< Ezekieli 21 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
And the word of Jehovah came to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane ku Yerusalemu ndipo ulalike mawu odzudzula malo ake opatulika. Unenere zodzudzula anthu a ku Yerusalemu.
Son of man, set thy face toward Jerusalem, and drop thy word toward the sanctuaries, and prophesy against the land of Israel.
3 Uwawuze kuti, Ambuye Yehova akuti, ‘Taona, Ine ndidzalimbana nawe. Ndidzasolola lupanga langa mʼchimake ndi kuwononga anthu olungama ndi ochimwa omwe.
And say to the land of Israel, Thus says Jehovah: Behold, I am against thee. And will draw forth my sword out of its sheath, and will cut off from thee the righteous and the wicked.
4 Motero ndidzapha aliyense kuchokera kummawa mpaka kumpoto.
Seeing then that I will cut off from thee the righteous and the wicked, therefore my sword shall go forth out of its sheath against all flesh from the south to the north.
5 Pamenepo anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndasolola lupanga langa mʼchimake; sindidzalilowetsanso mʼchimakemo.’
And all flesh shall know that I, Jehovah, have drawn forth my sword out of its sheath. It shall not return any more.
6 “Tsono iwe mwana wa munthu, buwula. Buwula pamaso pawo ndi mtima wosweka ndi wachisoni chachikulu.
Sigh therefore, thou son of man. With the breaking of thy loins and with bitterness thou shall sigh before their eyes.
7 Ndipo akadzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ukubuwula?’ Iwe udzayankhe kuti, ‘Ndikubuwula chifukwa cha nkhani imene ndamva. Zikadzachitika zimenezi, mitima yonse idzangoti fumu, manja onse adzangolefuka, mpweya wawo udzawathera, ndipo mawondo onse adzangoti zii.’ Izi zikubwera! Ndipo zidzachitika ndithu, akutero Ambuye Yehova.”
And it shall be, when they say to thee, Why do thou sigh? That thou shall say, Because of the news. For it comes, and every heart shall melt, and all hands shall be feeble, and every spirit shall faint, and all knees shall be weak as water. Behold, it comes, and it shall be done, says the lord Jehovah.
8 Yehova anandiyankhulanso kuti,
And the word of Jehovah came to me, saying,
9 “Iwe mwana wa munthu, unenere ndipo unene kuti, Ambuye Yehova akuti, “Izi ndi zimene Yehova akunena: Lupanga, lupanga, lanoledwa ndipo lapukutidwa.
Son of man, prophesy, and say, Thus says Jehovah: Say, A sword, a sword. It is sharpened, and also furbished.
10 Lanoledwa kuti likaphe, lapukutidwa kuti lingʼanime ngati mphenzi! “‘Kodi tingakondwere bwanji? Wanyoza ndodo, mwana wanga ndi chilichonse cha mtengo.
It is sharpened that it may make a slaughter. It is polished that it may be as lightning. Shall we then make mirth? It scorns the scepter of my son, every tree.
11 “‘Lupanga laperekedwa kuti lipukutidwe, ndi kuti linyamulidwe, lanoledwa ndi kupukutidwa, kuti liperekedwe mʼmanja mwa munthu amene amapha.
And it is given to be polished, that it may be handled. The sword, it is sharpened, yea, it is polished, to give it into the hand of the slayer.
12 Fuwula ndi kulira, iwe mwana wa munthu, pakuti zimenezi zidzagwera anthu anga; zidzagweranso akalonga onse a Israeli. Adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi anthu anga. Chifukwa chake udzigugude pa chifuwa ndi chisoni.
Cry and wail, son of man, for it is upon my people. It is upon all the rulers of Israel. They are delivered over to the sword with my people. Smite therefore upon thy thigh.
13 “‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Ndikuwayesa anthu anga, ndipo ngati satembenuka mtima, ndiye kuti zimenezi sizidzalephera kuwagwera.’
For there is a trial, and what if even the rod that scorns shall be no more? says the lord Jehovah.
14 “Tsono mwana wa munthu, nenera ndipo uwombe mʼmanja. Lupanga likanthe kawiri ngakhale katatu. Limenelo ndilo lupanga lophera anthu. Inde ndilodi lupanga lophera anthu koopsa limene likuwazungulira.
Thou therefore, son of man, prophesy, and smite thy hands together. And let the sword be doubled the third time, the sword of the deadly wounded. It is the sword of the great man who is deadly wounded, which enters into their chambers.
15 Ndawayikira pa zipata zawo zonse lupanga laphuliphuli kuti ataye mtima ndiponso kuti anthu ambiri agwe. Aa! Lapangidwa lupanga kuti lizingʼanima ngati mphenzi ndi kuti azilisolola kuphera anthu.
I have set the threatening sword against all their gates, that their heart may melt, and their stumblings be multiplied. Ah! It is made as lightning. It is pointed for slaughter.
16 Iwe lupanga, ipha anthu kumanja, kenaka kumanzere, kulikonse kumene msonga yako yaloza.
Gather thee together. Go to the right. Set thyself in array. Go to the left, wherever thy face is set.
17 Inenso ndidzawomba mʼmanja mwanga, ndipo ndidzaziziritsa ukali wanga Ine Yehova ndayankhula.”
I will also smite my hands together, and I will cause my wrath to rest. I, Jehovah, have spoken it.
18 Yehova anandiyankhulanso kuti,
The word of Jehovah came to me again, saying,
19 “Iwe mwana wa munthu, ulembe zizindikiro za misewu iwiri imene lupanga la mfumu ya ku Babuloni lingathe kudzeramo. Misewu yonse ikhale yochokera mʼdziko limodzi. Ika chikwangwani pa mphambano yopita mu mzinda.
Also, thou son of man, appoint thee two ways that the sword of the king of Babylon may come. Those two shall come forth out of one land. And mark out a place. Mark it out at the head of the way to the city.
20 Ulembe chizindikiro pa msewu umene lupanga lidzadzere popita ku Raba wa ku Amoni, ndiponso ku Yuda ndi ku Yerusalemu, mzinda wotetezedwa.
Thou shall appoint a way for the sword to come to Rabbah of the sons of Ammon, and to Judah in Jerusalem the fortified.
21 Pakuti mfumu ya ku Babuloni yayima pa msewu, pa mphambano ya misewu iwiriyo. Ikuwombeza ndi mivi yake kuti idziwe njira yoyenera kudzeramo. Ikupempha nzeru kwa milungu yake ndipo ikuyangʼana chiwindi cha nyama yoperekedwa ku nsembe.
For the king of Babylon stood at the parting of the way, at the head of the two ways, to use divination. He shook the arrows to and fro. He consulted the teraphim. He looked in the liver.
22 Mʼdzanja lake lamanja muli muvi waula wolembedwa Yerusalemu. Kumeneko mfumuyo idzayika zida zogumulira, idzalamula kupha anthu ndiponso kufuwula mfuwu wa nkhondo. Mfumuyo idzapanga zida zogumulira makoma, kuwunda mitumbira ya nkhondo ndi kumanga nsanja za nkhondo.
In his right hand was the divination for Jerusalem, to set battering rams, to open the mouth in the slaughter, to lift up the voice with shouting, to set battering rams against the gates, to cast up mounds, to build forts.
23 Koma kwa anthu a ku Yerusalemu zidzaoneka ngati zowombeza zabodza chifukwa cha malumbiro amene anachita kwa mfumuyo. Koma mfumuyo idzawakumbutsa za zolakwa zawo kuti atengedwe ku ukapolo.
And it shall be to them as a false divination in their sight, who have sworn oaths to them. But he brings iniquity to remembrance, that they may be taken.
24 “Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Popeza mwandikumbutsa zolakwa, moti kundiwukira kwanu kwaonekera poyera ndi kuti mu zochita zanu zonse mukuonetsa machimo anu, nʼchifukwa chake mudzagwidwa ndi kutengedwa ukapolo.
Therefore thus says the lord Jehovah: Because ye have made your iniquity to be remembered, in that your transgressions are uncovered, so that in all your doings your sins do appear, because ye have come to remembrance, ye shall be taken with the hand.
25 “‘Tsono iwe kalonga wonyozedwa ndi woyipa wa Israeli, amene tsiku lako lafika, amene nthawi yako yolangidwa yafika penipeni,
And thou, O deadly wounded wicked man, the ruler of Israel, whose day has come, in the time of the iniquity of the end,
26 Ambuye Yehova akuti: Vula nduwira, chotsa chipewa chaufumu. Zinthu sizidzakhala monga zinalili: anthu wamba adzakwezedwa ndipo okwezedwa adzatsitsidwa.
thus says the lord Jehovah: Remove the miter, and take off the crown. This shall be no more the same. Exalt that which is low, and abase that which is high.
27 Chipasupasu! Chipasupasu! Ine ndidzawupasula mzindawo! Ndipo sadzawumanganso mpaka atafika amene ali woyenera kuwulandira; Ine ndidzawupereka kwa iyeyo.’
I will overturn, overturn, overturn it. This also shall be no more, until he comes whose right it is. And I will give it.
28 “Ndipo iwe mwana wa munthu, nenera kuti, ponena za Aamoni ndi zonyoza zawo, Ambuye Yehova akuti, “‘Lupanga, lupanga, alisolola kuti liphe anthu, alipukuta kuti liwononge ndi kuti lingʼanime ngati mphenzi.
And thou, son of man, prophesy, and say, Thus says the lord Jehovah concerning the sons of Ammon, and concerning their reproach. And say thou, A sword, a sword is drawn. It is polished for the slaughter, to cause it to devour, that it may be as lightning,
29 Zimene akuti akuona mʼmasomphenya zokhudza inu ndi zabodza. Mawula awo okhudza inu ndi abodzanso. Mudzakhala pamodzi ndi anthu oyipa amene tsiku lawo lafika, ndiye kuti nthawi ya kulangidwa kwawo komaliza.
while they see for thee false visions, while they divine lies to thee, to lay thee upon the necks of the wicked who are deadly wounded, whose day has come in the time of the iniquity of the end.
30 “‘Bwezerani lupanga mʼchimake. Ku malo kumene inu munabadwira, mʼdziko la makolo anu, ndidzakuweruzani.
Cause it to return into its sheath. In the place where thou were created, in the land of thy birth, I will judge thee.
31 Ndidzakhuthula ukali wanga pa inu, ndipo mkwiyo wanga udzakuyakirani. Ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu ankhanza; anthu odziwa bwino kuwononga zinthu.
And I will pour out my indignation upon thee. I will blow upon thee with the fire of my wrath, and I will deliver thee into the hand of brutish men, skilful to destroy.
32 Mudzakhala ngati nkhuni pa moto. Ena adzakhetsa magazi anu mʼdziko lanu lomwe. Simudzakumbukiridwanso pakuti Ine Yehova ndayankhula.’”
Thou shall be for fuel to the fire. Thy blood shall be in the midst of the land. Thou shall no more be remembered. For I, Jehovah, have spoken it.

< Ezekieli 21 >