amira pamodzi nawe.
In the time that thou were broken by the seas in the depths of the waters, thy merchandise and all thy company fell in the midst of thee.
35 Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja aopsedwa ndi zimene zakuchitikira. Mafumu awo akuchita mantha ndipo nkhope zangoti khululu.
All the inhabitants of the isles are astonished at thee, and their kings are horribly afraid; they are troubled in their countenance.
36 Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola. Watha mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”
The merchants among the peoples hiss at thee. Thou have become a horror, and thou shall nevermore have any being.

< Ezekieli 27 >