< Ezekieli 19 >

1 “Imba nyimbo ya madandawulo, kuyimbira akalonga a ku Israeli.
Moreover, take thou up a lamentation for the rulers of Israel,
2 Uzinena kuti, “‘Amayi ako anali ndani? Anali ngati mkango waukazi! Iwo unabwatama pakati pa mikango yayimuna; unkalera ana ake pakati pa misona.
and say, What was thy mother? A lioness. She couched among lions. In the midst of the young lions she nourished her whelps.
3 Unalera mmodzi mwa ana ake, ndipo mwanayo anasanduka mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama, ndipo unayamba kudya anthu.
And she brought up one of her whelps. He became a young lion, and he learned to catch the prey. He devoured men.
4 Anthu amitundu anamva za mkangowo, ndipo tsiku lina unagwa mʼmbuna mwawo. Iwo anawukoka ndi ngowe kupita nawo ku dziko la Igupto.
The nations also heard of him. He was taken in their pit, and they brought him with hooks to the land of Egypt.
5 “‘Amayi aja ataona kuti mwana ankamukhulupirira uja wagwidwa ndi kuti chiyembekezo chake chapita padera, amayiwo anatenganso mwana wina namusandutsa mkango wamphamvu.
Now when she saw that she had waited, and her hope was lost, then she took another of her whelps, and made him a young lion.
6 Unkayendayenda pakati pa mikango inzake, pakuti tsopano unali mkango wamphamvu. Unaphunzira kugwira nyama ndipo unayamba kudya anthu.
And he went up and down among the lions. He became a young lion, and he learned to catch the prey. He devoured men.
7 Unagwetsa malinga awo, ndikuwononga mizinda yawo. Onse a mʼdzikomo anachita mantha chifukwa cha kubangula kwake.
And he knew their palaces, and laid waste their cities. And the land was desolate, and the fullness of it, because of the noise of his roaring.
8 Pamenepo mitundu ya anthu, makamaka ochokera madera ozungulira, inabwera kudzalimbana nawo. Anawutchera ukonde wawo, ndipo tsiku lina unagwera mʼmbuna mwawo.
Then the nations set against him on every side from the provinces, and they spread their net over him. He was taken in their pit.
9 Anawukoka ndi ngowe nawuponya mʼchitatanga. Anabwera nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ndipo mfumuyo inawuponya mʼndende ndi cholinga choti liwu lake lisamamvekenso ku mapiri a Israeli.
And they put him in a cage with hooks, and brought him to the king of Babylon. They brought him into strongholds, that his voice should no more be heard upon the mountains of Israel.
10 “‘Amayi ako anali ngati mpesa mʼmunda wamphesa wodzalidwa mʼmbali mwa madzi. Unabereka bwino ndipo unali ndi nthambi zambiri chifukwa cha kuchuluka kwa madzi.
Thy mother was like a vine in thy blood, planted by the waters. It was fruitful and full of branches because of many waters.
11 Nthambi zake zinali zolimba, zoyenera kupangira ndodo yaufumu. Unatalika nusomphoka pakati pa zomera zina. Unkaoneka bwino chifukwa cha kutalika kwake, ndi nthambi zake zambiri.
And it had strong twigs for the scepters of those who bore rule. And their stature was exalted among the thick boughs, and they were seen in their height with the multitude of their branches.
12 Koma unazulidwa mwaukali ndipo unagwetsedwa pansi. Unawuma ndi mphepo ya kummawa, zipatso zake zinayoyoka; nthambi zake zolimba zinafota ndipo moto unapsereza mtengo wonse.
But it was plucked up in fury. It was cast down to the ground, and the east wind dried up its fruit. Its strong twigs were broken off and withered. The fire consumed them.
13 Ndipo tsopano anawuwokeranso ku chipululu, dziko lowuma ndi lopanda madzi.
And now it is planted in the wilderness, in a dry and thirsty land.
14 Moto unatulukanso mu mtengomo ndi kupsereza nthambi ndi zipatso zake. Palibe nthambi yolimba inatsala pa mtengowo yoyenera kupangira ndodo yaufumu. Imeneyi ndi nyimbo yachisoni ndipo yasanduka nyimbo ya pa maliro.’”
And fire has gone out of the twigs of its branches. It has devoured its fruit, so that there is no strong twig in it to be a scepter to rule. This is a lamentation, and shall be for a lamentation.

< Ezekieli 19 >