< Ezekieli 24 >

1 Pa tsiku lakhumi la mwezi wakhumi chaka chachisanu ndi chinayi, Yehova anandiyankhula kuti:
Again, in the ninth year, in the tenth month, in the tenth day of the month, the word of Jehovah came to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu lemba dzina la tsiku lalero, lero lomwe lino, chifukwa mfumu ya Babuloni yazungulira Yerusalemu lero lino.
Son of man, write thee the name of the day, even of this selfsame day; the king of Babylon drew close to Jerusalem this selfsame day.
3 Uwaphere mwambi anthu owukirawa ndi kuwawuza kuti: ‘Ambuye Yehova akuti, “‘Ikani mʼphika pa moto, ndipo mu mʼphikamo muthiremo madzi.
And utter a parable to the rebellious house, and say to them, Thus says the lord Jehovah: Set on the caldron. Set it on, and also pour water into it.
4 Mu mʼphikamo muyikemo nthuli za nyama, nthuli zonse zabwino kwambiri za mwendo wathako ndi mwendo wamwamba. Mudzadzemo mafupa abwino kwambiri.
Gather the pieces of it into it, even every good piece, the thigh, and the shoulder; fill it with the choice bones.
5 Pa gulu la nkhosa musankhepo nkhosa yabwino kwambiri. Muyike nkhuni pansi pa mʼphikawo. Madzi awire. Kenaka muphike nyamayo pamodzi ndi mafupa omwe.’
Take the choice of the flock, and also a pile of wood for the bones under the caldron. Make it boil well, yea, let the bones of it be boiled in the midst of it.
6 “‘Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova akuti, “‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi, tsoka kwa mʼphika wadzimbiri; dzimbiri lake losachoka! Mutulutsemo nthuli imodzimodzi osasankhulapo.
Therefore thus says the lord Jehovah: Woe to the bloody city, to the caldron whose rust is therein, and whose rust has not gone out of it! Take out of it piece after piece. No lot has fallen upon it.
7 “‘Paja magazi amene anakhetsa akanali pakati pake mu mzindamo. Iye awakhuthulira pa thanthwe losalala. Sanawakhutulire pa dothi kuopa kuti fumbi lingawafotsere.
For her blood is in the midst of her. She set it upon the bare rock. She did not pour it upon the ground to cover it with dust.
8 Ndinasiya magaziwo pa mwala wosalala kuti asafotseredwe ndi fumbi chifukwa ndinafuna kuonetsa mkwiyo wanga ndi kulipsira.
That it may cause wrath to come up to take vengeance, I have set her blood upon the bare rock, that it should not be covered.
9 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Tsoka kwa mzinda wokhetsa magazi! Inenso, ndidzawunjika mulu waukulu wa nkhuni.
Therefore thus says the lord Jehovah: Woe to the bloody city! I also will make the pile great.
10 Choncho wonjeza nkhuni ndipo muyatse moto. Phikani nyamayo bwinobwino, muthiremo zokometsera, mutsanule msuzi, ndipo mupsereze mafupawo.
Heap on the wood; make the fire hot. Boil the flesh well, and make the broth thick. And let the bones be burned.
11 Tsono muyike pa makala mʼphika wopanda kanthuwo mpaka utenthe kuchita kuti psuu kuti zonyansa zake zisungunuke ndi kuti dzimbiri lake lichoke.
Then set it empty upon the coals of it, that it may be hot, and the brass of it may burn, and that the filthiness of it may be molten in it, that the scum of it may be consumed.
12 Koma mʼphikawo walephereka kuyeretsedwa. Dzimbiri lake linalowerera silingatheke kuchoka ngakhale ndi moto womwe.
She has wearied herself with toil, yet her great scum does not go forth out of her, her scum by fire.
13 “‘Tsono dzimbiri limeneli ndi zilakolako za dama lako. Pakuti ine ndinayesa kukutsuka koma iwe sunayere, ndipo sudzayeranso mpaka ukali wanga utakwaniratu pa iwe.
In thy filthiness is lewdness. Because I have cleansed thee and thou were not cleansed, thou shall not be cleansed from thy filthiness any more, till I have caused my wrath toward thee to rest.
14 “‘Ine Yehova ndayankhula. Zimenezi zikubwera ndipo ndidzazichitadi. Sindidzabwerera mʼmbuyo. Sindidzakulekerera kapena kukuchitira chifundo. Ndidzakulanga molingana ndi makhalidwe ndi machitidwe ako, akutero Ambuye Yehova.’”
I, Jehovah, have spoken it. It shall come to pass, and I will do it. I will not go back. I will neither spare, nor will I relent. According to thy ways, and according to thy doings, they shall judge thee, says the lord Jehovah.
15 Yehova anandiyankhula kuti:
Also the word of Jehovah came to me, saying,
16 “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikulanda mwadzidzidzi mkazi amene amakukomera mʼmaso kwambiri. Koma usadandaule, usalire kapena kukhetsa misozi.
Son of man, behold, I take the desire of thine eyes away from thee with a stroke. Yet thou shall neither mourn nor weep. Neither shall thy tears run down.
17 Ubuwule koma mwakachetechete. Usamulire wakufayo. Uvale nduwira yako ndithu, nsapato zakonso usavule. Usaphimbe nkhope kapena kudya chakudya cha anamfedwa.”
Sigh, but not aloud. Make no mourning for the dead. Bind thy headdress upon thee, and put thy shoes upon thy feet. And do not cover thy lips, and do not eat the bread of men.
18 Choncho ndinayankhula ndi anthu mmawa, ndipo madzulo mkazi wanga anamwalira. Mmawa mwake ndinachita monga momwe anandilamulira.
So I spoke to the people in the morning, and at evening my wife died. And I did in the morning as I was commanded.
19 Ndipo anthu anandifunsa kuti, “Kodi sutifotokozera tanthauzo la zimene ukuchitazi?”
And the people said to me, Will thou not tell us what these things are to us, that thou do so?
20 Ndinawayankha kuti, “Yehova anandipatsa uthenga wakuti,
Then I said to them, The word of Jehovah came to me, saying,
21 ‘Awuze Aisraeli kuti: Ine Ambuye Yehova ndikuti: ndidzayipitsa Nyumba yanga yopatulika, nyumba imene mwakhala mukuyinyadira. Mumakondwa kwambiri poyiona, ndipo mumayikonda ndi mtima onse. Ana aamuna ndi aakazi amene munawasiya mʼmbuyo adzaphedwa ndi lupanga.
Speak to the house of Israel, Thus says the lord Jehovah: Behold, I will profane my sanctuary, the pride of your power, the desire of your eyes, and that which your soul has compassion. And your sons and your daughters whom ye have left behind shall fall by the sword.
22 Ndipo mudzachita monga ndachitira inemu. Inu simudzaphimba nkhope zanu kapena kudya chakudya cha anamfedwa.
And ye shall do as I have done. Ye shall not cover your lips, nor eat the bread of men.
23 Mudzavala nduwira zanu kumutu ndi nsapato zanu ku mapazi anu. Simudzabuma maliro kapena kukhetsa misozi koma mudzavutika kwambiri chifukwa cha machimo anu ndipo mudzabuwula pakati panu.
And your coverings shall be upon your heads, and your shoes upon your feet. Ye shall not mourn nor weep, but ye shall pine away in your iniquities, and moan one toward another.
24 Ine Ezekieli ndidzakhala chitsanzo chanu. Mudzachita monga momwe ndachitira. Izi zikadzachitika, akutero Yehova, ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Wamphamvuzonse.’
Thus Ezekiel shall be to you a sign, according to all that he has done ye shall do. When this comes, then ye shall know that I am the lord Jehovah.
25 “Ndipo Yehova anandiyankhula nati: Iwe mwana wa munthu, tsiku lina ndidzawachotsera anthuwa linga lawo limene ankakondwerera kukongola kwake, limene linkawakomera mʼmaso mwawo, limenenso anayikapo mtima wawo kwambiri. Ndidzawachotsera ana awo aamuna ndi aakazi.
And thou, son of man, shall it not be in the day when I take from them their strength, the joy of their glory, the desire of their eyes, and that upon which they set their heart-their sons and their daughters-
26 Pa tsiku limenelo wothawa nkhondo adzabwera kudzakuwuzani zimenezo.
that in that day he who escapes shall come to thee, to cause thee to hear it with thine ears?
27 Pa tsiku limenelo pakamwa pako padzatsekuka. Udzatha kuyankhula naye ndipo sudzakhalanso chete. Motero udzakhala chizindikiro kwa iwo, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
In that day thy mouth shall be opened to him who is escaped, and thou shall speak, and no more be mute. So thou shall be a sign to them, and they shall know that I am Jehovah.

< Ezekieli 24 >